< 1 Cronache 2 >

1 Questi sono i figli di Israele: Ruben, Simeone, Levi, Giuda, Issacar, Zàbulon,
Ana a Israeli anali awa: Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Zebuloni,
2 Dan, Giuseppe, Beniamino, Nèftali, Gad e Aser.
Dani, Yosefe, Benjamini, Nafutali, Gadi ndi Aseri.
3 Figli di Giuda: Er, Onan, Sela; i tre gli nacquero dalla figlia di Sua la Cananea. Er, primogenito di Giuda, era malvagio agli occhi del Signore, che perciò lo fece morire.
Ana a Yuda anali awa: Eri, Onani ndi Sela. Ana atatu awa anabereka ndi mkazi wa Chikanaani, Batisuwa. Eri, mwana woyamba wa Yuda anali woyipa kwambiri pamaso pa Yehova, kotero Yehova anamupha.
4 Tamàr sua nuora gli partorì Perez e Zerach. Totale dei figli di Giuda: cinque.
Mpongozi wake Tamara anamuberekera Perezi ndi Zera. Ana onse a Yuda analipo asanu.
5 Figli di Perez: Chezròn e Camùl.
Ana a Perezi anali awa: Hezironi ndi Hamuli.
6 Figli di Zerach: Zimri, Etan, Eman, Calcol e Darda; in tutto: cinque.
Ana a Zera anali awa: Zimuri, Etani, Hemani, Kalikoli ndi Dara. Onse analipo asanu.
7 Figli di Carmì: Acar, che provocò una disgrazia in Israele con la trasgressione dello sterminio.
Mwana wa Karimi anali Akani, amene anabweretsa mavuto pakati pa Israeli pamene anatenga zinthu zoyenera kuwonongedwa.
8 Figli di Etan: Azaria.
Mwana wa Etani anali Azariya.
9 Figli che nacquero a Chezròn: Ieracmèl, Ram e Chelubài.
Ana amene anabadwa kwa Hezironi anali: Yerahimeeli, Ramu ndi Kelubai.
10 Ram generò Amminadàb; Amminadàb generò Nacsòn, capo dei figli di Giuda.
Ramu anabereka Aminadabu ndipo Aminadabu anali abambo ake a Naasoni, mtsogoleri wa fuko la Yuda.
11 Nacsòn generò Salmà; Salmà generò Booz.
Naasoni anabereka Salima, Salima anabereka Bowazi,
12 Booz generò Obed; Obed generò Iesse.
Bowazi anabereka Obedi ndipo Obedi anabereka Yese.
13 Iesse generò Eliàb il primogenito, Abinadàb, secondo, Simèa, terzo,
Yese anabereka Eliabu mwana wake woyamba, wachiwiri Abinadabu, wachitatu Simea,
14 Netaneèl, quarto, Raddài, quinto,
wachinayi Netaneli, wachisanu Radai,
15 Ozem, sesto, Davide, settimo.
wachisanu ndi chimodzi Ozemu ndi wachisanu ndi chiwiri Davide.
16 Loro sorelle furono: Zeruià e Abigàil. Figli di Zeruià furono Abisài, Ioab e Asaèl: tre.
Alongo awo anali Zeruya ndi Abigayeli. Ana atatu a Zeruya anali Abisai Yowabu ndi Asaheli.
17 Abigàil partorì Amasà, il cui padre fu Ieter l'Ismaelita.
Abigayeli anali amayi ake a Amasa amene abambo ake anali Yeteri wa fuko la Ismaeli.
18 Caleb, figlio di Chezròn, dalla moglie Azubà ebbe Ieriòt. Questi sono i figli di lei: Ieser, Sobàb e Ardon.
Kalebe mwana wa Hezironi anabereka ana mwa Azuba mkazi wake (ndi mwa Yerioti). Ana a mkaziyo anali awa: Yeseri, Sobabu ndi Aridoni.
19 Morta Azubà, Caleb prese in moglie Efrat, che gli partorì Cur.
Azuba atamwalira, Kalebe anakwatira Efurata, amene anamuberekera Huri.
20 Cur generò Uri; Uri generò Bezaleèl.
Huri anabereka Uri ndipo Uri anabereka Bezaleli.
21 Dopo Chezròn si unì alla figlia di Machir, padre di Gàlaad; egli la sposò a sessant'anni ed essa gli partorì Segùb.
Patapita nthawi, Hezironi anagona ndi mwana wamkazi wa Makiri abambo ake a Giliyadi (iye anamukwatira ali ndi zaka 60) ndipo anamuberekera Segubu.
22 Segùb generò Iair, cui appartennero ventitrè città nella regione di Gàlaad.
Segubu anabereka Yairi, amene anali ndi mizinda 23 ku Giliyadi.
23 Ghesur e Aram presero loro i villaggi di Iair con Kenat e le dipendenze: sessanta città. Tutti questi furono figli di Machir, padre di Gàlaad.
(Koma Gesuri ndi Aramu analanda Havoti Yairi komanso Kenati ndi madera ake onse ozungulira, mizinda makumi asanu ndi umodzi). Onsewa anali adzukulu, a Makiri abambo ake a Giliyadi.
24 Dopo la morte di Chezròn, Caleb si unì a Efrata, moglie di suo padre Chezròn, la quale gli partorì Ascùr, padre di Tekòa.
Atamwalira Hezironi ku Kalebe Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anamuberekera Asihuri abambo a Tekowa.
25 I figli di Ieracmèl, primogenito di Chezròn, furono Ram il primogenito, Buna, Oren, Achia.
Ana a Yerahimeeli, mwana woyamba wa Hezironi anali: Ramu, mwana wake woyamba, Buna, Oreni, Ozemu ndi Ahiya.
26 Ieracmèl ebbe una seconda moglie che si chiamava Atara e fu madre di Onam.
Yerahimeeli anali ndi mkazi wina amene dzina lake linali Atara, amene anali amayi a Onamu.
27 I figli di Ram, primogenita di Ieracmèl, furono Maas, Iamin ed Eker.
Ana a Ramu, mwana woyamba wa Yerahimeeli, anali awa: Maazi, Yamini ndi Ekeri.
28 I figli di Onam furono Sammài e Iada. Figli di Sammài: Nadàb e Abisùr.
Ana a Onamu anali awa: Shamai ndi Yada. Ana a Shamai anali awa: Nadabu ndi Abisuri.
29 La moglie di Abisùr si chiamava Abiàil e gli partorì Acbàn e Molìd.
Mkazi wa Abisuri anali Abihaili, amene anamuberekera Ahibani ndi Molidi.
30 Figli di Nadàb furono Seled ed Efraim. Seled morì senza figli.
Ana a Nadabu anali awa: Seledi ndi Apaimu. Koma Seledi anamwalira wopanda ana.
31 Figli di Efraim: Isèi; figli di Isèi: Sesan; figli di Sesan: Aclài.
Ana a Apaimu anali awa: Isi, amene anabereka Sesani. Sesani anabereka Ahilai.
32 Figli di Iada, fratello di Sammài: Ieter e Giònata. Ieter morì senza figli.
Ana a Yada, mʼbale wa Samai, anali awa: Yereri ndi Yonatani. Koma Yeteri anamwalira wopanda ana.
33 Figli di Giònata: Pelet e Zaza. Questi furono i discendenti di Ieracmèl.
Ana a Yonatani anali awa: Peleti ndi Zaza. Amenewa anali adzukulu a Yerahimeeli.
34 Sesan non ebbe figli, ma solo figlie; egli aveva uno schiavo egiziano chiamato Iarcà.
Sesani sanabereke ana aamuna koma aakazi okhaokha. Iye anali ndi wantchito wa ku Igupto, dzina lake Yariha.
35 Sesan diede in moglie allo schiavo Iarcà una figlia, che gli partorì Attài.
Sesani anapereka mwana wake wamkazi kwa Yariha wantchito wake kuti amukwatire ndipo anamuberekera Atayi.
36 Attài generò Natàn; Natàn generò Zabad;
Atayi anali abambo ake a Natani, Natani anali abambo ake a Zabadi,
37 Zabad generò Eflal; Eflal generò Obed;
Zabadi anali abambo a Efilali, Efilali anali abambo a Obedi,
38 Obed generò Ieu; Ieu generò Azaria;
Obedi anali abambo a Yehu, Yehu anali abambo a Azariya,
39 Azaria generò Chelez; Chelez generò Eleasà;
Azariya anali abambo a Helezi, Helezi anali abambo a Eleasa,
40 Eleasà generò Sismài; Sismài generò Sallùm;
Eleasa anali abambo ake a Sisimai, Sisimai anali abambo a Salumu,
41 Sallùm generò Iekamià; Iekamià generò Elisamà.
Salumu anali abambo a Yekamiya, Yekamiya anali abambo a Elisama.
42 Figli di Caleb, fratello di Ieracmèl, furono Mesa, suo primogenito, che fu padre di Zif; il figlio di Maresà fu padre di Ebron.
Ana a Kalebe mʼbale wa Yerahimeeli anali awa: Mesa mwana wachisamba, anali abambo a Zifi, ndipo mwana wake Maresa anali abambo a Hebroni.
43 Figli di Ebron: Core, Tappùach, Rekem e Samài.
Ana a Hebroni anali awa: Kora, Tapuwa, Rekemu ndi Sema.
44 Samài generò Ràcam, padre di Iorkoàm; Rekem generò Sammài.
Sema anali abambo ake Rahamu ndipo Rahamu anali abambo a Yorikeamu. Rekemu anali abambo a Samai.
45 Figlio di Sammài: Maòn, che fu padre di Bet-Zur.
Mwana wa Samai anali Maoni, ndipo Maoni anali abambo a Beti Zuri.
46 Efa, concubina di Caleb, partorì Caràn, Moza e Gazez; Caran generò Gazez.
Efai, mzikazi wa Kalebe, anali amayi a Harani, Moza ndi Gazezi. Harani anali abambo a Gazezi.
47 Figli di Iadài: Reghem, Iotam, Ghesan, Pelet, Efa e Saàf.
Ana a Yahidai anali awa: Regemu, Yotamu, Gesani, Peleti, Efai ndi Saafi.
48 Maaca, concubina di Caleb, partorì Seber e Tircanà;
Maaka mzikazi wa Kalebe anali mayi Seberi ndi Tirihana.
49 partorì anche Saàf, padre di Madmannà, e Seva, padre di Macbenà e padre di Gàbaa. Figlia di Caleb fu Acsa.
Iye anaberekanso Saafi abambo a Madimena ndi Seva abambo a Makibena ndi Gibeya. Mwana wamkazi wa Kalebe anali Akisa.
50 Questi furono i figli di Caleb. Ben-Cur, primogenito di Efrata, Sobal, padre di Kiriat-Iearìm,
Izi zinali zidzukulu za Kalebe. Ana a Huri mwana wachisamba wa Efurata anali awa: Sobala abambo a Kiriati Yearimu,
51 Salma, padre di Betlemme, Haref, padre di Bet-Gader.
Salima abambo a Betelehemu ndi Harefu abambo ake a Beti-Gadera.
52 Sobal, padre di Kiriat-Iearìm, ebbe come figli Reaia, Cazi e Manacàt.
Zidzukulu za Sobala abambo a Kiriati Yearimu zinali izi: Harowe, theka la banja la Manahati,
53 Le famiglie di Kiriat-Iearìm sono quelle di Ieter, di Put, di Suma e di Masra. Da costoro derivarono quelli di Zorea e di Estaòl.
ndipo mabanja a Kiriati-Yeyarimu anali awa: Aitiri, Aputi, Asumati ndi Amisirai. Azorati ndi Aesitaoli anachokera kwa amenewa.
54 Figli di Salma: Betlemme, i Netofatiti, Atarot-Bet-Ioab e metà dei Manactei e degli Zoreatei.
Zidzukulu za Salima zinali izi: Betelehemu, Anetofati, Atiroti-Beti-Yowabu, theka la banja la Manahati, Azori,
55 Le famiglie degli scribi che abitavano in Iabèz: i Tireatei, Simeatei e i Sucatei. Questi erano Keniti, discendenti da Cammat della famiglia di Recàb.
ndiponso mabanja a alembi amene amakhala ku Yabesi: Atiroti, Asimeati ndiponso Asukati. Awa ndi Akeni amene anachokera kwa Hamati, kholo la Arekabu.

< 1 Cronache 2 >