< Nahum 2 >

1 Un distruttore sale contro di te, o Ninive; custodisci bene la fortezza, sorveglia le strade, fortìficati i fianchi, raccogli tutte quante le tue forze!
Wodzathira nkhondo akubwera kudzalimbana nawe, Ninive. Tetezani malinga anu, dziyangʼanani ku msewu, konzekerani nkhondo, valani dzilimbe.
2 Poiché l’Eterno ristabilisce la gloria di Giacobbe, e la gloria d’Israele, perché i saccheggiatori li han saccheggiati, e han distrutto i loro tralci.
Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo ngati ulemerero wa Israeli, ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu ndipo anawononganso mpesa wawo.
3 Lo scudo de’ suoi prodi è tinto in rosso, i suoi guerrieri veston di scarlatto; il giorno in cui ei si prepara, l’acciaio dei carri scintilla, e si brandiscon le lance di cipresso.
Zishango za ankhondo ake ndi zofiira; asilikali ake avala zovala zofiirira. Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira tsiku la kukonzekera kwake. Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
4 I carri si slancian furiosamente per le strade, si precipitano per le piazze; il loro aspetto è come di fiaccole, guizzan come folgori.
Magaleta akuthamanga mʼmisewu akungothamangathamanga pa mabwalo. Akuoneka ngati miyuni yoyaka; akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
5 Il re si ricorda de’ suoi prodi ufficiali; essi inciampano nella loro marcia, si precipitano verso le mura, e la difesa è preparata.
Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka, koma iwo akubwera napunthwa. Akuthamangira ku linga la mzinda; akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
6 Le porte de’ fiumi s’aprono, e il palazzo crolla.
Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje ndipo nyumba yaufumu yagwa.
7 E’ fatto! Ninive è spogliata nuda e portata via; le sue serve gemono con voce di colombe, e si picchiano il petto.
Zatsimikizika kuti mzinda utengedwa ndi kupita ku ukapolo. Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda ndipo akudziguguda pachifuwa.
8 Essa è stata come un serbatoio pieno d’acqua, dal giorno che esiste; e ora fuggono! “Fermate! fermate!” ma nessuno si vòlta.
Ninive ali ngati dziwe, ndipo madzi ake akutayika. Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!” Koma palibe amene akubwerera.
9 Predate l’argento, predate l’oro! Vi son de’ tesori senza fine, dei monti d’oggetti preziosi d’ogni sorta.
Funkhani siliva! Funkhani golide! Katundu wake ndi wochuluka kwambiri, chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
10 Essa è vuotata, spogliata, devastata; i cuori si struggono, le ginocchia tremano, tutti i fianchi si contorcono, tutti i volti impallidiscono.
Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa! Mitima yasweka, mawondo akuwombana, anthu akunjenjemera ndipo nkhope zasandulika ndi mantha.
11 Dov’è questo ricetto di leoni, questo luogo dove facevano il pasto i leoncelli, dove passeggiavano il leone, la leonessa e i leoncini, senza che alcuno li spaventasse?
Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti, malo amene mikango inkadyetserako ana ake, kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako, ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
12 Quivi il leone sbranava per i suoi piccini, strangolava per le sue leonesse, ed empiva le sue grotte di preda, e le sue tane di rapina.
Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake ndiponso kuphera nyama mkango waukazi, kudzaza phanga lake ndi zimene wapha ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
13 Eccomi a te, dice l’Eterno degli eserciti; io arderò i tuoi carri che andranno in fumo, e la spada divorerà i tuoi leoncelli; io sterminerò dalla terra la tua preda, e più non s’udrà la voce de’ tuoi messaggeri.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo, ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono; sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi. Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”

< Nahum 2 >