< Giobbe 27 >
1 Giobbe riprese il suo discorso e disse:
Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 “Come vive Iddio che mi nega giustizia, come vive l’Onnipotente che mi amareggia l’anima,
“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
3 finché avrò fiato e il soffio di Dio sarà nelle mie nari,
nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
4 le mie labbra, no, non diranno nulla d’ingiusto, e la mia lingua non proferirà falsità.
pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
5 Lungi da me l’idea di darvi ragione! Fino all’ultimo respiro non mi lascerò togliere la mia integrità.
Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
6 Ho preso a difendere la mia giustizia e non cederò; il cuore non mi rimprovera uno solo de’ miei giorni.
Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
7 Sia trattato da malvagio il mio nemico e da perverso chi si leva contro di me!
“Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
8 Quale speranza rimane mai all’empio quando Iddio gli toglie, gli rapisce l’anima?
Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
9 Iddio presterà egli orecchio al grido di lui, quando gli verrà sopra la distretta?
Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
10 Potrà egli prendere il suo diletto nell’Onnipotente? invocare Iddio in ogni tempo?
Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
11 Io vi mostrerò il modo d’agire di Dio, non vi nasconderò i disegni dell’Onnipotente.
“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
12 Ma queste cose voi tutti le avete osservate e perché dunque vi perdete in vani discorsi?
Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
13 Ecco la parte che Dio riserba all’empio, l’eredità che l’uomo violento riceve dall’Onnipotente.
“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
14 Se ha figli in gran numero son per la spada; la sua progenie non avrà pane da saziarsi.
Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
15 I superstiti son sepolti dalla morte, e le vedove loro non li piangono.
Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
16 Se accumula l’argento come polvere, se ammucchia vestiti come fango;
Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
17 li ammucchia, sì, ma se ne vestirà il giusto, e l’argento l’avrà come sua parte l’innocente.
zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
18 La casa ch’ei si edifica è come quella della tignuola, come il capanno che fa il guardiano della vigna.
Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
19 Va a letto ricco, ma per l’ultima volta; apre gli occhi e non è più.
Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
20 Terrori lo sorprendono come acque; nel cuor della notte lo rapisce un uragano.
Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
21 Il vento d’oriente lo porta via, ed egli se ne va; lo spazza in un turbine dal luogo suo.
Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
22 Iddio gli scaglia addosso i suoi dardi, senza pietà, per quanto egli tenti di scampare a’ suoi colpi.
Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
23 La gente batte le mani quando cade, e fischia dietro a lui quando lascia il luogo dove stava.
Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”