< Proverbi 13 >

1 Il figliuol savio ascolta l’istruzione di suo padre, ma il beffardo non ascolta rimproveri.
Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
2 Per il frutto delle sue labbra uno gode del bene, ma il desiderio dei perfidi è la violenza.
Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
3 Chi custodisce la sua bocca preserva la propria vita; chi apre troppo le labbra va incontro alla rovina.
Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
4 L’anima del pigro desidera, e non ha nulla, ma l’anima dei diligenti sarà soddisfatta appieno.
Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
5 Il giusto odia la menzogna, ma l’empio getta sugli altri vituperio ed onta.
Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
6 La giustizia protegge l’uomo che cammina nella integrità, ma l’empietà atterra il peccatore.
Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
7 C’è chi fa il ricco e non ha nulla; c’è chi fa il povero e ha di gran beni.
Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
8 La ricchezza d’un uomo serve come riscatto della sua vita, ma il povero non ode mai minacce.
Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
9 La luce dei giusti è gaia, ma la lampada degli empi si spegne.
Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
10 Dall’orgoglio non vien che contesa, ma la sapienza è con chi dà retta ai consigli.
Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
11 La ricchezza male acquistata va scemando, ma chi accumula a poco a poco l’aumenta.
Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
12 La speranza differita fa languire il cuore, ma il desiderio adempiuto è un albero di vita.
Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
13 Chi sprezza la parola si costituisce, di fronte ad essa, debitore, ma chi rispetta il comandamento sarà ricompensato.
Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
14 L’insegnamento del savio è una fonte di vita per schivare le insidie della morte.
Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
15 Buon senno procura favore, ma il procedere dei perfidi è duro.
Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
16 Ogni uomo accorto agisce con conoscenza, ma l’insensato fa sfoggio di follia.
Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
17 Il messo malvagio cade in sciagure, ma l’ambasciatore fedele reca guarigione.
Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
18 Miseria e vergogna a chi rigetta la correzione, ma chi dà retta alla riprensione è onorato.
Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
19 Il desiderio adempiuto è dolce all’anima, ma agl’insensati fa orrore l’evitare il male.
Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
20 Chi va coi savi diventa savio, ma il compagno degl’insensati diventa cattivo.
Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
21 Il male perseguita i peccatori ma il giusto è ricompensato col bene.
Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
22 L’uomo buono lascia una eredità ai figli de’ suoi figli, ma la ricchezza del peccatore è riserbata al giusto.
Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
23 Il campo lavorato dal povero dà cibo in abbondanza, ma v’è chi perisce per mancanza di equità.
Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
24 Chi risparmia la verga odia il suo figliuolo, ma chi l’ama, lo corregge per tempo.
Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
25 Il giusto ha di che mangiare a sazietà, ma il ventre degli empi manca di cibo.
Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.

< Proverbi 13 >