< Salmi 8 >
1 Al maestro di coro. Sul canto: «I Torchi...». Salmo. Di Davide. O Signore, nostro Dio, quanto è grande il tuo nome su tutta la terra: sopra i cieli si innalza la tua magnificenza.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
2 Con la bocca dei bimbi e dei lattanti affermi la tua potenza contro i tuoi avversari, per ridurre al silenzio nemici e ribelli.
Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
3 Se guardo il tuo cielo, opera delle tue dita, la luna e le stelle che tu hai fissate,
Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
4 che cosa è l'uomo perché te ne ricordi e il figlio dell'uomo perché te ne curi?
munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
5 Eppure l'hai fatto poco meno degli angeli, di gloria e di onore lo hai coronato:
Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
6 gli hai dato potere sulle opere delle tue mani, tutto hai posto sotto i suoi piedi;
Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
7 tutti i greggi e gli armenti, tutte le bestie della campagna;
nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
8 Gli uccelli del cielo e i pesci del mare, che percorrono le vie del mare.
mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
9 O Signore, nostro Dio, quanto è grande il tuo nome su tutta la terra.
Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!