< Proverbi 1 >
1 Proverbi di Salomone, figlio di Davide, re d'Israele,
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 per conoscere la sapienza e la disciplina, per capire i detti profondi,
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 per acquistare un'istruzione illuminata, equità, giustizia e rettitudine,
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 per dare agli inesperti l'accortezza, ai giovani conoscenza e riflessione.
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 Ascolti il saggio e aumenterà il sapere, e l'uomo accorto acquisterà il dono del consiglio,
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 per comprendere proverbi e allegorie, le massime dei saggi e i loro enigmi.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 Il timore del Signore è il principio della scienza; gli stolti disprezzano la sapienza e l'istruzione.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Ascolta, figlio mio, l'istruzione di tuo padre e non disprezzare l'insegnamento di tua madre,
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 perché saranno una corona graziosa sul tuo capo e monili per il tuo collo.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Figlio mio, se i peccatori ti vogliono traviare, non acconsentire!
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 Se ti dicono: «Vieni con noi, complottiamo per spargere sangue, insidiamo impunemente l'innocente,
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 inghiottiamoli vivi come gli inferi, interi, come coloro che scendon nella fossa; (Sheol )
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
13 troveremo ogni specie di beni preziosi, riempiremo di bottino le nostre case;
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 tu getterai la sorte insieme con noi, una sola borsa avremo in comune»,
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 figlio mio, non andare per la loro strada, tieni lontano il piede dai loro sentieri!
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 I loro passi infatti corrono verso il male e si affrettano a spargere il sangue.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 Invano si tende la rete sotto gli occhi degli uccelli.
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 Ma costoro complottano contro il proprio sangue, pongono agguati contro se stessi.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Tale è la fine di chi si dà alla rapina; la cupidigia toglie di mezzo colui che ne è dominato.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 La Sapienza grida per le strade nelle piazze fa udire la voce;
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 dall'alto delle mura essa chiama, pronunzia i suoi detti alle porte della città:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 «Fino a quando, o inesperti, amerete l'inesperienza e i beffardi si compiaceranno delle loro beffe e gli sciocchi avranno in odio la scienza?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Volgetevi alle mie esortazioni: ecco, io effonderò il mio spirito su di voi e vi manifesterò le mie parole.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Poiché vi ho chiamato e avete rifiutato, ho steso la mano e nessuno ci ha fatto attenzione;
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 avete trascurato ogni mio consiglio e la mia esortazione non avete accolto;
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 anch'io riderò delle vostre sventure, mi farò beffe quando su di voi verrà la paura,
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 quando come una tempesta vi piomberà addosso il terrore, quando la disgrazia vi raggiungerà come un uragano, quando vi colpirà l'angoscia e la tribolazione.
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Allora mi invocheranno, ma io non risponderò, mi cercheranno, ma non mi troveranno.
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 Poiché hanno odiato la sapienza e non hanno amato il timore del Signore;
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 non hanno accettato il mio consiglio e hanno disprezzato tutte le mie esortazioni;
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 mangeranno il frutto della loro condotta e si sazieranno dei risultati delle loro decisioni.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Sì, lo sbandamento degli inesperti li ucciderà e la spensieratezza degli sciocchi li farà perire;
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 ma chi ascolta me vivrà tranquillo e sicuro dal timore del male».
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”