< Proverbi 20 >

1 Il vino è schernitore, la bevanda alcoolica è turbolenta, e chiunque se ne lascia sopraffare non è savio.
Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola; aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.
2 Il terrore che incute il re è come il ruggito d’un leone; chi lo irrita pecca contro la propria vita.
Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango; amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.
3 E’ una gloria per l’uomo l’astenersi dalle contese, ma chiunque è insensato mostra i denti.
Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano, koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.
4 Il pigro non ara a causa del freddo; alla raccolta verrà a cercare, ma non ci sarà nulla.
Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera; kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.
5 I disegni nel cuor dell’uomo sono acque profonde, ma l’uomo intelligente saprà attingervi.
Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya, munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.
6 Molta gente vanta la propria bontà; ma un uomo fedele chi lo troverà?
Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo, koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?
7 I figliuoli del giusto, che cammina nella sua integrità, saranno beati dopo di lui.
Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino; odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.
8 Il re, assiso sul trono dove rende giustizia, dissipa col suo sguardo ogni male.
Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo, imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.
9 Chi può dire: “Ho nettato il mio cuore, sono puro dal mio peccato?”
Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga; ndilibe tchimo lililonse?”
10 Doppio peso e doppia misura sono ambedue in abominio all’Eterno.
Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa.
11 Anche il fanciullo dà a conoscere con i suoi atti se la sua condotta sarà pura e retta.
Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake, ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.
12 L’orecchio che ascolta e l’occhio che vede, li ha fatti ambedue l’Eterno.
Makutu amene amamva ndi maso amene amaona, zonsezi anazilenga ndi Yehova.
13 Non amare il sonno, che tu non abbia a impoverire; tieni aperti gli occhi, e avrai pane da saziarti.
Usakonde tulo ungasauke; khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.
14 “Cattivo! cattivo!” dice il compratore; ma, andandosene, si vanta dell’acquisto.
Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.” Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.
15 C’è dell’oro e abbondanza di perle, ma le labbra ricche di scienza son cosa più preziosa.
Pali golide ndi miyala yamtengowapatali, koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.
16 Prendigli il vestito, giacché ha fatta cauzione per altri; fatti dare dei pegni, poiché s’è reso garante di stranieri.
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.
17 Il pane frodato è dolce all’uomo; ma, dopo, avrà la bocca piena di ghiaia.
Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu, koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.
18 I disegni son resi stabili dal consiglio; fa’ dunque la guerra con una savia direzione.
Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu; ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.
19 Chi va sparlando palesa i segreti; perciò non t’immischiare con chi apre troppo le labbra.
Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi. Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.
20 Chi maledice suo padre e sua madre, la sua lucerna si spegnerà nelle tenebre più fitte.
Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake, moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.
21 L’eredità acquistata troppo presto da principio, alla fine non sarà benedetta.
Cholowa chochipeza mofulumira poyamba, sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.
22 Non dire: “Renderò il male”; spera nell’Eterno, ed egli ti salverà.
Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!” Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.
23 Il peso doppio è in abominio all’Eterno, e la bilancia falsa non è cosa buona.
Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino.
24 I passi dell’uomo li dirige l’Eterno; come può quindi l’uomo capir la propria via?
Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova, tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?
25 E’ pericoloso per l’uomo prender leggermente un impegno sacro, e non riflettere che dopo aver fatto un voto.
Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,” popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.
26 Il re savio passa gli empi al vaglio, dopo aver fatto passare la ruota su loro.
Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu anthu oyipa.
27 Lo spirito dell’uomo è una lucerna dell’Eterno che scruta tutti i recessi del cuore.
Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova; imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.
28 La bontà e la fedeltà custodiscono il re; e con la bontà egli rende stabile il suo trono.
Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu; chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.
29 La gloria dei giovani sta nella loro forza, e la bellezza dei vecchi, nella loro canizie.
Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo, imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.
30 Le battiture che piagano guariscono il male; e così le percosse che vanno al fondo delle viscere.
Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa, ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.

< Proverbi 20 >