< Giobbe 9 >
1 Giobbe rispose dicendo:
Ndipo Yobu anayankha kuti,
2 In verità io so che è così: e come può un uomo aver ragione innanzi a Dio?
“Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
3 Se uno volesse disputare con lui, non gli risponderebbe una volta su mille.
Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
4 Saggio di mente, potente per la forza, chi s'è opposto a lui ed è rimasto salvo?
Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
5 Sposta le montagne e non lo sanno, egli nella sua ira le sconvolge.
Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
6 Scuote la terra dal suo posto e le sue colonne tremano.
Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
7 Comanda al sole ed esso non sorge e alle stelle pone il suo sigillo.
Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
8 Egli da solo stende i cieli e cammina sulle onde del mare.
Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
9 Crea l'Orsa e l'Orione, le Pleiadi e i penetrali del cielo australe.
Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
10 Fa cose tanto grandi da non potersi indagare, meraviglie da non potersi contare.
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
11 Ecco, mi passa vicino e non lo vedo, se ne va e di lui non m'accorgo.
Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
12 Se rapisce qualcosa, chi lo può impedire? Chi gli può dire: «Che fai?».
Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
13 Dio non ritira la sua collera: sotto di lui sono fiaccati i sostenitori di Raab.
Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
14 Tanto meno io potrei rispondergli, trovare parole da dirgli!
“Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
15 Se avessi anche ragione, non risponderei, al mio giudice dovrei domandare pietà.
Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
16 Se io lo invocassi e mi rispondesse, non crederei che voglia ascoltare la mia voce.
Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
17 Egli con una tempesta mi schiaccia, moltiplica le mie piaghe senza ragione,
Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
18 non mi lascia riprendere il fiato, anzi mi sazia di amarezze.
Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
19 Se si tratta di forza, è lui che dà il vigore; se di giustizia, chi potrà citarlo?
Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
20 Se avessi ragione, il mio parlare mi condannerebbe; se fossi innocente, egli proverebbe che io sono reo.
Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
21 Sono innocente? Non lo so neppure io, detesto la mia vita!
“Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
22 Per questo io dico: «E' la stessa cosa»: egli fa perire l'innocente e il reo!
Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
23 Se un flagello uccide all'improvviso, della sciagura degli innocenti egli ride.
Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
24 La terra è lasciata in balìa del malfattore: egli vela il volto dei suoi giudici; se non lui, chi dunque sarà?
Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
25 I miei giorni passano più veloci d'un corriere, fuggono senza godere alcun bene,
“Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
26 volano come barche di giunchi, come aquila che piomba sulla preda.
Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
27 Se dico: «Voglio dimenticare il mio gemito, cambiare il mio volto ed essere lieto»,
Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
28 mi spavento per tutti i miei dolori; so bene che non mi dichiarerai innocente.
ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
29 Se sono colpevole, perché affaticarmi invano?
Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
30 Anche se mi lavassi con la neve e pulissi con la soda le mie mani,
Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
31 allora tu mi tufferesti in un pantano e in orrore mi avrebbero le mie vesti.
mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
32 Poiché non è uomo come me, che io possa rispondergli: «Presentiamoci alla pari in giudizio».
“Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
33 Non c'è fra noi due un arbitro che ponga la mano su noi due.
Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
34 Allontani da me la sua verga sì che non mi spaventi il suo terrore:
munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
35 allora io potrò parlare senza temerlo, perché così non sono in me stesso.
Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.