< Mazmur 31 >
1 Untuk pemimpin kor. Mazmur Daud. Pada-Mu aku berlindung ya TUHAN, jangan biarkan aku dikecewakan. Selamatkanlah aku demi keadilan-Mu
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo; musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi; mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.
2 dengarlah aku dan bebaskanlah aku segera. Jadilah bagiku seperti gunung batu tempat aku berlindung, seperti benteng yang kuat, di mana aku selamat.
Tcherani khutu lanu kwa ine, bwerani msanga kudzandilanditsa; mukhale thanthwe langa lothawirapo, linga lolimba kundipulumutsa ine.
3 Ya, Engkau seperti gunung batu dan benteng yang kuat bagiku! Bimbinglah aku sesuai dengan janji-Mu.
Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa, chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.
4 Lepaskanlah aku dari jerat yang dipasang bagiku, sebab Engkaulah tempat aku berlindung.
Ndimasuleni mu msampha umene anditchera pakuti ndinu pothawirapo panga.
5 Ke dalam tangan-Mu kuserahkan diriku; Engkau membebaskan aku, ya TUHAN, Allah yang setia.
Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga; womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.
6 Orang yang menyembah berhala Kaubenci; tetapi aku percaya kepada TUHAN.
Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe; ine ndimadalira Yehova.
7 Aku akan bergembira dan bersukaria sebab Engkau tetap mengasihi aku. Engkau melihat penderitaanku dan memperhatikan kesusahanku.
Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu popeza Inu munaona masautso anga ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.
8 Engkau tidak membiarkan aku ditawan musuh, tetapi memungkinkan aku berjalan dengan bebas.
Inu simunandipereke kwa mdani koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.
9 Kasihanilah aku, ya TUHAN, sebab aku dalam kesusahan; mataku pedih karena menangis, jiwa ragaku merana.
Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto; maso anga akulefuka ndi chisoni, mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.
10 Hidupku habis dalam penderitaan, tahun-tahunku berlalu dalam keluh kesah. Kekuatanku berkurang karena kejahatanku, bahkan tulang-tulangku menjadi rapuh.
Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula; mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso, ndipo mafupa anga akulefuka.
11 Aku menjadi tertawaan bagi semua musuhku, bahkan bagi para tetanggaku. Semua kenalanku terkejut bila melihat aku, mereka lari bila bertemu dengan aku di jalan.
Chifukwa cha adani anga onse, ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga; ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga. Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.
12 Aku dilupakan seperti orang mati, dan menjadi seperti barang yang dibuang.
Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira; ndakhala ngati mʼphika wosweka.
13 Di mana-mana ada kengerian; kudengar desas-desus musuhku. Mereka bersekongkol melawan aku, dan membuat rencana untuk membunuh aku.
Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri; zoopsa zandizungulira mbali zonse; iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane, kuti atenge moyo wanga.
14 Tetapi aku berharap pada-Mu, ya TUHAN, sebab Engkaulah Allahku.
Koma ndikudalira Inu Yehova; ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”
15 Engkau selalu memelihara aku; selamatkanlah aku dari musuh-musuhku, dan dari orang-orang yang mengejar aku.
Masiku anga ali mʼmanja mwanu; ndipulumutseni kwa adani anga ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.
16 Semoga Engkau berkenan kepada hamba-Mu; selamatkanlah aku karena kasih-Mu.
Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu; pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.
17 Jangan biarkan aku mendapat malu, ya TUHAN, sebab aku berseru kepada-Mu. Biarlah orang jahat dipermalukan, dan dengan diam turun ke dunia orang mati. (Sheol )
Yehova musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndalirira kwa Inu; koma oyipa achititsidwe manyazi ndipo agone chete mʼmanda. (Sheol )
18 Sumbatlah mulut para pembohong yang dengan sombong mencemooh orang jujur.
Milomo yawo yabodzayo ikhale chete, pakuti chifukwa cha kunyada ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.
19 Betapa limpahnya kebaikan-Mu yang Kausediakan bagi orang takwa! Setiap orang melihat kebaikan yang Kaulakukan, bagi mereka yang berlindung pada-Mu.
Ndi waukulu ubwino wanu umene mwawasungira amene amakuopani, umene mumapereka anthu akuona kwa iwo amene amathawira kwa Inu.
20 Engkau menyembunyikan mereka dalam naungan-Mu terhadap siasat orang jahat; Kaujagai mereka dalam perlindungan-Mu terhadap tuduhan lawan.
Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa, kuwateteza ku ziwembu za anthu; mʼmalo anu okhalamo mumawateteza kwa anthu owatsutsa.
21 Terpujilah TUHAN! Sangat mengagumkan kasih-Nya bagiku, waktu aku dikepung dan diserang.
Matamando akhale kwa Yehova, pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.
22 Dalam kebingunganku aku menyangka TUHAN telah membuang aku dari hadirat-Nya. Tetapi Ia telah mendengar permohonanku waktu aku berseru kepada-Nya.
Ndili mʼnkhawa zanga ndinati, “Ine ndachotsedwa pamaso panu!” Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.
23 Cintailah TUHAN, hai seluruh umat-Nya, TUHAN melindungi orang yang setia. Tetapi orang congkak dihukum-Nya dengan tidak tanggung-tanggung.
Kondani Yehova oyera mtima ake onse! Yehova amasunga wokhulupirika koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.
24 Kuatkanlah dan teguhkan hatimu, kamu semua yang berharap kepada TUHAN!
Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima, inu nonse amene mumayembekezera Yehova.