< 1 Cronache 24 >

1 OR quant'è a' figliuoli d'Aaronne, i loro spartimenti [furono questi]: I figliuoli d'Aaronne [furono] Nadab, ed Abihu, Eleazaro, ed Itamar.
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 Ed essendo Nadab ed Abihu morti senza figliuoli davanti al padre loro, Eleazaro ed Itamar esercitaroro il sacerdozio.
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 Or Davide li distribuì secondo gli ordini loro nel lor ministerio, [essendo] Sadoc de' figliuoli di Eleazaro, ed Ahimelec de' figliuoli d'Itamar.
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 Ed i figliuoli di Eleazaro si trovarono in più gran numero di capi d'uomini, che i figliuoli di Itamar, quando gli spartimenti furono fatti. De' figliuoli di Eleazaro [vi erano] sedici capi di famiglie paterne, e de' figliuoli d'Itamar otto.
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 E gli spartimenti furono fatti a sorte, gli uni per mezzo gli altri; perciocchè anche i capi del santuario, e [della Casa] di Dio, erano de' figliuoli di Eleazaro, e de' figliuoli d'Itamar.
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 E Semaia, figliuolo di Natanael, Scriba, [della tribù] di Levi, li descrisse davanti al re, e davanti a' capi [del popolo], ed al sacerdote Sadoc, e ad Ahimelec, figliuolo di Ebiatar, ed a' capi delle [famiglie] paterne de' sacerdoti, e de' Leviti; una casa paterna si prendeva [de' discendenti] di Eleazaro, ed un'[altra congiuntamente di que]'d'Itamar.
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 La prima sorte adunque scadde a Ioiarib, la seconda a Iedaia,
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 la terza ad Harim, la quarta a Seorim,
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 la quinta a Malchia,
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 la sesta a Miamin, la settima a Cos, l'ottava ad Abia,
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 la nona a Iesua, la decima a Secania,
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 l'undecima ad Eliasib, la duodecima a Iachim,
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 la tredicesima ad Huppa, la quartadecima a Iesebeab,
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 la quintadecima a Bilga, la sestadecima ad Immer,
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 la diciassettesima ad Hezir, la diciottesima a Pisses,
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 la diciannovesima a Petahia, la ventesima ad Ezechiele,
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 la ventunesima a Iachin, la ventiduesima a Gamul,
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 la ventesimaterza a Delaia, la ventiquattresima a Maazia.
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 Questi [furono] i loro ordini nel lor ministerio, [secondo i quali aveano] da venir nella Casa del Signore, secondo che era loro ordinato, sotto la condotta di Aaronne, lor padre; come il Signore Iddio d'Israele gli avea comandato.
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 E QUANT'è al rimanente de' figliuoli di Levi, de' figliuoli di Amram, [vi fu] Subael; e de' figliuoli di Subael, Iedeia.
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 Quant'è a' figliuoli di Rehabia, Isia [fu] il capo.
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 Degl'Ishariti, Selomot; de' figliuoli di Selomot, Iahat.
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 [De' figliuoli di Hebron, Ieria era il primo], Amaria il secondo, Iahaziel il terzo, Iecamam il quarto.
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 De' figliuoli di Uzziel [fu capo] Mica; de' figliuoli di Mica, Samir.
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 Il fratello di Mica [fu] Isia; de' figliuoli d'Isia, Zaccaria [fu il capo].
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 I figliuoli di Merari[furono] Mehali, e Musi; e de' figliuoli di Iaazia, Beno [fu il capo].
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 I figliuoli di Merari, per Iaazia, [furono] Beno, e Soham, e Zaccur, ed Ibri.
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 Di Mahali [il capo fu] Eleazaro, il quale non ebbe figliuoli.
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 Quant'è a Chis, [il capo de]'suoi figliuoli [fu] Ierameel.
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 E de' figliuoli di Musi [furono i capi] Mahali, ed Eder, e Ierimot. Questi [furono] i figliuoli de' Leviti, secondo le lor case paterne.
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 E tirarono anch'essi le sorti, al pari de' figliuoli d'Aaronne, lor fratelli, in presenza del re Davide, e di Sadoc, e d'Ahimelec, e de' capi delle [famiglie] paterne de' sacerdoti, e de' Leviti; le principali delle [case] paterne [essendo] pareggiate ad [altre più] piccole de' lor fratelli.
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

< 1 Cronache 24 >