< Mazmur 71 >
1 Pada-Mu aku berlindung, ya TUHAN, jangan biarkan aku dipermalukan.
Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
2 Bebaskanlah aku, sebab Engkau adil, dengarlah dan selamatkan aku.
Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
3 Jadilah bagiku seperti gunung batu tempat aku berdiam, yang mudah kucapai selalu. Sebab Engkau telah memutuskan untuk menyelamatkan aku, Engkaulah tempat aku berlindung dan bernaung.
Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
4 Ya Allahku, luputkanlah aku dari orang jahat, dari kuasa orang-orang lalim dan kejam.
Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
5 Sebab Engkaulah harapanku, ya TUHAN, TUHAN, aku percaya kepada-Mu sejak masa mudaku.
Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
6 Selama hidupku aku bertopang pada-Mu; Engkau melindungi aku sejak aku lahir maka aku selalu memuji Engkau.
Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
7 Hidupku menjadi teladan bagi orang banyak, sebab Engkaulah pelindungku yang kuat.
Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
8 Aku selalu memuji Engkau, sepanjang hari kuwartakan keagungan-Mu.
Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
9 Janganlah Kaubuang aku di masa tuaku jangan tinggalkan aku bila kekuatanku sudah habis,
Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
10 sebab musuh-musuhku membicarakan aku, orang-orang yang mau membunuh aku berkomplot.
Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
11 Kata mereka, "Dia sudah ditinggalkan Allah; mari kita kejar dan kita tangkap dia, sebab tak ada yang menyelamatkan dia."
Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
12 Jangan Engkau jauh dari aku, ya Allah, Allahku, tolonglah aku segera.
Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
13 Biarlah orang yang menyerang aku dipermalukan dan dilenyapkan. Biarlah orang yang mau mencelakakan aku kebingungan dan diliputi kehinaan.
Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
14 Tapi aku selalu berharap pada-Mu, dan semakin banyak memuji Engkau.
Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
15 Sepanjang hari akan kukisahkan perbuatan-perbuatan-Mu yang adil, dan keselamatan daripada-Mu yang tak terhitung.
Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
16 Kupuji perbuatan-Mu yang perkasa, ya TUHAN Allah, kumasyhurkan keadilan-Mu, keadilan-Mu saja.
Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
17 Ya Allah, Engkau mengajar aku sejak masa mudaku, sampai sekarang kukisahkan karya-Mu yang menakjubkan.
Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
18 Ya Allah, jangan meninggalkan aku, sampai aku tua dan beruban, supaya aku mewartakan kuasa dan keperkasaan-Mu kepada semua keturunan yang akan datang.
Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
19 Ya Allah, keadilan-Mu setinggi langit; besarlah perbuatan-perbuatan-Mu; siapa dapat menyamai Engkau?
Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
20 Engkau memberi aku banyak penderitaan yang berat, tetapi Engkau akan memulihkan tenagaku dan membangkitkan aku dari kuburan.
Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
21 Engkau akan membuat aku lebih terhormat, dan menghibur aku lagi.
Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
22 Aku hendak memuji Engkau dengan gambus, sebab Engkau setia, ya Allahku. Aku mau menyanyikan pujian bagi-Mu dengan kecapi, ya Allah kudus Israel.
Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
23 Aku bersorak dengan penuh sukacita, sambil menyanyikan pujian bagi-Mu. Jiwa ragaku menyanyi dengan ria, sebab Engkau telah menyelamatkan aku.
Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
24 Sepanjang hari akan kuwartakan keadilan-Mu, sebab orang-orang yang mau mencelakakan aku sudah dikalahkan dan dipermalukan.
Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.