< Proverbi 16 >

1 All’uomo, i disegni del cuore; ma la risposta della lingua vien dall’Eterno.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 Tutte le vie dell’uomo a lui sembran pure, ma l’Eterno pesa gli spiriti.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Rimetti le cose tue nell’Eterno, e i tuoi disegni avran buona riuscita.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 L’Eterno ha fatto ogni cosa per uno scopo; anche l’empio, per il dì della sventura.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 Chi è altero d’animo è in abominio all’Eterno; certo è che non rimarrà impunito.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 Con la bontà e con la fedeltà l’iniquità si espia, e col timor dell’Eterno si evita il male.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 Quando l’Eterno gradisce le vie d’un uomo, riconcilia con lui anche i nemici.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Meglio poco con giustizia, che grandi entrate senza equità.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 Il cuor dell’uomo medita la sua via, ma l’Eterno dirige i suoi passi.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 Sulle labbra del re sta una sentenza divina; quando pronunzia il giudizio la sua bocca non erra.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 La stadera e le bilance giuste appartengono all’Eterno, tutti i pesi del sacchetto son opera sua.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 I re hanno orrore di fare il male, perché il trono è reso stabile con la giustizia.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Le labbra giuste sono gradite ai re; essi amano chi parla rettamente.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 Ira del re vuol dire messaggeri di morte, ma l’uomo savio la placherà.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 La serenità del volto del re dà la vita, e il suo favore è come nube di pioggia primaverile.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 L’acquisto della sapienza oh quanto è migliore di quello dell’oro, e l’acquisto dell’intelligenza preferibile a quel dell’argento!
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 La strada maestra dell’uomo retto è evitare il male; chi bada alla sua via preserva l’anima sua.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 La superbia precede la rovina, e l’alterezza dello spirito precede la caduta.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 Meglio esser umile di spirito coi miseri, che spartir la preda coi superbi.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 Chi presta attenzione alla Parola se ne troverà bene, e beato colui che confida nell’Eterno!
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 Il savio di cuore è chiamato intelligente, e la dolcezza delle labbra aumenta il sapere.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 Il senno, per chi lo possiede, è fonte di vita, ma la stoltezza è il castigo degli stolti.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 Il cuore del savio gli rende assennata la bocca, e aumenta il sapere sulle sue labbra.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Le parole soavi sono un favo di miele: dolcezza all’anima, salute al corpo.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 V’è tal via che all’uomo par diritta, ma finisce col menare alla morte.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 La fame del lavoratore lavora per lui, perché la sua bocca lo stimola.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 L’uomo cattivo va scavando ad altri del male, sulle sue labbra c’è come un fuoco divorante.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 L’uomo perverso semina contese, e il maldicente disunisce gli amici migliori.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 L’uomo violento trascina il compagno, e lo mena per una via non buona.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 Chi chiude gli occhi per macchinar cose perverse, chi si morde le labbra, ha già compiuto il male.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 I capelli bianchi sono una corona d’onore; la si trova sulla via della giustizia.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 Chi è lento all’ira val più del prode guerriero; chi padroneggia sé stesso val più di chi espugna città.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 Si gettan le sorti nel grembo, ma ogni decisione vien dall’Eterno.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

< Proverbi 16 >