< Geremia 15 >

1 Poi il Signore mi disse: Avvegnachè Mosè e Samuele si presentassero davanti alla mia faccia, l'anima mia non sarebbe però inverso questo popolo; manda[li] fuori della mia presenza, ed escansene fuori.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Ngakhale Mose ndi Samueli akanayima pamaso panga kupempherera anthu awa, Ine sindikanawachitira chisoni. Achotseni ndipo ndisawaonenso! Aleke apite!
2 Che se pur ti dicono: Dove usciremo? di' loro: Così ha detto il Signore: Chi [è condannato] alla mortalità, [esca] alla mortalità; chi alla spada, [esca] alla spada; chi alla fame, [esca] alla fame; chi alla cattività, [esca] alla cattività.
Ndipo ngati akufunsa iwe kuti, ‘Kodi tipite kuti?’ uwawuze kuti, ‘Yehova akuti, “‘Oyenera kufa adzafa; oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga; oyenera kufa ndi njala adzafa ndi njala; oyenera kupita ku ukapolo adzapita ku ukapolo.’
3 Ed io costituirò sopra loro quattro generazioni, dice il Signore: la spada, per uccidere; i cani, per istrascinare; gli uccelli del cielo, e le bestie della terra, per divorare, e per distruggere.
“Ine ndidzawatumizira mitundu inayi ya zinthu zowononga,” akutero Yehova, “lupanga lowapha, agalu owaluma, mbalame zamumlengalenga ndiponso zirombo zoti ziwadye ndi kuwawononga.
4 E farò che saranno agitati per tutti i regni della terra, per cagion di Manasse, figliuolo di Ezechia, re di Giuda; per quello ch'egli ha fatto in Gerusalemme.
Ndidzawasandutsa kukhala chinthu chonyansa kwa anthu a maufumu onse a dziko lapansi chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya mfumu ya Yuda anachita mu Yerusalemu.
5 Perciocchè, o Gerusalemme, chi avrebbe pietà di te? chi si condorrebbe teco? o chi si rivolgerebbe per domandar[ti] del tuo bene stare?
“Kodi adzakumvera chisoni ndani, Yerusalemu? Kodi adzakulira ndani? Kodi ndani amene adzapatuka kufunsa za moyo wako?
6 Tu mi hai abbandonato, dice il Signore, e te ne sei ita indietro; io altresì stenderò la mano sopra te, e ti distruggerò; io sono stanco di pentirmi.
Inu mwandikana Ine,” akutero Yehova. “Inu mukubwererabe mʼmbuyo. Choncho Ine ndidzakukanthani. Ndatopa ndi kukuchitirani chifundo.
7 Benchè io li abbia sventolati con la ventola nelle porte del paese, [ed] abbia deserto, [e] distrutto il mio popolo, non però si son convertiti dalle lor vie.
Ine ndidzakubalalitsani kukuchotsani mʼmizinda ya mʼdzikomo monga mmene amachitira ndi mankhusu popeta ndi lichero. Anthu anga ndinawaliritsa ndi kuwawononga chifukwa sanasinthe makhalidwe awo oyipa.
8 Le sue vedove sono state da me moltiplicate, più che la rena de' mari; io ho loro addotto in pien mezzodì un guastatore contro alla madre de' giovani; io ho fatto di subito cader sopra lei turbamento e spaventi.
Ndinachulukitsa amayi awo amasiye kupambana mchenga wa kunyanja. Amayiwo ndinawawonongera ana awo aamuna dzuwa lili pamutu. Mwadzidzidzi ndinawagwetsera kuwawa mtima ndi mantha.
9 Quella che avea partoriti sette [figliuoli] è divenuta fiacca, l'anima sua ha ansato io suo sole è tramontato, mentre [era] ancora giorno; è stata confusa e svergognata; ancora darò il lor rimanente alla spada, all'arbitrio de'lor nemici, dice il Signore.
Mayi wa ana asanu ndi awiri wakomoka ndipo akupuma wefuwefu. Dzuwa lake lalowa ukanali usana; anamuchititsa manyazi ndipo wathedwa nzeru. Otsala ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo kuti awaphe ndi lupanga,” akutero Yehova.
10 Ahi lasso me! madre mia; perciocchè tu mi hai partorito [per essere] uomo di lite, e di contesa a tutto il paese: io non ho [loro] dato [nulla] in presto, ed essi altresì non mi hanno prestato [nulla; e pur] tutti quanti mi maledicono.
Kalanga ine, amayi pakuti munandibereka ine, munthu amene ndikutsutsana ndi kulimbana ndi anthu pa dziko lonse! Ine sindinakongoze kapena kukongola kanthu, komatu aliyense akunditemberera.
11 Il Signore ha detto: Se il tuo [sol] rimanente non [è riserbato] per lo bene; se io non fo che il nemico si scontri in te nel tempo dell'avversità, e nel tempo della distretta.
Yehova anati, “Ndithudi, Ine ndidzakulanditsa kuti upeze bwino. Ndithudi, adani ako adzakupempha pa nthawi ya tsoka ndi ya mavuto awo.
12 Potrebbesi rompere il ferro, il ferro di Aquilone, e il rame?
“Palibe munthu amene angathe kudula chitsulo, makamaka chitsulo chochokera kumpoto chosakaniza ndi mkuwa.
13 Io darò senza prezzo in preda le tue facoltà, e i tuoi tesori, in tutti i tuoi confini; e [ciò] per tutti i tuoi peccati.
Anthu ako ndi chuma chako ndidzazipereka kwa ofunkha popanda malipiro, chifukwa cha machimo anu onse a mʼdziko lanu lonse.
14 E farò passare i tuoi nemici per un paese [che] tu non sai; perciocchè un fuoco si è acceso nella mia ira, il quale si apprenderà sopra voi.
Ndidzakusandutsani akapolo a adani anu mʼdziko limene inu simulidziwa, chifukwa mkwiyo wanga wayaka ngati moto umene udzakutenthani.”
15 O Signore, tu [il] sai; ricordati di me, e visitami, e vendicami de' miei persecutori; non rapirmi, mentre tu sei lento all'ira; conosci che io soffero vituperio per te.
Ine ndinati, “Inu Yehova, mumadziwa zonse; kumbukireni ndi kundisamalira. Ndilipsireni anthu ondizunza. Ndilezereni mtima musandilande moyo wanga. Onani momwe ndi kuvutikira chifukwa cha Inu.
16 [Tosto che] le tue parole sono state ritrovate [da me], io le ho mangiate; e la tua parola mi è stata in gioia, e in allegrezza del mio cuore; perciocchè il tuo Nome è invocato sopra me, o Signore Iddio degli eserciti.
Munandiyankhula ndipo mawu anu ndinawalandira bwino. Mawu anu anandipatsa chimwemwe ndipo mtima wanga unasangalala. Paja ine, Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndimadziwika ndi dzina lanu.
17 Io non son seduto nel consiglio degli schernitori, per far festa, ed allegrezza; io son seduto tutto solo, per cagion della tua mano; perciocchè tu mi hai empiuto d'indegnazione.
Sindinakhale nawo mʼgulu la anthu amadyera, sindinasangalale nawo anthu amenewo. Ndinakhala ndekha chifukwa choti dzanja lanu linali pa ine ndipo munadzaza mu mtima mwanga ndi mkwiyo.
18 Perchè è stato il mio dolore perpetuo, e la mia piaga disperata? perchè ha ella ricusato d'esser guarita? mi saresti tu pure come una cosa fallace, [come] acque che non son perenni?
Nanga nʼchifukwa chiyani mavuto anga sakutha? Bwanji chilonda changa sichikupola? Kodi inu mudzakhala ngati mtsinje wowuma nthawi yachilimwe, kapena ngati kasupe wopanda madzi?”
19 Perciò così ha detto il Signore: Se tu ti converti, io ti ristorerò, e tu starai davanti a me; e se tu separi il prezioso dal vile, tu sarai come la mia bocca; convertansi eglino a te; ma tu, non convertirti a loro.
Tsono Yehova anandiyankha kuti, “Ukabwerera kwa Ine, ndidzakulandiranso ndipo udzakhalanso mtumiki wanga. Ngati udzayankhula mawu oyenera osati achabechabe, udzakhalanso mneneri wanga. Anthu adzabwera kwa iwe ndipo sipadzafunika kuti iwe upite kwa iwo.
20 Ed io ti farò essere a questo popolo, a guisa d'un muro fortissimo di rame; ed essi combatteranno contro a te, ma non ti vinceranno; perciocchè io [son] teco, per salvarti e per riscuoterti, dice il Signore.
Ndidzakusandutsa ngati khoma lolimba ngati mkuwa kwa anthu awa. Adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, pakuti Ine ndili nawe kukulanditsa ndi kukupulumutsa,” akutero Yehova.
21 E ti trarrò di man de' maligni, e ti riscoterò di man de' violenti.
“Ndidzakupulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa ndipo ndidzakuwombola kwa anthu ankhanza.”

< Geremia 15 >