< Proverbi 15 >

1 La risposta dolce calma il furore, ma la parola dura eccita l’ira.
Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
2 La lingua dei savi è ricca di scienza, ma la bocca degli stolti sgorga follia.
Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
3 Gli occhi dell’Eterno sono in ogni luogo, osservando i cattivi ed i buoni.
Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
4 La lingua che calma, è un albero di vita, ma la lingua perversa strazia lo spirito.
Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
5 L’insensato disdegna l’istruzione di suo padre, ma chi tien conto della riprensione diviene accorto.
Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
6 Nella casa del giusto v’è grande abbondanza, ma nell’entrate dell’empio c’è turbolenza.
Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
7 Le labbra dei savi spargono scienza, ma non così il cuore degli stolti.
Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
8 Il sacrifizio degli empi è in abominio all’Eterno, ma la preghiera degli uomini retti gli è grata.
Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
9 La via dell’empio è in abominio all’Eterno, ma egli ama chi segue la giustizia.
Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
10 Una dura correzione aspetta chi lascia la diritta via; chi odia la riprensione morrà.
Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
11 Il soggiorno de’ morti e l’abisso stanno dinanzi all’Eterno; quanto più i cuori de’ figliuoli degli uomini! (Sheol h7585)
Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol h7585)
12 Il beffardo non ama che altri lo riprenda; egli non va dai savi.
Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
13 Il cuore allegro rende ilare il volto, ma quando il cuore è triste, lo spirito è abbattuto.
Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
14 Il cuor dell’uomo intelligente cerca la scienza, ma la bocca degli stolti si pasce di follia.
Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
15 Tutt’i giorni dell’afflitto sono cattivi, ma il cuor contento è un convito perenne.
Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
16 Meglio poco col timor dell’Eterno, che gran tesoro con turbolenza.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
17 Meglio un piatto d’erbe, dov’è l’amore, che un bove ingrassato, dov’è l’odio.
Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
18 L’uomo iracondo fa nascere contese, ma chi è lento all’ira acqueta le liti.
Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
19 La via del pigro è come una siepe di spine, ma il sentiero degli uomini retti è piano.
Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
20 Il figliuol savio rallegra il padre, ma l’uomo stolto disprezza sua madre.
Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
21 La follia è una gioia per chi è privo di senno, ma l’uomo prudente cammina retto per la sua via.
Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
22 I disegni falliscono, dove mancano i consigli; ma riescono, dove son molti i consiglieri.
Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
23 Uno prova allegrezza quando risponde bene; e com’è buona una parola detta a tempo!
Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
24 Per l’uomo sagace la via della vita mena in alto e gli fa evitare il soggiorno de’ morti, in basso. (Sheol h7585)
Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol h7585)
25 L’Eterno spianta la casa dei superbi, ma rende stabili i confini della vedova.
Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
26 I pensieri malvagi sono in abominio all’Eterno, ma le parole benevole son pure agli occhi suoi.
Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
27 Chi è avido di lucro conturba la sua casa, ma chi odia i regali vivrà.
Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
28 Il cuor del giusto medita la sua risposta, ma la bocca degli empi sgorga cose malvage.
Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
29 L’Eterno è lungi dagli empi, ma ascolta la preghiera dei giusti.
Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
30 Uno sguardo lucente rallegra il cuore; una buona notizia impingua l’ossa.
Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
31 L’orecchio attento alla riprensione che mena a vita, dimorerà fra i savi.
Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
32 Chi rigetta l’istruzione disprezza l’anima sua, ma chi dà retta alla riprensione acquista senno.
Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
33 Il timor dell’Eterno è scuola di sapienza; e l’umiltà precede la gloria.
Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.

< Proverbi 15 >