< Yeremia 42 >
1 Setelah itu semua orang, besar kecil, bersama perwira-perwira, termasuk Yohanan anak Kareah dan Azarya anak Hosaya datang
Atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi Yohanani mwana wa Kareya ndi Azariya mwana wa Hosayia, ndiponso anthu onse, ana ndi akuluakulu omwe, anapita
2 kepadaku dan berkata, "Pak, seperti yang Bapak lihat sendiri, kami ini dulu banyak, sekarang tinggal sedikit saja. Kami mohon Bapak mau berdoa untuk kami kepada TUHAN Allah yang Bapak sembah. Doakanlah kami yang masih tersisa ini,
kwa mneneri Yeremiya ndipo anamuwuza kuti, “Chonde imvani dandawulo lathu ndipo mutipempherere anthu otsalafe kwa Yehova Mulungu wanu. Pakuti monga tsopano mukuona, ngakhale kuti kale tinalipo ambiri, koma tsopano ochepa okha ndiye amene atsala.
3 supaya TUHAN Allah menunjukkan kepada kami ke mana kami harus pergi dan apa yang harus kami lakukan."
Mupemphere kuti Yehova Mulungu wanu atiwuze kumene tiyenera kupita ndi chimene tiyenera kuchita.”
4 Aku menjawab, "Baiklah kalau begitu. Aku menerima permintaanmu itu. Aku akan berdoa kepada TUHAN Allah kita, dan apa pun jawaban-Nya, akan kuberitahukan semuanya; satu pun tidak akan kusembunyikan daripadamu."
Mneneri Yeremiya anawayankha kuti, “Ndamva zimene mwanenazi. Ndithu ndidzapemphera kwa Yehova Mulungu wanu monga momwe mwandipemphera. Ndidzakuwuzani chilichonse chimene Yehova anene ndipo sindidzakubisirani kanthu kalikonse.”
5 Mereka berkata kepadaku, "Kami minta Bapak berdoa kepada TUHAN Allah kita, karena kami mau taat kepada-Nya, supaya keadaan kami menjadi baik. Jadi, baik atau buruk pesan TUHAN itu, kami akan menurutinya. Biarlah TUHAN menjadi saksi yang jujur dan setia terhadap kami, apabila kami tidak menuruti semua perintah yang TUHAN berikan kepada kami melalui Bapak."
Ndipo iwo anawuza Yeremiya kuti, “Yehova akhale mboni yoona ndi yokhulupirika yodzatitsutsa ife ngati sitichita mogwirizana ndi chilichonse chimene Yehova Mulungu adzakutumani kuti mutiwuze.
Kaya ndi zotikomera kapena zosatikomera, ife tidzamvera Yehova Mulungu wathu, amene takutumaniko. Tidzamvera Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zidzatiyendere bwino.”
7 Sepuluh hari kemudian TUHAN berbicara kepadaku.
Patapita masiku khumi, Yehova anayankhula ndi Yeremiya.
8 Maka aku memanggil Yohanan serta perwira-perwiranya dan semua orang lain yang datang bersama dengan dia.
Choncho Yeremiya anayitana Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye ndiponso anthu onse, ana ndi akulu omwe.
9 Aku berkata kepada mereka, "Kamu menyuruh aku menyampaikan permohonanmu kepada TUHAN, Allah Israel. Nah, TUHAN berkata,
Yehova, Mulungu wa Israeli amene munanditumako kuti ndikapereke madandawulo mʼdzina lanu akuti,
10 'Kalau kamu mau tetap tinggal di negeri ini, Aku akan mengangkat kamu, bukan menjatuhkan; Aku akan menegakkan kamu, bukan meruntuhkan. Aku sedih sekali karena telah mendatangkan celaka ke atasmu.
“Ngati mukhala mʼdziko muno, ndiye kuti ndidzakukhazikitsani, osakuchotsani. Inde ndidzakudzalani osakuchotsani pakuti ndi kumva chisoni kwambiri chifukwa cha mavuto amene ndabweretsa pa inu.
11 Jangan lagi takut kepada raja Babel itu. Aku ada di tengah-tengahmu untuk menolong dan melepaskan kamu dari kekuasaannya.
Musayiope mfumu ya ku Babuloni, imene mukuyiopa tsopano. Musachite nayo mantha, akutero Yehova, pakuti Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani ndi kukulanditsani mʼmanja mwake.
12 Karena Aku berbelaskasihan kepadamu, Aku akan membuat raja Babel mengasihani kamu dan mengizinkan kamu pulang. Aku, TUHAN, telah berbicara.'"
Ndidzakuchitirani chifundo, ndipo mfumuyonso idzakuchitirani chifundo ndi kukulolani kuti mukhale mʼdziko mwanumwanu.
13 Tapi kamu yang masih tinggal di Yehuda janganlah membangkang kepada TUHAN Allahmu dan jangan berkata, "Kami tidak mau tinggal di negeri ini. Kami mau pergi ke Mesir dan tinggal di negeri itu. Di sana kami tidak lagi mengalami peperangan, tidak mendengar bunyi trompet yang memanggil untuk bertempur, dan tidak juga menderita kelaparan." Kalau kamu berkeras hati untuk pergi ke Mesir dan tinggal di sana, inilah pesan TUHAN Yang Mahakuasa, Allah Israel, bagimu:
“Koma mwina simudzamvera Yehova Mulungu wanu nʼkumanena kuti, ‘Ayi ife sitidzakhala mʼdziko muno,
ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’
Tsono, inu otsala a ku Yuda, imvani mawu a Yehova. Iye akuti, ngati mutsimikiza zopita ku Igupto, nʼkupitadi kukakhala kumeneko,
16 "Peperangan dan kelaparan yang kamu takuti itu akan mengejar kamu sampai ke Mesir, dan kamu akan mati di negeri itu.
ndiye nkhondo imene mukuyiopayo idzakugonjetsani ku Igupto komweko. Njala imene mukuyiopayo idzakupezani ku Igupto komweko ndipo mudzafera kumeneko.
17 Semua orang yang berkeras untuk pergi ke Mesir dan tinggal di sana akan mati dalam peperangan, atau mati karena kelaparan atau wabah penyakit. Tidak seorang pun akan luput dari bencana yang akan Kudatangkan ke atas mereka; semuanya akan mati.
Kunena zoona, onse amene atsimikiza zopita ku Igupto kuti akakhale kumeneko adzafa ndi nkhondo njala ndi mliri. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzapulumuke kapena kuthawa mavuto amene ndidzawagwetsera.’
18 Sebagaimana Aku, TUHAN Allah Israel menumpahkan kemarahan dan kegeraman-Ku ke atas penduduk Yerusalem, begitu pula akan Kutumpahkan kegeraman-Ku ke atas kamu yang pergi ke Mesir. Orang akan ngeri melihat kamu; kamu akan dihina, dan namamu akan dipakai sebagai kutukan. Kamu tidak akan melihat tanah airmu ini lagi."
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Momwe ndinawakwiyira mwaukali anthu okhala mu Yerusalemu, koteronso ndidzakukwiyirani mukapita ku Igupto. Mudzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, choseketsa ndi chonyozeka. Malo ano simudzawaonanso.’
19 Lalu aku berkata lagi, "TUHAN sudah memerintahkan supaya kamu yang masih tersisa di Yehuda tidak pergi ke Mesir. Karena itu aku memperingatkan kamu sekarang
“Inu otsala a ku Yuda, Yehova wakuwuzani kuti, ‘Musapite ku Igupto.’ Dziwani chinthu ichi: Ine lero ndikukuchenjezani
20 bahwa kamu telah membuat suatu kesalahan besar. Kamu minta supaya aku berdoa kepada TUHAN Allah kita untuk kamu, dan kamu berjanji untuk melaksanakan semua yang dikatakan oleh TUHAN.
kuti munalakwitsa kwambiri. Inu munandituma kwa Yehova Mulungu wanu nʼkumati ‘Mukatipempherere kwa Yehova Mulungu wathu, nʼkudzatiwuza chimene afuna kuti tichite, ndipo ife tidzachita.’
21 Sekarang aku sudah menyampaikan pesan TUHAN Allah kita kepadamu, tapi kamu tidak mau menuruti pesan itu.
Ine lero ndakuwuzani, koma inu simukumverabe zonse zimene Yehova Mulungu anandituma kuti ndikuwuzeni.
22 Sebab itu, ingatlah: di negeri yang kamu ingin datangi untuk menetap itu, kamu akan mati dalam peperangan, atau karena kelaparan atau wabah penyakit."
Tsono dziwani ichi: mudzafadi ndi nkhondo, njala ndi mliri kumalo kumene mukufuna mukakhaleko.”