< Salmi 76 >
1 Al maestro del coro. Su strumenti a corda con cetre. Salmo. Di Asaf. Canto. Dio è conosciuto in Giuda, in Israele è grande il suo nome.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
2 E' in Gerusalemme la sua dimora, la sua abitazione, in Sion.
Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
3 Qui spezzò le saette dell'arco, lo scudo, la spada, la guerra.
Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
4 Splendido tu sei, o Potente, sui monti della preda;
Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
5 furono spogliati i valorosi, furono colti dal sonno, nessun prode ritrovava la sua mano.
Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
6 Dio di Giacobbe, alla tua minaccia, si arrestarono carri e cavalli.
Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
7 Tu sei terribile; chi ti resiste quando si scatena la tua ira?
Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
8 Dal cielo fai udire la sentenza: sbigottita la terra tace
Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
9 quando Dio si alza per giudicare, per salvare tutti gli umili della terra.
pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
10 L'uomo colpito dal tuo furore ti dà gloria, gli scampati dall'ira ti fanno festa.
Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
11 Fate voti al Signore vostro Dio e adempiteli, quanti lo circondano portino doni al Terribile,
Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
12 a lui che toglie il respiro ai potenti; è terribile per i re della terra.
Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.