< Salmi 91 >
1 Tu che abiti al riparo dell'Altissimo e dimori all'ombra dell'Onnipotente,
Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
2 dì al Signore: «Mio rifugio e mia fortezza, mio Dio, in cui confido».
Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa, Mulungu wanga amene ndimadalira.”
3 Egli ti libererà dal laccio del cacciatore, dalla peste che distrugge.
Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje ndi ku mliri woopsa;
4 Ti coprirà con le sue penne sotto le sue ali troverai rifugio.
Adzakuphimba ndi nthenga zake, ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo; kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
5 La sua fedeltà ti sarà scudo e corazza; non temerai i terrori della notte né la freccia che vola di giorno,
Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku, kapena muvi wowuluka masana,
6 la peste che vaga nelle tenebre, lo sterminio che devasta a mezzogiorno.
kapena mliri umene umayenda mu mdima, kapena zowononga za pa nthawi ya masana.
7 Mille cadranno al tuo fianco e diecimila alla tua destra; ma nulla ti potrà colpire.
Anthu 1,000 atha kufa pambali pako, anthu 10,000 kudzanja lako lamanja, koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.
8 Solo che tu guardi, con i tuoi occhi vedrai il castigo degli empi.
Udzapenya ndi maso ako ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.
9 Poiché tuo rifugio è il Signore e hai fatto dell'Altissimo la tua dimora,
Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo; wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.
10 non ti potrà colpire la sventura, nessun colpo cadrà sulla tua tenda.
Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera, zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.
11 Egli darà ordine ai suoi angeli di custodirti in tutti i tuoi passi.
Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;
12 Sulle loro mani ti porteranno perché non inciampi nella pietra il tuo piede.
ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.
13 Camminerai su aspidi e vipere, schiaccerai leoni e draghi.
Udzapondaponda mkango ndi njoka, udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.
14 Lo salverò, perché a me si è affidato; lo esalterò, perché ha conosciuto il mio nome.
“Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa; ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
15 Mi invocherà e gli darò risposta; presso di lui sarò nella sventura, lo salverò e lo renderò glorioso.
Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha; ndidzakhala naye pa mavuto, ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
16 Lo sazierò di lunghi giorni e gli mostrerò la mia salvezza.
Ndidzamupatsa moyo wautali ndi kumupulumutsa.”