< Dagiti Salmo 9 >

1 Ayamanak kenni Yahweh iti amin a pusok; ibagak dagiti amin a nakakaskasdaaw nga aramidmo.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a nyimbo ya “Imfa ya Mwana.” Salimo la Davide. Ine ndidzakutamandani, Inu Yehova, ndi mtima wanga wonse; ndidzafotokoza za zodabwitsa zanu zonse.
2 Agragsak ken agrag-oak kenka; agkantaak iti panagdayaw iti naganmo, O Kangangatoan!
Ndidzakondwa ndi kusangalala mwa inu; Ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina lanu, Inu Wammwambamwamba.
3 No agsanud dagiti kabusorko, mapasag ken matayda iti sangoanam.
Adani anga amathawa, iwo amapunthwa ndi kuwonongedwa pamaso panu.
4 Ta inkanawam ti umno a kalintegak; agtugtugawka iti tronom, nalinteg nga ukom!
Pakuti Inu mwatsimikiza za kulungama kwanga ndi mlandu wanga; Inu mwakhala pa mpando wanu waufumu, kuweruza mwachilungamo.
5 Binutbutengmo dagiti nasion iti pukkawmo a pakigubat; dinadaelmo dagiti nadangkes; pinunasmo dagiti pakalaglagipanda iti agnanayon.
Mwadzudzula mitundu ya anthu ndipo mwawononga anthu oyipa; Inu mwafafaniza dzina lawo kwamuyaya.
6 Narebba ti kabusor a kasla kadagiti nadadael idi pinarmekmo dagiti siudadda. Napukaw amin a pakalaglagipanda.
Chiwonongeko chosatha chagwera adani, mwafafaniza mizinda yawo; ngakhale chikumbutso chawo chawonongedwa.
7 Ngem agtalinaed ni Yahweh iti agnanayon; isagsaganana ti tronona a mangukom.
Yehova akulamulira kwamuyaya; wakhazikitsa mpando wake waufumu woweruzira.
8 Uk-ukomenna ti lubong nga awan panangidumdumana. Nalinteg dagiti pangngeddengna para kadagiti nasion.
Iye adzaweruza dziko mwachilungamo; adzalamulira mitundu ya anthu mosakondera.
9 Ni Yahweh pay ti natalgedto a sarikedked dagiti maidaddadanes, natalged a sarikedked kadagiti tiempo ti riribuk.
Yehova ndiye kothawirako kwa opsinjika mtima, linga pa nthawi ya mavuto.
10 Agtaltalek kenka dagiti makaammo iti naganmo, ta sika O Yahweh, saanmo a baybay-an dagiti mangsapsapul kenka.
Iwo amene amadziwa dzina lanu adzadalira Inu, pakuti Inu Yehova, simunawatayepo amene amafunafuna inu.
11 Agkantakayo kadagiti pagdayaw kenni Yahweh, nga agturturay idiay Sion; ibagayo dagiti naaramidanna kadagiti nasion.
Imbani nyimbo zamatamando kwa Yehova, ali pa mpando waufumu mu Ziyoni; lengezani pakati pa mitundu ya anthu zimene wachita.
12 Ta ti Dios a mangibalbales iti panagsayasay ti dara ket mananglaglagip; saanna a malipatan ti sangit dagiti maidaddadanes.
Pakuti Iye amene amabwezera chilango akupha anzawo wakumbukira; Iye salekerera kulira kwa ozunzika.
13 Kaasiannak, O Yahweh; kitaem no kasano nga idaddadanesdak dagiti gumurgura kaniak, sika a makaisalakan kaniak manipud iti pannakatay.
Inu Yehova, onani momwe adani anga akundizunzira! Chitireni chifundo ndipo ndichotseni pa zipata za imfa,
14 O, tapno maipakaammok amin a pakaidaydayawam. Kadagiti ruangan iti anak a babai ti Sion, agrag-oak iti panangisalakanmo!
kuti ndilengeze za matamando anu pa zipata za ana aakazi a Ziyoni, kuti pamenepo ndikondwere ndi chipulumutso chanu.
15 Natnag dagiti nasion iti palab-og nga inaramidda; nasiloan dagiti sakada iti iket nga impakatda.
Mitundu ya anthu yagwa mʼdzenje limene yakumba; mapazi awo akodwa mu ukonde umene anawubisa.
16 Inyam-ammo ni Yahweh ti kinasiasinona; impatungpalna ti pannakaukom; nasiloan ti nadangkes babaen kadagiti bukodna nga aramid. (Selah)
Yehova amadziwika ndi chilungamo chake; oyipa akodwa ndi ntchito za manja awo. Higayoni. (Sela)
17 Timmallikud dagiti nadangkes ket naipanda idiay sheol, ti pagtungpalan dagiti amin a nasion a mangliplipat iti Dios. (Sheol h7585)
Oyipa amabwerera ku manda, mitundu yonse imene imayiwala Mulungu. (Sheol h7585)
18 Ta saan a kanayon a malipatan dagiti agkasapulan, wenno saan a kanayon a madadael dagiti namnama dagiti maidaddadanes.
Koma osowa sadzayiwalika nthawi zonse, kapena chiyembekezo cha ozunzika kutayika nthawi zonse.
19 Bumangonka, O Yahweh; saanmo nga ipalubos a parmekennakami ti tao; maukom koma dagiti nasion iti imatangmo.
Dzukani Inu Yehova, musalole munthu kuti apambane; mitundu yonse iweruzidwe pamaso panu.
20 Butbutngem ida, O Yahweh; maammoan koma dagiti nasion a tattaoda laeng. (Selah)
Akantheni ndi mantha aakulu, Inu Yehova; mitundu idziwe kuti iwo ndi anthu wamba. (Sela)

< Dagiti Salmo 9 >