< Salmi 2 >

1 Perché le genti congiurano perché invano cospirano i popoli?
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 Insorgono i re della terra e i principi congiurano insieme contro il Signore e contro il suo Messia:
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 «Spezziamo le loro catene, gettiamo via i loro legami».
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 Se ne ride chi abita i cieli, li schernisce dall'alto il Signore.
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 Egli parla loro con ira, li spaventa nel suo sdegno:
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 «Io l'ho costituito mio sovrano sul Sion mio santo monte».
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 Annunzierò il decreto del Signore. Egli mi ha detto: «Tu sei mio figlio, io oggi ti ho generato.
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 Chiedi a me, ti darò in possesso le genti e in dominio i confini della terra.
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 Le spezzerai con scettro di ferro, come vasi di argilla le frantumerai».
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 E ora, sovrani, siate saggi istruitevi, giudici della terra;
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 servite Dio con timore e con tremore esultate;
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 che non si sdegni e voi perdiate la via. Improvvisa divampa la sua ira. Beato chi in lui si rifugia.
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

< Salmi 2 >