< Lamentazioni 5 >

1 Ricordati, Eterno, di quello che ci è avvenuto! Guarda e vedi il nostro obbrobrio!
Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
2 La nostra eredità è passata a degli stranieri, le nostre case, a degli estranei.
Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
3 Noi siam diventati orfani, senza padre, le nostre madri son come vedove.
Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
4 Noi beviamo la nostr’acqua a prezzo di danaro, le nostre legna ci vengono a pagamento.
Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
5 Col collo carico noi siamo inseguiti, siamo spossati, non abbiamo requie.
Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
6 Abbiam teso la mano verso l’Egitto e verso l’Assiria, per saziarci di pane.
Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
7 I nostri padri hanno peccato, e non sono più; e noi portiamo la pena delle loro iniquità.
Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
8 Degli schiavi dominano su noi, e non v’è chi ci liberi dalle loro mani.
Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
9 Noi raccogliamo il nostro pane col rischio della nostra vita, affrontando la spada del deserto.
Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
10 La nostra pelle brucia come un forno, per l’arsura della fame.
Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
11 Essi hanno disonorato le donne in Sion, le vergini nelle città di Giuda.
Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
12 I capi sono stati impiccati dalle loro mani, la persona de’ vecchi non è stata rispettata.
Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
13 I giovani han portato le macine, i giovanetti han vacillato sotto il carico delle legna.
Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
14 I vecchi hanno abbandonato la porta, i giovani la musica dei loro strumenti.
Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
15 La gioia de’ nostri cuori è cessata, le nostre danze son mutate in lutto.
Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
16 La corona ci è caduta dal capo; guai a noi, poiché abbiamo peccato!
Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
17 Per questo langue il nostro cuore, per questo s’oscuran gli occhi nostri:
Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
18 perché il monte di Sion è desolato, e vi passeggian le volpi.
pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
19 Ma tu, o Eterno, regni in perpetuo; il tuo trono sussiste d’età in età.
Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
20 Perché ci dimenticheresti tu in perpetuo, e ci abbandoneresti per un lungo tempo?
Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
21 Facci tornare a te, o Eterno, e noi torneremo! Ridonaci de’ giorni come quelli d’un tempo!
Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
22 Ché, ora, tu ci hai veramente reietti, e ti sei grandemente adirato contro di noi!
pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.

< Lamentazioni 5 >