< Mazmur 94 >

1 Ya Allah, Engkaulah Allah yang membalas, tunjukkanlah pembalasan-Mu, ya TUHAN.
Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
2 Bangkitlah, ya Hakim seluruh bumi, hukumlah orang congkak setimpal perbuatan mereka.
Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
3 Ya TUHAN, sampai kapan orang jahat bergembira? Sampai kapan, ya TUHAN?
Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
4 Mereka melontarkan kata-kata yang kasar, dan menyombongkan kejahatan mereka.
Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
5 Mereka menindas umat-Mu, ya TUHAN, dan meremukkan orang-orang pilihan-Mu.
Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
6 Mereka membunuh janda dan yatim piatu dan orang asing yang tinggal di negeri ini.
Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
7 Kata mereka, "TUHAN tidak melihatnya, Allah Yakub tidak memperhatikannya."
Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
8 Hai bangsaku, janganlah sebodoh itu, belajarlah memakai akalmu!
Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
9 Allah yang membuat telinga, apakah Ia tidak mendengar? Dia yang membuat mata, apakah Ia tidak melihat?
Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
10 Dia yang mengajar bangsa-bangsa, apakah Ia tidak menghukum? Dia yang menjadi guru semua orang, apakah Ia tidak mempunyai pengetahuan?
Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
11 TUHAN menyelami pikiran manusia, Ia tahu semuanya sia-sia belaka.
Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
12 Berbahagialah orang yang Kaudidik, ya TUHAN, orang yang Kauajari hukum-hukum-Mu.
Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
13 Kautenangkan dia di hari-hari malapetaka, sampai digali lubang untuk menangkap orang jahat.
mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
14 Sebab TUHAN tak akan meninggalkan umat-Nya; Ia tak akan mengabaikan milik pusaka-Nya.
Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
15 Maka hukum akan ditegakkan lagi di pengadilan, semua orang jujur akan mendukungnya.
Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
16 Siapa membela aku terhadap orang durhaka? Siapa memihak aku melawan orang yang berbuat jahat?
Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
17 Sekiranya TUHAN tidak menolong aku, aku nyaris pindah ke dunia orang mati.
Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
18 Waktu aku berpikir bahwa aku akan jatuh, kasih-Mu, TUHAN, membuat aku berdiri kukuh.
Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
19 Apabila hatiku cemas dan gelisah, Engkau menghibur dan menggembirakan aku.
Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
20 Engkau tidak bersekutu dengan hakim-hakim jahat, yang merancangkan kejahatan berdasarkan hukum.
Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
21 Mereka bersekongkol melawan orang jujur, dan menghukum mati orang yang tak bersalah.
Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
22 Tetapi TUHAN adalah pembelaku, Allahku menjadi pelindungku.
Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
23 Ia menghukum orang jahat setimpal kejahatannya, dan membungkamkan mereka karena dosanya. TUHAN Allah kita akan membungkamkan mereka.
Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.

< Mazmur 94 >