< Roma 5 >
1 Agsipud ta napalintegtayo babaen iti pammati, addaantayo iti kapia iti Dios babaen kenni Apotayo a Jesu-Cristo.
Tsopano popeza tayesedwa olungama mwa chikhulupiriro, tili ndi mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
2 Babaen kenkuana naaddaantayo met iti dalan babaen ti pammati iti daytoy a parabur a pagtaktakderantayo. Agrag-otayo iti talged nga it-ited ti Dios kadatayo para iti masakbayan, ti talged a pagraranudantayonto iti dayag ti Dios.
Iyeyo ndiye amene anatsekulira njira mwachikhulupiriro yolowera mʼchisomo mʼmene takhazikikamo. Ndipo tikukondwerera chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu.
3 Saan laeng a daytoy, ngem agragrag-otayo met kadagiti panagsagsagabatayo. Ammotayo a patauden ti panagsagsagaba iti panagibtur.
Koma si pokhapo ayi, koma ife tikukondweranso mʼmasautso athu chifukwa tikudziwa kuti masautso amatiphunzitsa kupirira.
4 Patauden iti panagibtur iti panaganamong, ken patauden iti panaganamong ti talged para iti masakbayan.
Ndipo kupirira kumabweretsa makhalidwe, makhalidwe amabweretsa chiyembekezo.
5 Saan a makaupay daytoy a kinatalged, gapu ta naibukbok iti ayat ti Dios kadagiti puspusotayo babaen iti Espiritu Santo, a naited kadatayo.
Ndipo chiyembekezo chimenechi sichitikhumudwitsa chifukwa Mulungu mwa Mzimu Woyera, amene Iye anatipatsa, wadzaza mʼmitima mwathu ndi chikondi chake.
6 Ta kabayatan a nakapuytayo latta, natay ni Cristo iti umno a tiempo para kadagiti saan a nadiosan.
Pakuti pa nthawi yake, tikanali ochimwa, Khristu anatifera anthu osapembedzafe.
7 Ta narigat para iti maysa a tao a matay para iti nalinteg a tao. Dayta ket, nalabit nga adda natured a matay para iti naimbag a tao.
Sizichitika kawirikawiri kuti munthu wina afere munthu wolungama, ngakhale kuti chifukwa cha munthu wabwino wina atha kulimba mtima kumufera.
8 Ngem panpaneknekan ti Dios ti bukodna nga ayat kadatayo, gapu ta bayat a managbasoltayo pay laeng, natay ni Cristo para kadatayo.
Koma Mulungu anaonetsa chikondi chake kwa ife chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu anatifera.
9 Ngarud, ad-adda pay ita a napalintegtayo babaen iti darana, maisalakantayo babaen iti daytoy manipud iti pungtot iti Dios.
Popeza chifukwa cha magazi ake ife tapezeka olungama pamaso pa Mulungu, Iyeyo adzatipulumutsa koposa kotani ku mkwiyo wa Mulungu.
10 Ta bayat a kabusornatayo iti Dios, nakikapiatayo iti Dios babaen iti pannakatay ti Anakna, ad-adda pay a kalpasan a nakikapiatayo, maisalakantayonto babaen iti biagna.
Pakuti pamene tinali adani a Mulungu, tinayanjanitsidwa ndi Iye kudzera mu imfa ya Mwana wake. Nanga tidzapulumutsidwa bwanji kudzera mʼmoyo wake, titayanjanitsidwa naye?
11 Saan laeng a daytoy, ngem agrag-otayo met iti Dios babaen kenni Apotayo a Jesu-Cristo, naawattayo ita babaen kenkuana daytoy a pannakaikapia.
Sikuti izi zili chomwechi chabe, koma timakondweranso mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Kudzera mwa Iye, ife tsopano tayanjanitsidwa ndi Mulungu.
12 Ngarud simrek ti basol iti lubong babaen iti maysa a tao, iti daytoy a wagas simrek ti patay babaen iti basol. Ken nagsaknap ti patay iti amin a tattao, gapu ta nagbasol ti amin.
Choncho monga momwe tchimo linalowa mʼdziko lapansi kudzera mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzera mu tchimo, mʼnjirayi imfa inafika kwa anthu onse pakuti onse anachimwa.
13 Ta agingga nga adda iti linteg ket adda iti basol iti lubong, ngem awan maibilang a basol no awan iti linteg.
Pakuti Malamulo asanaperekedwe, tchimo linali mʼdziko lapansi. Koma pamene palibe Malamulo, tchimo silitengedwa kukhala tchimo.
14 Uray no kasta, nagari ti patay manipud kenni Adan agingga kenni Moises, uray kadagiti saan a nagbasol a kas iti panagsukir ni Adan, a kas kenkuana nga umayto.
Komabe, imfa inalamulira kuyambira nthawi ya Adamu mpaka nthawi ya Mose. Inalamulira ngakhalenso pa iwo amene sanachimwe posamvera Malamulo monga anachitira Adamu. Adamuyo amene anali chifaniziro cha wina amene ankabwera.
15 Ngem uray pay, ti sagut nga awan bayadna ket saan a kas iti panagsalungasing. Ta no ti nakatayan ti kaadduan ket gapu iti panagsalungasing ti maysa, ad-adda pay a nawadwad ti parabur ti Dios para iti kaadduan, ken ti sagut babaen iti parabur ti maysa a tao, a ni Jesu-Cristo, a nagsaknap iti kaadduan.
Koma sitingafananitse mphatso yaulereyo ndi kuchimwa kwa anthu. Pakuti ngati anthu ambiri anafa chifukwa cha kuchimwa kwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga chisomo cha Mulungu ndi mphatso zomwe zinabwera ndi chisomo cha munthu mmodzi, Yesu Khristu, ndi kusefukira kwa ambiri!
16 Ta iti sagut ket saan a kas iti nagbanagan ti nagbasol. Ta iti sabali a bangir, immay ti ukom iti pannakadusa gapu iti panagsalungasing ti maysa a tao. Ngem iti sabali nga bangir, immay ti awan bayadna a sagut a nagbanag iti pannakapalinteg kalpasan iti adu a panagsalungasing.
Ndiponso, mphatso ya Mulungu sifanana ndi zotsatira za kuchimwa kwa munthu mmodzi. Chiweruzo chinatsatira tchimo la munthu mmodzi ndi kubweretsa kutsutsidwa koma mphatso inatsatira zolakwa zambiri ndi kubweretsa kulungamitsidwa.
17 Ta no nagturay ti patay gapu iti panagsalungasing ti maysa, ad-addanto pay nga agturay dagiti umawat iti aglaplapusanan a parabur ken agturay ti sagut iti kinalinteg babaen ti biag iti maysa, a ni Jesu-Cristo.
Pakuti ngati, chifukwa cha kulakwa kwa munthu mmodziyo, imfa inalamulira kudzera mwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga kwa iwo amene adzalandira chisomo chochuluka ndi mphatso yachilungamo, adzalamulira mʼmoyo kudzera mwa munthu mmodzi, Yesu Khristu.
18 Iti pannakaiyeg ngarud iti pannusa iti amin a tattao ket gapu iti panagsalungasing ti maymaysa, kasta met immay ti pannakapalinteg iti biag iti amin a tattao babaen iti maysa a panagtignay iti kinalinteg.
Choncho monga tchimo limodzi linabweretsa kutsutsika pa anthu onse, chimodzimodzinso ntchito imodzi yolungama inabweretsa chilungamo kwa anthu onse ndi kuwapatsa moyo.
19 Ta iti saan a panagtulnog ti maysa a tao, adu dagiti nagbalin a managbasol, kasta met nga adunto ti mapalinteg babaen iti panagtulnog iti maysa.
Pakuti kusamvera kwa munthu mmodzi kunasandutsa anthu ambiri kukhala ochimwa, chimodzimodzinso anthu ambiri adzasanduka olungama kudzera mwa munthu mmodzinso.
20 Ngem immay ti linteg, tapno agsaknap koma ti panagsukir. Ngem iti nagsaknapan ti basol, ad-adda pay a nagsaknap iti parabur.
Malamulo a Mulungu anaperekedwa ndi cholinga chakuti anthu onse azindikire kuchuluka kwa machimo awo. Koma pamene machimo anachuluka, chisomo chinachuluka koposa.
21 Napasamak daytoy tapno kas panagturay ti basol iti patay, kasta met a mabalin nga agari uray ti parabur babaen iti kinalinteg a para iti agnanayon a biag babaen kenni Jesu- Cristo nga Apotayo. (aiōnios )
Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu. (aiōnios )