< Proverbi 12 >

1 Chi ama la correzione ama la scienza, ma chi odia la riprensione è uno stupido.
Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
2 L’uomo buono ottiene il favore dell’Eterno, ma l’Eterno condanna l’uomo pien di malizia.
Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
3 L’uomo non diventa stabile con l’empietà, ma la radice dei giusti non sarà mai smossa.
Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
4 La donna virtuosa è la corona del marito, ma quella che fa vergogna gli è un tarlo nell’ossa.
Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
5 I pensieri dei giusti sono equità, ma i disegni degli empi son frode.
Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
6 Le parole degli empi insidiano la vita, ma la bocca degli uomini retti procura liberazione.
Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
7 Gli empi, una volta rovesciati, non sono più, ma la casa dei giusti rimane in piedi.
Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
8 L’uomo è lodato in proporzione del suo senno, ma chi ha il cuore pervertito sarà sprezzato.
Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
9 E’ meglio essere in umile stato ed avere un servo, che fare il borioso e mancar di pane.
Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
10 Il giusto ha cura della vita del suo bestiame, ma le viscere degli empi sono crudeli.
Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
11 Chi coltiva la sua terra avrà pane da saziarsi, ma chi va dietro ai fannulloni e privo di senno.
Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
12 L’empio agogna la preda de’ malvagi, ma la radice dei giusti porta il suo frutto.
Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
13 Nel peccato delle labbra sta un’insidia funesta, ma il giusto uscirà dalla distretta.
Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
14 Per il frutto della sua bocca l’uomo è saziato di beni, e ad ognuno è reso secondo l’opera delle sue mani.
Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
15 La via dello stolto è diritta agli occhi suoi, ma chi ascolta i consigli è savio.
Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
16 Lo stolto lascia scorger subito il suo cruccio, ma chi dissimula un affronto è uomo accorto.
Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
17 Chi dice la verità proclama ciò ch’è giusto, ma il falso testimonio parla con inganno.
Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
18 C’è chi, parlando inconsultamente trafigge come spada, ma la lingua de’ savi reca guarigione.
Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
19 Il labbro veridico è stabile in perpetuo, ma la lingua bugiarda non dura che un istante.
Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
20 L’inganno è nel cuore di chi macchina il male, ma per chi nutre propositi di pace v’è gioia.
Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
21 Nessun male incoglie al giusto, ma gli empi son pieni di guai.
Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
22 Le labbra bugiarde sono un abominio per l’Eterno, ma quelli che agiscono con sincerità gli sono graditi.
Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
23 L’uomo accorto nasconde quello che sa, ma il cuor degli stolti proclama la loro follia.
Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
24 La mano dei diligenti dominerà, ma la pigra sarà tributaria.
Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
25 Il cordoglio ch’è nel cuore dell’uomo l’abbatte, ma la parola buona lo rallegra.
Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
26 Il giusto indica la strada al suo compagno, ma la via degli empi li fa smarrire.
Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
27 Il pigro non arrostisce la sua caccia, ma la solerzia è per l’uomo un tesoro prezioso.
Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
28 Nel sentiero della giustizia sta la vita, e nella via ch’essa traccia non v’è morte.
Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.

< Proverbi 12 >