< Yesaya 13 >

1 Inilah pesan Allah, yang diterima Yesaya anak Amos tentang Babel:
Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:
2 Kibarkanlah panji-panji perang di puncak bukit yang gundul! Berserulah kepada para prajurit, dan acungkan lenganmu supaya mereka menyerbu pintu-pintu gerbang kota yang congkak itu.
Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see, muwafuwulire ankhondo; muwakodole kuti adzalowe pa zipata za anthu olemekezeka.
3 TUHAN telah memanggil pejuang-pejuang pilihan-Nya. Mereka perkasa, percaya diri dan dapat Ia banggakan. TUHAN menugaskan mereka untuk menghukum orang-orang yang kena kemarahan-Nya.
Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga; ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira amene amadzikuza ndi chipambano changa.
4 Dengarlah bunyi gaduh di pegunungan, seperti bunyi kumpulan orang yang sangat banyak. Dengarlah keributan kerajaan-kerajaan dan bangsa-bangsa yang sedang berkumpul. TUHAN Yang Mahakuasa memeriksa pasukan perang.
Tamvani phokoso ku mapiri, likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu! Tamvani phokoso pakati pa maufumu, ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi! Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera kuchita nkhondo.
5 Mereka datang dari negeri-negeri jauh di ujung-ujung bumi. Dalam kemarahan-Nya TUHAN memakai mereka untuk membinasakan seluruh bumi.
Iwo akuchokera ku mayiko akutali, kuchokera kumalekezero a dziko Yehova ali ndi zida zake za nkhondo kuti adzawononge dziko la Babuloni.
6 Merataplah, sebab hari TUHAN sudah dekat, yaitu hari kebinasaan yang didatangkan TUHAN Yang Mahakuasa.
Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
7 Setiap orang akan merasa lumpuh tangannya dan kehilangan keberaniannya.
Zimenezi zinafowoketsa manja onse, mtima wa munthu aliyense udzachokamo.
8 Mereka semua akan ditimpa ketakutan hebat, dan menggeliat kesakitan seperti wanita yang sedang bersalin. Mereka akan saling memandang dengan cemas, mukanya merah karena malu.
Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu, zowawa ndi masautso zidzawagwera; adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka. Adzayangʼanana mwamantha, nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.
9 Hari TUHAN akan datang, dan pada hari itu TUHAN melampiaskan kemarahan-Nya dan murka-Nya yang hebat. Bumi akan menjadi padang tandus, dan setiap orang berdosa akan binasa.
Taonani, tsiku la Yehova likubwera, tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo; kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.
10 Setiap bintang dan gugusan bintang akan berhenti bersinar; matahari akan gelap pada saat ia terbit, dan bulan tak akan bercahaya lagi.
Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga sizidzaonetsa kuwala kwawo. Dzuwa lidzada potuluka, ndipo mwezi sudzawala konse.
11 TUHAN berkata, "Aku akan menghukum dunia karena kejahatannya, dan orang-orang jahat karena dosa-dosa mereka. Setiap orang congkak akan Kurendahkan, orang angkuh dan kejam akan Kuhukum.
Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake, anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo. Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza, ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.
12 Orang yang diselamatkan sedikit sekali, mereka lebih jarang dari emas murni.
Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino. Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.
13 Aku akan membuat langit gemetar dan bumi bergoncang dari tempatnya pada hari Aku, TUHAN Yang Mahakuasa, menunjukkan kemarahan-Ku.
Tsono ndidzagwedeza miyamba ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake. Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.
14 Orang asing yang tinggal di Babel akan tercerai-berai dan lari ke negerinya masing-masing. Mereka seperti rusa yang melarikan diri dari pemburu, atau kawanan domba yang tidak mempunyai gembala.
Ngati mbawala zosakidwa, ngati nkhosa zopanda wozikusa, munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo, aliyense adzathawira ku dziko lake.
15 Siapa saja yang tertangkap akan ditikam sampai mati.
Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa adzaphedwa momubaya ndi lupanga.
16 Mereka akan menyaksikan bayi-bayi mereka diremukkan, rumah-rumah mereka dirampok dan istri-istri mereka diperkosa."
Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona; nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.
17 TUHAN berkata, "Aku menggerakkan bangsa Madai untuk menyerang Babel. Mereka tidak bisa disuap dengan perak atau emas.
Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva ndipo sasangalatsidwa ndi golide, kuti amenyane ndi Ababuloni.
18 Dengan busur dan panahnya mereka akan membunuh orang-orang muda. Mereka tidak sayang kepada bayi dan tidak kasihan kepada anak.
Adzapha anyamata ndi mauta awo; sadzachitira chifundo ana ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.
19 Dari semua kerajaan, Babel itu yang paling indah dan menjadi kebanggaan penduduknya. Tetapi Aku, TUHAN, akan menghancurkannya, seperti sudah Kulakukan terhadap Sodom dan Gomora.
Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse. Anthu ake amawunyadira. Koma Yehova adzawuwononga ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.
20 Tak seorang pun akan tinggal lagi di sana. Tak ada orang Arab pengembara yang akan memasang kemahnya di tempat itu, dan tak ada gembala yang akan membawa kambing dombanya untuk merumput di situ.
Anthu sadzakhalamonso kapena kukhazikikamo pa mibado yonse; palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake, palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.
21 Tempat itu akan didiami binatang-binatang liar. Burung hantu akan bersarang di rumah-rumah mereka, dan burung unta akan tinggal di sana. Kambing-kambing liar akan berjingkrak-jingkrak di antara reruntuhan.
Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko, nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe; mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi, ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.
22 Raungan anjing hutan dan serigala akan bergema dari puri-puri dan istana-istana Babel. Saat kehancurannya sudah hampir tiba dan waktunya tidak ditunda lagi."
Mu nsanja zake muzidzalira afisi, mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe. Nthawi yake yayandikira ndipo masiku ake ali pafupi kutha.

< Yesaya 13 >