< 1 Tawarikh 22 >

1 Maka kata Daud, "Di tempat inilah harus dibangun Rumah TUHAN Allah. Dan di mezbah inilah orang Israel harus mempersembahkan kurban bakaran mereka kepada TUHAN."
Ndipo Davide anati, “Nyumba ya Yehova Mulungu idzakhala pano, ndiponso guwa lansembe zopsereza za Israeli.”
2 Raja Daud menyuruh mengumpulkan semua orang asing yang tinggal di negeri Israel, lalu ia mempekerjakan mereka. Sebagian dari mereka memahat batu untuk membangun Rumah TUHAN.
Choncho Davide analamula kuti asonkhanitse alendo onse amene amakhala mu Israeli ndipo kuchokera pakati pawo anasankha amisiri a miyala kuti aseme miyala yomangira nyumba ya Mulungu.
3 Untuk membuat paku dan engsel bagi pintu-pintu gerbang Rumah TUHAN itu, Daud mengumpulkan banyak sekali besi. Ia juga mengumpulkan begitu banyak perunggu, sehingga tidak dapat ditimbang.
Ndipo anapereka zitsulo zambiri zopangira misomali ya zitseko za pa zipata ndi zolumikiza zake. Anaperekanso mkuwa wochuluka wokanika kuwuyeza.
4 Dari orang Tirus dan Sidon ia memesan sejumlah besar kayu cemara Libanon.
Iye anaperekanso mitengo yambiri ya mkungudza, yosawerengeka, pakuti anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo anabweretsa yambiri kwa Davide.
5 Daud melakukan semuanya itu karena ia berpikir begini: "Aku harus mempersiapkan apa yang diperlukan untuk pembangunan Rumah TUHAN. Sebab Salomo putraku masih muda dan kurang pengalaman, sedangkan Rumah TUHAN yang akan dibangunnya itu harus sangat megah dan termasyhur di seluruh dunia." Maka sebelum Daud meninggal, ia menyediakan banyak sekali bahan bangunan.
Davide anati, “Mwana wanga Solomoni ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Koma nyumba yomwe timangire Yehova iyenera kukhala yaulemerero, yotchuka ndi yokongola pamaso pa anthu a mitundu yonse. Choncho ndikonzekeratu zambiri.” Motero Davide anayikonzekera kwambiri asanamwalire.
6 Daud memanggil putranya, Salomo, dan memerintahkan dia untuk mendirikan rumah bagi TUHAN Allah yang disembah oleh umat Israel.
Tsono iye anayitana Solomoni mwana wake ndipo anamulamula kuti adzamangire nyumba Yehova Mulungu wa Israeli.
7 Kata Daud kepada Salomo, "Anakku, sudah lama aku berniat mendirikan sebuah rumah untuk menghormati TUHAN Allahku.
Davide anati kwa Solomoni, “Mwana wanga, ine ndinali ndi maganizo oti ndimangire nyumba Dzina la Yehova Mulungu wanga.
8 Tetapi TUHAN berkata bahwa aku terlalu sering bertempur dan telah membunuh banyak orang. Karena itu Ia tidak mengizinkan aku mendirikan rumah untuk Dia.
Koma Yehova anandiyankhula kuti, ‘Iwe wapha anthu ambiri ndiponso wachita nkhondo zambiri. Sumangira dzina langa nyumba chifukwa wapha anthu ambiri pa dziko lapansi pamaso panga.
9 Meskipun begitu, Ia telah memberikan kepadaku janji ini: 'Engkau akan mendapat seorang putra yang akan memerintah dengan tentram, sebab Aku akan menolong dia sehingga tak ada musuh yang memerangi dia. Ia akan dinamakan Salomo sebab selama ia memerintah, Aku akan memberikan ketentraman dan keamanan di seluruh Israel.
Koma udzabala mwana wamwamuna amene adzakhala munthu wamtendere ndi wabata ndipo ndidzamupatsa mpumulo kuchokera kwa adani ake onse a mbali zonse. Dzina lake adzatchedwa Solomoni ndipo Ine ndidzapereka mtendere ndi bata kwa Israeli pa nthawi ya ulamuliro wake.
10 Putramu itulah yang akan mendirikan rumah untuk-Ku. Dia akan menjadi anak-Ku dan Aku menjadi bapaknya. Takhta kerajaan Israel akan tetap pada keturunannya untuk selama-lamanya.'"
Iye ndiye adzandimangire nyumba. Adzakhala mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake. Ndipo ndidzakhazikitsa mpando wake waufumu mʼdziko la Israeli mpaka muyaya.’”
11 Lalu kata Daud lagi, "Sekarang, anakku, semoga TUHAN Allahmu selalu menolong engkau. Dan semoga engkau berhasil mendirikan rumah untuk TUHAN seperti yang telah dijanjikan-Nya.
“Tsopano mwana wanga, Yehova akhale nawe ndipo upambane ndi kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wako, monga momwe Iye ananenera kuti udzatero.
12 Dan mudah-mudahan TUHAN Allahmu memberikan kepadamu kebijaksanaan dan pengertian untuk memerintah Israel sesuai dengan hukum-hukum-Nya.
Yehova akupatse nzeru ndi kumvetsetsa pamene Iye adzakuyika kukhala wolamulira Israeli, kuti udzasunge malamulo a Yehova Mulungu wako.
13 Kalau engkau mentaati semua hukum yang diberikan TUHAN kepada Musa untuk bangsa Israel, engkau akan berhasil. Engkau harus yakin dan berani. Jangan takut menghadapi apa pun juga.
Ndipo udzapambana ngati udzamvera mosamala malangizo ndi malamulo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kudzera mwa Mose. Khala wamphamvu ndi wolimba mtima. Usachite mantha kapena kutaya mtima.
14 Mengenai Rumah TUHAN itu aku sudah berusaha sungguh-sungguh untuk mengumpulkan 3.400 ton emas dan lebih dari 34.000 ton perak. Selain itu ada perunggu dan besi yang tidak terhitung banyaknya. Kayu dan batu pun sudah kusiapkan, tetapi engkau harus menambahkannya lagi.
“Ine movutikira kwambiri ndapereka ku Nyumba ya Mulungu matani 3,400 agolide, matani 34,000 asiliva, ndiponso mkuwa ndi chitsulo, matabwa ndi miyala. Ndipo iwe utha kuwonjezerapo pa zimenezi.
15 Engkau mempunyai banyak pekerja. Ada yang dapat bekerja di tambang batu, ada tukang kayu, tukang batu dan banyak sekali pengrajin yang pandai mengerjakan
Iwe uli ndi antchito ambiri: osema miyala, amisiri a miyala, ndi amisiri a matabwa, komanso anthu ambiri aluso la ntchito zosiyanasiyana,
16 emas, perak, perunggu dan besi. Nah, mulailah segera! Semoga TUHAN menolong engkau."
zagolide ndi zasiliva, zamkuwa, zazitsulo, amisiri osawerengeka. Tsopano yamba ntchito, ndipo Yehova akhale nawe.”
17 Lalu Daud menyuruh semua pemimpin Israel membantu Salomo.
Tsono Davide analamula atsogoleri onse a Israeli kuti athandize Solomoni mwana wake.
18 Katanya, "TUHAN Allahmu sudah menolong kalian, dan memberi damai serta ketentraman di seluruh negeri. Ia sudah memungkinkan aku mengalahkan semua bangsa yang dulu tinggal di negeri ini. Sekarang mereka takluk kepadamu dan kepada TUHAN.
Iye anawawuza kuti, “Kodi Yehova Mulungu, sali nanu? Ndipo Iye siwakupatsani mpumulo mbali zonse? Pakuti Iyeyo wapereka eni nthaka kwa inu ndipo dziko lili pa ulamuliro wa Yehova ndi anthu ake.
19 Jadi, hendaklah kalian mengabdi kepada TUHAN Allahmu dengan segenap jiwa ragamu. Mulailah membangun rumah untuk TUHAN, supaya Peti Perjanjian-Nya dan semua perkakas lain yang dipakai khusus untuk ibadat dapat ditempatkan di situ."
Tsono perekani mtima wanu ndi moyo wanu kufunafuna Yehova Mulungu wanu. Yambani kumanga malo opatulika a Yehova Mulungu, kuti mubweretse Bokosi la Chipangano la Yehova ndi zinthu zopatulika za Mulungu mʼNyumba ya Mulungu imene idzamangidwa chifukwa cha dzina la Yehova.”

< 1 Tawarikh 22 >