< Yesaya 66 >

1 TUHAN berkata, "Langit adalah takhta-Ku, dan bumi tumpuan kaki-Ku. Jadi rumah macam apakah hendak kaubangun untuk-Ku, dan tempat apakah hendak kaujadikan kediaman-Ku?
Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
2 Alam semesta adalah buatan tangan-Ku, maka semua itu dijadikan. Tetapi kesukaan-Ku ialah orang yang rendah hati, yang menyesali dosa-dosanya, yang takut dan taat kepada-Ku.
Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
3 Tetapi bangsa itu berbuat semau mereka; mereka senang beribadah dengan cara yang menjijikkan. Bagi mereka tak ada bedanya: mengurbankan sapi jantan dan mengurbankan manusia, mengurbankan anak domba dan mematahkan leher anjing; mempersembahkan gandum dan mengurbankan darah babi, membakar kemenyan dan menyembah patung.
Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
4 Sebab itu Aku pun akan berbuat semau-Ku dan menimpakan atas mereka bencana-bencana yang mereka takuti. Sebab ketika Aku memanggil, tak ada yang menjawab; ketika Aku berbicara, tak ada yang mendengarkan. Mereka lebih suka melawan Aku dan melakukan yang jahat."
Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
5 Dengarlah apa yang dikatakan TUHAN, hai kamu yang takut dan taat kepada-Nya, "Karena kamu setia kepada-Ku, ada di antara bangsamu yang membenci kamu, dan tak mau bergaul dengan kamu. Mereka memperolok-olok kamu dengan berkata, 'Biarlah TUHAN menunjukkan keagungan-Nya, supaya kami melihat kegembiraanmu.' Tetapi mereka sendirilah yang mendapat malu.
Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
6 Dengar! Ada bunyi gemuruh di kota; ada suara dari Rumah-Ku; itulah suara-Ku yang sedang membalas musuh!
Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
7 Kota suci-Ku seperti seorang ibu yang melahirkan sebelum menggeliat sakit; yang melahirkan anak laki-laki sebelum merasakan sakit beranak.
“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
8 Siapa pernah mendengar hal seperti itu? Siapa pernah melihat kejadian semacam itu? Tetapi bangsa Israel sudah lahir pada saat Sion mulai merasakan sakit beranak.
Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
9 Jangan menyangka Aku membawa umat-Ku sampai saat kelahiran dan tidak membiarkan mereka dilahirkan." Begitulah kata TUHAN.
Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
10 Bersukacitalah bersama Yerusalem, hai semua orang yang mencintainya. Kamu yang berduka karena dia, sekarang boleh bergembira ria.
“Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
11 Kamu akan menikmati kemakmurannya, seperti seorang anak menyusu pada ibunya.
Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
12 Sebab TUHAN berkata, "Kamu akan Kuberi kesejahteraan seperti sungai yang mengalir; kekayaan bangsa-bangsa akan dibawa kepadamu seperti sungai yang meluap-luap. Kamu seperti anak yang disusui dan digendong ibunya, serta dibelai-belai di pangkuannya.
Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
13 Aku akan menghibur kamu di Yerusalem, seperti seorang ibu menghibur anaknya.
Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
14 Melihat itu, kamu akan bergembira, dan menjadi kuat dan sehat seperti rumput muda. Maka hamba-hamba-Ku akan mengalami kekuasaan-Ku dan musuh-musuh-Ku akan merasakan kemarahan-Ku."
Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
15 Sungguh, TUHAN akan datang dengan api; Ia akan mengendarai kereta-Nya seperti badai, untuk melampiaskan kemarahan-Nya, dan menghardik dengan keras.
Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
16 Sebab semua orang yang kedapatan bersalah akan dihukum-Nya dengan api dan pedang, dan banyaklah yang dihukum mati.
Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
17 TUHAN berkata, "Semua orang yang menyucikan diri untuk berarak ke kebun-kebun untuk dewa-dewa dan beribadah kepada mereka, akan lenyap bersama orang-orang yang makan daging babi dan tikus serta makanan lain yang menjijikkan.
Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
18 Aku mengetahui pikiran dan perbuatan mereka. Aku datang untuk menghimpun orang-orang dari segala bangsa. Pada waktu mereka berkumpul, mereka akan melihat kuasa-Ku.
“Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
19 Aku akan menempatkan sebuah tanda di tengah-tengah mereka. Sebagian kecil di antara mereka akan Kuselamatkan. Mereka akan Kuutus kepada bangsa-bangsa di negeri-negeri jauh yang belum pernah mendengar tentang Aku atau melihat keagungan dan kuasa-Ku: ke Spanyol, Libia, dan Lidia dengan pemanah-pemanahnya yang cakap, ke Tubal dan Yunani. Mereka akan mewartakan kebesaran-Ku di antara bangsa-bangsa itu.
“Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
20 Dari negeri-negeri itu mereka akan membawa kembali saudara-saudaramu sebangsa sebagai hadiah untuk-Ku. Mereka akan membawa orang-orang itu ke bukit-Ku yang suci di Yerusalem dengan mengendarai kuda, keledai dan unta, dan dengan kereta serta pedati, seperti lazimnya orang Israel membawa ke Rumah TUHAN persembahan gandum dalam wadah yang bersih.
Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
21 Sebagian di antara mereka akan Kujadikan imam dan orang Lewi.
Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
22 Seperti langit baru dan bumi baru akan bertahan karena kuasa-Ku, begitu juga keturunanmu dan namamu akan tinggal tetap.
“Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
23 Setiap Bulan Baru dan setiap hari Sabat seluruh umat manusia akan datang untuk menyembah Aku di Yerusalem.
“Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
24 Waktu berangkat, mereka akan melihat mayat orang-orang yang telah berontak terhadap-Ku. Ulat yang memakan bangkai mereka tak akan mati, dan api yang membakar mereka tak akan padam; suatu pemandangan yang mengerikan bagi semua orang."
“Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”

< Yesaya 66 >