< Ulangan 29 >
1 Inilah kata-kata perjanjian yang atas perintah TUHAN dibuat Musa dengan bangsa Israel waktu mereka berada di tanah Moab. Perjanjian itu merupakan tambahan dari perjanjian yang dibuat TUHAN dengan mereka di Gunung Sinai.
Awa ndiwo mawu a mʼpangano limene Yehova analamula Mose kuti achite ndi Aisraeli ku Mowabu, powonjezera pa pangano limene anapangana nawo ku Horebu.
2 Musa menyuruh semua orang Israel berkumpul, lalu berkata kepada mereka, "Kamu sudah melihat sendiri apa yang dilakukan TUHAN terhadap raja Mesir, para pejabatnya dan seluruh negerinya.
Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati kwa iwo: Inu munaona zonse zimene Yehova anachita kwa Farao, nduna zake ndi dziko lake lonse ku Igupto.
3 Kamu juga sudah melihat bencana-bencana yang dahsyat, mujizat-mujizat dan keajaiban-keajaiban yang dilakukan TUHAN.
Ndi maso anu munaona mayesero onse aja, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zazikulu zija.
4 Tetapi sampai hari ini Ia belum memungkinkan kamu mengerti semua yang kamu alami itu.
Koma mpaka lero Yehova sanakupatseni mtima wozindikira kapena maso openya kapena makutu akumva.
5 Empat puluh tahun lamanya TUHAN memimpin kamu melalui padang gurun, namun pakaian dan sandalmu tidak menjadi usang.
Mʼzaka makumi anayi zimene ndinakutsogolerani mʼchipululu, zovala zanu ndiponso nsapato za ku mapazi anu sizinangʼambike.
6 Kamu tidak mempunyai roti untuk makanan, air anggur atau minuman keras, tetapi TUHAN memberi segala yang kamu perlukan supaya kamu tahu bahwa Dialah TUHAN Allahmu.
Inu simunadye buledi ndi kumwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa. Ndinachita izi kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
7 Dan ketika kita sampai di tempat ini, Raja Sihon dari Hesybon dan Raja Og dari Basan datang memerangi kita. Tetapi kita kalahkan mereka.
Pamene munafika malo ano, Sihoni mfumu ya ku Hesiboni ndi Ogi mfumu ya ku Basani anabwera kudzamenyana nafe koma tinawagonjetsa iwo.
8 Tanah mereka kita rebut dan kita bagikan kepada suku Ruben, Gad dan sebagian suku Manasye.
Tinatenga dziko lawo ndi kulipereka ngati cholowa cha fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase.
9 Maka hendaklah kamu setia mentaati seluruh perjanjian ini, supaya kamu berhasil dalam segala usahamu.
Tsatirani mosamalitsa mawu a mʼpangano ili kuti zinthu zizikuyenderani bwino pa zochitika zanu zonse.
10 Hari ini kamu semua berdiri di hadapan TUHAN Allahmu, semua kepala suku, pemuka, perwira, semua laki-laki,
Lero lino nonse mukuyima pamaso pa Yehova Mulungu wanu, atsogoleri a mafuko anu, akuluakulu ndi nduna zanu, ndi amuna ena onse a mu Israeli,
11 wanita, anak-anak, dan semua orang asing yang tinggal di antara kamu dan membantu kamu memotong kayu dan memikul air.
pamodzi ndi ana ndi akazi anu, kudzanso alendo amene akukhala pakati panu omwe amakuwazirani nkhuni ndi kukutungirani madzi.
12 TUHAN Allahmu membuat perjanjian dengan kamu, dan kamu semua berkumpul di sini untuk mengikat perjanjian itu serta menerima kewajiban-kewajibannya.
Mukuyimirira pano kuti mulowe mʼpangano ndi Yehova Mulungu wanu, pangano limene Yehova akuchita ndi inu lero ndi kulisindikiza ndi malumbiro,
13 Dengan perjanjian itu TUHAN hari ini mengukuhkan kamu menjadi bangsa-Nya, dan Ia menjadi Allahmu seperti yang dijanjikan-Nya kepadamu dan kepada nenek moyangmu Abraham, Ishak dan Yakub.
kukukhazikitsani lero lino ngati anthu ake, ndi kuti Iye akhale Mulungu wanu monga anakulonjezani inu ndiponso monga analumbira kwa makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
14 Perjanjian itu dengan segala kewajibannya dibuat TUHAN bukan dengan kamu saja,
Ndikupanga pangano ili ndi malumbiro ake osati kwa inu nokha,
15 tetapi dengan setiap orang yang pada hari ini berdiri di sini, di hadapan TUHAN Allah kita, dan juga dengan keturunan kita di masa depan."
amene muli pano pamaso pa Yehova Mulungu wathu, koma ndi iwonso amene sali pano lero.
16 "Kamu masih ingat bagaimana nasib kita di Mesir dan bagaimana kita berjalan melalui negeri bangsa-bangsa lain.
Inu nomwe mukudziwa mmene tinkakhalira ku Igupto ndi mmene tinadutsira mayiko pa ulendo wobwera kuno.
17 Kamu sudah melihat patung-patung berhala mereka yang menjijikkan dari kayu, batu, perak dan emas.
Ife tinaona pakati pawo mafanizo ndi mafano awo onyansa, amtengo ndi amiyala, asiliva ndi agolide.
18 Jadi jagalah jangan sampai seorang pun di antara kamu, laki-laki atau perempuan, keluarga atau suku yang berdiri di sini, berbalik dari TUHAN Allah kita untuk menyembah ilah-ilah bangsa lain. Perbuatan itu seperti akar yang tumbuh menjadi tanaman pahit dan beracun.
Onetsetsani kuti pasapezeke mwamuna kapena mkazi, banja kapena fuko pakati panu lero amene mtima wawo udzapandukira Yehova Mulungu wanu ndi kupita kukapembedza milungu ya mitundu iyo. Onetsetsani kuti pasapezeke muzu pakati panu wotulutsa mankhwala akupha otere.
19 Di antara kamu yang mendengar tuntutan yang keras itu janganlah ada yang berpikir bahwa nasibnya akan tetap baik, sekalipun ia dengan nekat mengikuti jalannya sendiri. Hal itu akan membinasakan kamu semua, orang-orang yang jahat maupun yang baik.
Munthu wotere akamva mawu a lumbiro ili, asadzidalitse yekha mʼmaganizo mwake namati, “Ine ndidzapulumuka ngakhale nditapitiriza kuyenda njira yanga.” Zoterezi zidzadzetsa masautso pa nthaka ya chinyontho ndi yowuma yomwe.
20 TUHAN tidak akan mengampuni orang seperti itu. Sebaliknya, dia akan kena kemarahan TUHAN yang meluap-luap, dan segala bencana yang tertulis di dalam buku ini akan menimpa dia, sampai ia dibinasakan TUHAN.
Yehova sadzamukhululukira. Mkwiyo ndi nsanje ya Yehova zidzamuyakira munthuyo. Matemberero onse wolembedwa mʼbukuli adzamugwera iye ndipo Yehova adzafafaniza dzina lake pa dziko lapansi.
21 TUHAN akan menjadikan dia sebuah contoh untuk semua suku Israel, dan menghukum dia dengan kutuk yang disebut dalam perjanjian yang tertulis di dalam buku ini, buku Hukum TUHAN.
Yehova adzasankha pakati pa Aisraeli anthu oyenera masautso monga mwa matemberero onse a mʼpangano olembedwa Mʼbuku la Malamulo.
22 Di kemudian hari, keturunanmu dan orang asing dari negeri jauh akan melihat bencana-bencana dan penderitaan yang didatangkan TUHAN atas negerimu.
Ana anu a mibado yakutsogolo ndi alendo amene adzachokera kutali adzaona matsoka amene adzakugwerani mʼdziko muno ndiponso matenda amene Yehova adzabweretsa pa dzikoli.
23 Ladang-ladangmu akan menjadi padang tandus tertutup belerang dan garam. Tanahnya tak dapat ditanami dan rumput tak mau tumbuh di situ. Negerimu akan menyerupai kota-kota Sodom dan Gomora, Adma dan Zeboim yang dimusnahkan TUHAN ketika kemarahan-Nya berkobar-kobar.
Dziko lonse lidzasanduka nthaka ya mchere ndi ya sulufule. Simudzadzalamo kanthu, simudzakhala chomera chilichonse, ndi mbewu yomera mʼmenemo. Dziko lanu lidzakhala lowonongeka ngati Sodomu ndi Gomora, Adima ndi Zeboimu, mizinda imene Yehova anayiwononga ndi mkwiyo wake waukulu.
24 Maka seluruh dunia akan bertanya, 'Mengapa TUHAN berbuat begitu dengan negeri mereka? Apa sebab Ia marah sehebat itu?'
Mitundu yonse ya anthu idzafunsa kuti, “Kodi chifukwa chiyani Yehova anachita zotere mʼdziko lake? Kodi chifukwa chiyani anaonetsa mkwiyo woopsa wotere?”
25 Dan jawabnya ialah, 'Karena mereka mengingkari perjanjian TUHAN, Allah nenek moyang mereka; perjanjian yang dibuat-Nya dengan mereka pada waktu Ia membawa mereka keluar dari Mesir.
Ndipo yankho la mafunso amenewa lidzakhala lakuti, “Chifukwa chakuti anthu awa aphwanya pangano la Yehova Mulungu wa makolo awo, pangano limene Iye anapangana nawo pamene anawatulutsa ku Igupto.
26 Mereka mengabdi kepada ilah-ilah lain yang tidak mereka kenal, padahal TUHAN melarang mereka menyembah ilah-ilah itu.
Iwo anachoka ndi kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, milungu imene sanayidziwe, milungu imene sanawapatse.
27 Itulah sebabnya TUHAN marah kepada umat-Nya dan mendatangkan atas negeri mereka semua bencana yang tertulis di dalam buku ini.
Choncho Yehova anakwiyira dziko lino, kotero anabweretsa matemberero onse amene analembedwa mʼbuku lino.
28 Kemarahan TUHAN meledak dengan hebatnya, dan dalam kemarahan-Nya yang besar Ia mencabut bangsa Israel dari tanah mereka dan melemparkan mereka ke negeri asing sehingga mereka ada di sana.'
Ndi mkwiyo komanso ukali wake woopsa Yehova anawazula mʼdziko lawo ndi kuwaponyera mʼdziko lina, monga mmene zilili lero lino.”
29 Ada beberapa hal yang dirahasiakan TUHAN Allah kita; tetapi hukum-Nya telah dinyatakan-Nya kepada kita, dan kita serta keturunan kita harus mentaatinya untuk selama-lamanya."
Zinsinsi ndi za Yehova Mulungu wathu koma zinthu zimene zaululidwa ndi zathu ndi ana athu kwamuyaya, kuti titsatire mawu onse a mʼmalamulowa.