< Mazmur 34 >
1 Mazmur Daud, ketika ia pura-pura tidak waras pikirannya di depan Abimelekh, sehingga ia diusir lalu pergi. Aku hendak bersyukur kepada TUHAN setiap waktu, dan tak henti-hentinya memuji Dia.
Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka. Ndidzayamika Yehova nthawi zonse; matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.
2 Aku hendak bermegah-megah karena perbuatan TUHAN; semoga orang tertindas mendengarnya dan bergembira.
Moyo wanga udzanyadira Yehova; anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.
3 Agungkanlah TUHAN bersamaku, mari bersama-sama memuliakan nama-Nya.
Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine; tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.
4 Aku berdoa kepada TUHAN, dan Ia menjawab, dan melepaskan aku dari segala ketakutan.
Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha; anandilanditsa ku mantha anga onse.
5 Orang tertindas berharap kepada-Nya dan bergembira, mereka tidak mempunyai alasan untuk menjadi malu.
Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira; nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.
6 Orang malang berseru dan TUHAN menjawabnya, membebaskan dia dari segala kesesakannya.
Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva; Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.
7 Malaikat TUHAN menjagai orang yang takwa, dan membebaskan mereka dari bahaya.
Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye ndi kuwalanditsa.
8 Rasakanlah sendiri betapa baiknya TUHAN, berbahagialah orang yang berlindung pada-Nya.
Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino; wodala munthu amene amathawira kwa Iye.
9 Hormatilah TUHAN, hai kamu umat-Nya, sebab orang takwa tak akan berkekurangan.
Wopani Yehova inu oyera mtima ake, pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.
10 Singa-singa pun lapar karena kurang makanan; tapi orang yang menyembah TUHAN tidak berkekurangan.
Mikango itha kulefuka ndi kumva njala koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.
11 Dengarlah, hai anak-anak sekalian, kuajari kamu menghormati TUHAN.
Bwerani ana anga, mundimvere; ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.
12 Inginkah kamu panjang umur dan menikmati yang baik?
Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13 Jangan mengeluarkan kata-kata jahat, dan jangan suka akan tipu muslihat.
asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14 Jauhilah yang jahat, lakukanlah yang baik, usahakanlah perdamaian dengan sekuat tenaga.
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
15 TUHAN memperhatikan orang saleh, Ia mendengar bila mereka berteriak minta tolong.
Maso a Yehova ali pa olungama ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;
16 Tetapi orang yang berbuat jahat ditentang-Nya; kalau mereka mati, mereka lekas dilupakan.
nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa, kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.
17 Bila orang saleh berseru, TUHAN mendengarkan, dan menyelamatkan mereka dari segala kesesakan.
Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva; Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.
18 TUHAN dekat pada orang yang berkecil hati; Ia menyelamatkan orang yang patah semangat.
Yehova ali pafupi kwa osweka mtima ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.
19 Banyaklah penderitaan orang baik, tetapi TUHAN membebaskan dia dari semuanya.
Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri, Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,
20 Tubuhnya tetap dijaga TUHAN, dari tulangnya tak satu pun dipatahkan.
Iye amateteza mafupa ake onse, palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.
21 Orang jahat akan mati karena kejahatannya, orang yang membenci orang saleh akan dihukum.
Choyipa chidzapha anthu oyipa; adani a olungama adzapezeka olakwa.
22 TUHAN menyelamatkan hamba-hamba-Nya; yang berlindung pada-Nya tak akan dihukum.
Yehova amawombola atumiki ake; aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.