< Giobbe 31 >
1 Avevo stretto con gli occhi un patto di non fissare neppure una vergine.
“Ndinachita pangano ndi maso anga kuti sindidzapenya namwali momusirira.
2 Che parte mi assegna Dio di lassù e che porzione mi assegna l'Onnipotente dall'alto?
Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani? Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?
3 Non è forse la rovina riservata all'iniquo e la sventura per chi compie il male?
Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa, tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?
4 Non vede egli la mia condotta e non conta tutti i miei passi?
Kodi Mulungu saona zochita zanga, ndi kudziwa mayendedwe anga?
5 Se ho agito con falsità e il mio piede si è affrettato verso la frode,
“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso, kapena kufulumira kukachita zachinyengo,
6 mi pesi pure sulla bilancia della giustizia e Dio riconoscerà la mia integrità.
Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,
7 Se il mio passo è andato fuori strada e il mio cuore ha seguito i miei occhi, se alla mia mano si è attaccata sozzura,
ngati mayendedwe anga asempha njira, ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona, kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.
8 io semini e un altro ne mangi il frutto e siano sradicati i miei germogli.
Pamenepo ena adye zimene ndinadzala, ndipo zomera zanga zizulidwe.
9 Se il mio cuore fu sedotto da una donna e ho spiato alla porta del mio prossimo,
“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi, ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,
10 mia moglie macini per un altro e altri ne abusino;
pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya, ndipo amuna ena azigona naye.
11 difatti quello è uno scandalo, un delitto da deferire ai giudici,
Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi, tchimo loyenera kulangidwa nalo.
12 quello è un fuoco che divora fino alla distruzione e avrebbe consumato tutto il mio raccolto.
Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko; ukanapsereza zokolola zanga.
13 Se ho negato i diritti del mio schiavo e della schiava in lite con me,
“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi, pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,
14 che farei, quando Dio si alzerà, e, quando farà l'inchiesta, che risponderei?
ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa? Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?
15 Chi ha fatto me nel seno materno, non ha fatto anche lui? Non fu lo stesso a formarci nel seno?
Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo? Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?
16 Mai ho rifiutato quanto brama il povero, né ho lasciato languire gli occhi della vedova;
“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba, kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,
17 mai da solo ho mangiato il mio tozzo di pane, senza che ne mangiasse l'orfano,
ngati chakudya changa ndinadya ndekha, wosagawirako mwana wamasiye,
18 poiché Dio, come un padre, mi ha allevato fin dall'infanzia e fin dal ventre di mia madre mi ha guidato.
chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake, ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,
19 Se mai ho visto un misero privo di vesti o un povero che non aveva di che coprirsi,
ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa, kapena munthu wosauka alibe chofunda,
20 se non hanno dovuto benedirmi i suoi fianchi, o con la lana dei miei agnelli non si è riscaldato;
ndipo ngati iyeyo sananditamandepo chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,
21 se contro un innocente ho alzato la mano, perché vedevo alla porta chi mi spalleggiava,
ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye, poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,
22 mi si stacchi la spalla dalla nuca e si rompa al gomito il mio braccio,
pamenepo phewa langa lipokonyeke, mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.
23 perché mi incute timore la mano di Dio e davanti alla sua maestà non posso resistere.
Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu, ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.
24 Se ho riposto la mia speranza nell'oro e all'oro fino ho detto: «Tu sei la mia fiducia»;
“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’
25 se godevo perché grandi erano i miei beni e guadagnava molto la mia mano;
ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri, zinthu zimene manja anga anazipeza,
26 se vedendo il sole risplendere e la luna chiara avanzare,
ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala, kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,
27 si è lasciato sedurre in segreto il mio cuore e con la mano alla bocca ho mandato un bacio,
ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,
28 anche questo sarebbe stato un delitto da tribunale, perché avrei rinnegato Dio che sta in alto.
pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo, chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.
29 Ho gioito forse della disgrazia del mio nemico e ho esultato perché lo colpiva la sventura,
“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga, kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,
30 io che non ho permesso alla mia lingua di peccare, augurando la sua morte con imprecazioni?
ine sindinachimwe ndi pakamwa panga potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,
31 Non diceva forse la gente della mia tenda: «A chi non ha dato delle sue carni per saziarsi?».
ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti, ‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’
32 All'aperto non passava la notte lo straniero e al viandante aprivo le mie porte.
Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse, pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,
33 Non ho nascosto, alla maniera degli uomini, la mia colpa, tenendo celato il mio delitto in petto,
ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena, kubisa kulakwa mu mtima mwanga
34 come se temessi molto la folla, e il disprezzo delle tribù mi spaventasse, sì da starmene zitto senza uscire di casa.
chifukwa choopa gulu la anthu, ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.
“Aa, pakanakhala wina wondimva! Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe; mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.
Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa, ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.
Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita; ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.
“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,
ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,
pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu ndi udzu mʼmalo mwa barele.” Mawu a Yobu athera pano.