< Yehezkiel 35 >

1 TUHAN berkata kepadaku,
Yehova anandiyankhula kuti:
2 "Hai manusia fana, kutukilah negeri Edom.
“Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
3 Sampaikanlah kepada penduduknya apa yang Aku TUHAN Yang Mahatinggi katakan kepada mereka, 'Aku ini musuhmu, hai penduduk pegunungan Edom! Tanahmu akan Kujadikan sunyi sepi tanpa penghuni, dan kota-kotamu akan menjadi puing-puing. Maka tahulah kamu bahwa Akulah TUHAN.
awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
4
Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
5 Sejak dahulu kamu memusuhi Israel dan membiarkan mereka dibantai pada waktu mereka ditimpa bencana sebagai hukuman terakhir atas dosa mereka.
“Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
6 Oleh karena itu, demi Aku, Allah yang hidup, TUHAN Yang Mahatinggi, maut adalah nasibmu, dan kamu tidak dapat lolos daripadanya. Kamu telah bersalah sebab melakukan pembunuhan, maka pembunuhan pun akan mengejarmu.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
7 Kota-kotamu di pegunungan Edom akan Kujadikan sepi dan setiap orang yang melintasinya akan Kubunuh.
Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
8 Gunung-gunung akan Kututupi dengan mayat-mayatmu, bukit dan lembah akan Kupenuhi dengan korban pertempuran.
Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
9 Negerimu akan Kujadikan padang belantara untuk selama-lamanya, dan kota-kotamu tak akan lagi didiami orang. Maka tahulah kamu bahwa Akulah TUHAN.
Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
10 Kamu mengatakan bahwa baik Yehuda maupun Israel dengan tanahnya masing-masing adalah hakmu, dan bahwa kamu akan memilikinya meskipun Aku, TUHAN, adalah Allah mereka.
“Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
11 Sebab itu, demi Aku, Allah yang hidup, TUHAN Yang Mahatinggi, Aku akan membalas dendam kepadamu, karena kamu marah, cemburu dan benci kepada umat-Ku. Mereka akan tahu bahwa kamu Kuhukum karena perbuatanmu terhadap mereka.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
12 Maka tahulah kamu bahwa Aku, TUHAN, telah mendengar ejekanmu waktu kamu berkata: Gunung-gunung Israel sudah menjadi sunyi sepi dan diserahkan menjadi mangsa kita.
Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
13 Hai bangsa Edom, kamu besar mulut dan berbicara dengan sombong kepada-Ku. Aku telah mendengar semua itu.
Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
14 Aku TUHAN Yang Mahatinggi berkata: Seluruh dunia akan senang pada waktu seluruh negerimu Kujadikan padang yang sunyi sepi,
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
15 sama seperti kamu pun senang waktu melihat Israel milik-Ku, menjadi sunyi sepi. Gunung-gunung Seir, bahkan seluruh tanah Edom akan menjadi sunyi sepi. Maka semua orang akan tahu bahwa Akulah TUHAN.'"
Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Yehezkiel 35 >