< Proverbi 21 >

1 Il cuore del re, nella mano dell’Eterno, è come un corso d’acqua; egli lo volge dovunque gli piace.
Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
2 Tutte le vie dell’uomo gli paion diritte, ma l’Eterno pesa i cuori.
Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
3 Praticare la giustizia e l’equità è cosa che l’Eterno preferisce ai sacrifizi.
Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
4 Gli occhi alteri e il cuor gonfio, lucerna degli empi, sono peccato.
Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
5 I disegni dell’uomo diligente menano sicuramente all’abbondanza, ma chi troppo s’affretta non fa che cader nella miseria.
Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
6 I tesori acquistati con lingua bugiarda sono un soffio fugace di gente che cerca la morte.
Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
7 La violenza degli empi li porta via, perché rifiutano di praticare l’equità.
Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
8 La via del colpevole è tortuosa, ma l’innocente opera con rettitudine.
Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
9 Meglio abitare sul canto d’un tetto, che una gran casa con una moglie rissosa.
Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
10 L’anima dell’empio desidera il male; il suo amico stesso non trova pietà agli occhi di lui.
Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
11 Quando il beffardo è punito, il semplice diventa savio; e quando s’istruisce il savio, egli acquista scienza.
Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
12 Il Giusto tien d’occhio la casa dell’empio, e precipita gli empi nelle sciagure.
Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
13 Chi chiude l’orecchio al grido del povero, griderà anch’egli, e non gli sarà risposto.
Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
14 Un dono fatto in segreto placa la collera, e un regalo dato di sottomano, l’ira violenta.
Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
15 Far ciò ch’è retto è una gioia per il giusto, ma è una rovina per gli artefici d’iniquità.
Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
16 L’uomo che erra lungi dalle vie del buon senso, riposerà nell’assemblea dei trapassati.
Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
17 Chi ama godere sarà bisognoso, chi ama il vino e l’olio non arricchirà.
Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
18 L’empio serve di riscatto al giusto; e il perfido, agli uomini retti.
Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
19 Meglio abitare in un deserto, che con una donna rissosa e stizzosa.
Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
20 In casa del savio c’è dei tesori preziosi e dell’olio, ma l’uomo stolto dà fondo a tutto.
Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
21 Chi ricerca la giustizia e la bontà troverà vita, giustizia e gloria.
Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
22 Il savio dà la scalata alla città dei forti, e abbatte il baluardo in cui essa confidava.
Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
23 Chi custodisce la sua bocca e la sua lingua preserva l’anima sua dalle distrette.
Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
24 Il nome del superbo insolente è: beffardo; egli fa ogni cosa con furore di superbia.
Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
25 I desideri del pigro l’uccidono perché le sue mani rifiutano di lavorare.
Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
26 C’è chi da mane a sera brama avidamente, ma il giusto dona senza mai rifiutare.
Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
27 Il sacrifizio dell’empio è cosa abominevole; quanto più se l’offre con intento malvagio!
Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
28 Il testimonio bugiardo perirà, ma l’uomo che ascolta potrà sempre parlare.
Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
29 L’empio fa la faccia tosta, ma l’uomo retto rende ferma la sua condotta.
Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
30 Non c’è sapienza, non intelligenza, non consiglio che valga contro l’Eterno.
Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
31 Il cavallo è pronto per il dì della battaglia, ma la vittoria appartiene all’Eterno.
Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.

< Proverbi 21 >