< Zacarias 1 >

1 Iti maikawalo a bulan iti maikadua a tawen a panagturay ni Dario, immay ti sao ni Yahweh kenni profeta Zacarias a putot ni Barakias a putot ni Iddo a kunana,
Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:
2 “Nakapungtot unay ni Yahweh kadagiti ammayo!
“Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.
3 Ibagam kadakuada, 'Kastoy ti kuna ni Yahweh a Mannakabalin-amin: “Agsublikayo kaniak!”—daytoy ket pakaammo ni Yahweh a Mannakabalin-amin!“—”ket agsubliak kadakayo!” kuna ni Yahweh a Mannakabalin-amin.
Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
4 Saanyo koma a tuladen dagiti ammayo nga imun-una a binagaan dagiti profeta, a kunada, “Kastoy ti kuna ni Yahweh a Mannakabalin-amin: isardengyon dagiti dakes a wagasyo ken dagiti nadangkes nga aramidyo!” Ngem saanda a dimngeg ken saandak nga impangag.”' Daytoy ket pakaammo ni Yahweh.
Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova.
5 “Saan kadi nga awanen dagiti ammayo? Ken agtalinaed kadi dagiti profeta iti agnanayon?
Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya?
6 Ngem saan kadi a sinagaba dagiti ammayo ti subad iti panagsukirda kadagiti sasaok ken paglintegak nga imbilinko kadagiti adipenko a profeta? Nagbabawida ngarud ket kinunada, 'Kas iti pinanggep ni Yahweh a Mannakabalin-amin nga aramiden kadatayo gapu kadagiti wagas ken tigtignaytayo, isu ti inaramidna kadatayo.'”
Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu? “Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’”
7 Iti maikadua a tawen a panagturay ni Dario, iti maika-dua pulo ket uppat nga aldaw iti maikasangapulo ket maysa a bulan, a bulan ti Sebat, immay ti sao ni Yahweh kenni profeta Zacarias a putot ni Barakias a putot ni Iddo a kunana
Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.
8 “Iti rabii, adtoy, nakitak ti maysa a lalaki a nakasakay iti nalabaga a kabalio, ket adda isuna kadagiti babassit a kayo nga addaan kadagiti napipintas a sabsabong nga adda iti tanap; ket adda iti likudanna dagiti nalabaga, alazan ken puraw a kabalio.”
Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.
9 Kinunak “Apo, ania dagitoy a banbanag?” Ket kinuna ti anghel a nakisarita kaniak, “Ipakitakto kenka no ania dagitoy a banbanag.”
Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?” Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”
10 Ket simmungbat ti lalaki a nakatakder iti ayan dagiti babassit a kayo nga addaan kadagiti napipintas a sabsabong a kunana, “Dagitoy dagiti imbaon ni Yahweh nga agsursor iti entero a daga.”
Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”
11 Simmungbatda iti anghel ni Yahweh a nakatakder iti ayan dagiti babassit a kayo nga addaan kadagiti napipintas a sabsabong; kinunada kenkuana, “Sursursorenmin ti entero a daga; kitaem, agal-aliwaksay dagiti amin a daga.”
Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”
12 Ket simmungbat ti anghel ni Yahweh a kunana, “O Yahweh a Mannakabalin-amin, kasano kadi pay kabayag ti panangipakitam iti saanmo a panangngaasi iti Jerusalem ken kadagiti siudad ti Juda a nagsagaba iti pungtotmo iti pitopulo a tawen?”
Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?”
13 Simmungbat ni Yahweh iti anghel a nakisararita kaniak babaen kadagiti nasasayaat a sasao, dagiti sasao a pangliwliwa.
Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.
14 Ket kinuna kaniak ti anghel a nakisarita kaniak, “Ipakaammom daytoy, 'Kastoy ti kuna ni Yahweh a Mannakabalin-amin: “Kasta unay ti pakaseknak iti Jerusalem ken iti Sion!
Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni,
15 Ket napalalo ti pungtotko kadagiti nasion a nanam-ay; ta saanak unay a nakaunget iti Juda, ngem kinarkaro dagitoy a nasion ti panagsagaba ti Juda.”
koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’
16 Ngarud, kastoy ti kuna ni Yahweh a Mannakabalin-amin: “Nagsubliak iti Jerusalem nga addaan iti asi. Maipatakderto ti balayko iti daytoy”'—daytoy ket pakaammo ni Yahweh a Mannakabalin-amin—”ket maibinnatto ti tali a pagrukod iti entero a Jerusalem!”
“Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
17 Ipakaammom pay daytoy, 'Kastoy ti kuna ni Yahweh a Mannakabalin- amin: 'Rumang-ayto manen dagiti siudadko, ket liwliwaento manen ni Yahweh ti Sion, ken piliennanto manen ti Jerusalem.”
“Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’”
18 Kalpasanna, timmangadak ket nakakitaak iti uppat a sara!
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi.
19 Kinasaritak ti anghel a nakisarita kaniak, “Ania dagitoy?” Insungbatna kaniak, “Dagitoy dagiti sara a nangiwarawara iti Juda, Israel, ken Jerusalem.”
Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?” Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”
20 Ket nangipakita kaniak ni Yahweh iti uppat a mammanday.
Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi.
21 Kinunak, “Ania ti umay aramiden dagitoy a tattao?” Insungbatna, “Dagitoy dagiti sara a nangiwarawara iti Juda, isu a nagsagabada iti nakaro. Ngem immay dagitoy a tattao tapno pagtalawen dagiti nasion, tapno parmekenda dagiti armada dagiti nasion a nangraut iti daga ti Juda tapno iwarawarada daytoy.”
Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?” Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”

< Zacarias 1 >