< Proverbi 18 >
1 Colui che si separa cerca le sue cupidità, E schernisce ogni legge e ragione.
Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
2 Lo stolto non si diletta nella prudenza, Ma in ciò che il cuor suo si manifesti.
Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
3 Quando viene un empio, viene anche lo sprezzo, E il vituperio con ignominia.
Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
4 Le parole della bocca dell'uomo eccellente sono acque profonde; La fonte di sapienza [è] un torrente che sgorga.
Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
5 Egli non [è] bene d'aver riguardo alla qualità dell'empio, Per far torto al giusto nel giudicio.
Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
6 Le labbra dello stolto entrano in contesa, E la sua bocca chiama le percosse.
Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
7 La bocca dello stolto [è] la sua ruina, E le sue labbra [sono] il laccio dell'anima sua.
Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
8 Le parole di chi va bisbigliando paiono lusinghevoli; Ma scendono fin nell'interiora del ventre.
Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
9 Chi si porta rimessamente nel suo lavoro, [È] fratello dell'uomo dissipatore.
Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
10 Il Nome del Signore [è] una forte torre; Il giusto vi ricorrerà, e sarà in salvo in luogo elevato.
Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
11 I beni del ricco [son] la sua città di fortezza, E come un alto muro alla sua immaginazione.
Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
12 Il cuor dell'uomo s'innalza avanti la ruina; Ma l'umiltà [va] davanti alla gloria.
Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
13 Chi fa risposta prima che abbia udito, Ciò gli [è] pazzia e vituperio.
Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
14 Lo spirito dell'uomo sostiene l'infermità di esso; Ma chi solleverà lo spirito afflitto?
Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
15 Il cuor dell'[uomo] intendente acquista scienza; E l'orecchio de' savi cerca conoscimento.
Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
16 Il presente dell'uomo gli fa far largo, E lo conduce davanti a' grandi.
Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
17 Chi [è] il primo a [piatir] la sua causa ha ragione; Ma il suo compagno vien [poi], ed esamina quello [ch'egli ha detto].
Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
18 La sorte fa cessar le liti, E fa gli spartimenti fra i potenti.
Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
19 Il fratello offeso [è più inespugnabile] che una forte città; E le contese [tra fratelli son] come le sbarre di un palazzo.
Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
20 Il ventre dell'uomo sarà saziato del frutto della sua bocca; Egli sarà saziato della rendita delle sue labbra.
Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
21 Morte e vita [sono] in poter della lingua; E chi l'ama mangerà del frutto di essa.
Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
22 Chi ha trovata moglie ha trovata una buona cosa, Ed ha ottenuto favor del Signore.
Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
23 Il povero parla supplichevolmente; Ma il ricco risponde duramente.
Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
24 Un uomo che ha degli amici deve portarsi da amico; E vi è tale amico, che è più congiunto che un fratello.
Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.