< Dagiti Salmo 88 >
1 O Yahweh, Dios a manangisalakanko, umasugak kenka iti aldaw ken rabii.
Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara. Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa, usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.
2 Dumngegka iti kararagko; ipangagmo ti ararawko.
Pemphero langa lifike pamaso panu; tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.
3 Ta napnoanak kadagiti riribuk, ken dimmanonen ti biagko iti sheol. (Sheol )
Pakuti ndili ndi mavuto ambiri ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda. (Sheol )
4 Tratraoendak dagiti tattao a kas kadagiti bumaba iti abut; maysaak a tao nga awanan iti pigsa.
Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje; ndine munthu wopanda mphamvu.
5 Napanawanak iti denna dagiti natay, kaslaak la natay a nakaidda iti tanem, a saanmon a pakibibiangan gapu ta naisinadan manipud iti pannakabalinmo.
Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa, monga ophedwa amene agona mʼmanda, amene Inu simuwakumbukiranso, amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.
6 Inkabilnak iti kaunggan a paset ti abut, iti nasipnget ken nauneg a luglugar.
Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni, mʼmalo akuya a mdima waukulu.
7 Nadagsen a nakatupak kaniak ti pungtotmo, ken laplapunosendak dagiti amin a dalluyonmo. (Selah)
Ukali wanu ukundipsinja kwambiri, mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse. (Sela)
8 Gapu kenka, likliklikandak dagiti makaam-ammo kaniak. Pinagbalinnak a makapakigtot iti panagkitada. Napalawlawanak ket saanak a makalibas.
Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo. Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;
9 Nabannogen dagiti matak manipud iti riribuk; Agmalmalem nga umaw-awagak kenka, O Yahweh; inyunnatko dagiti imak kenka.
maso anga ada ndi chisoni. Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse; ndimakweza manja anga kwa Inu.
10 Mangaramidka kadi kadagiti nakakaskasdaaw para kadagiti natay? Bumangon ken agdayaw kadi dagiti natay kenka? (Selah)
Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa? Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu? (Sela)
11 Maiwaragawag kadi ti kinapudnom iti tulagmo idiay tanem, ti kinapudnom iti lugar dagiti natay?
Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda, za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?
12 Maipakaammo kadi dagiti nakakaskasdaaw nga aramidmo iti kasipngetan, wenno ti kinalintegmo iti lugar iti pannakalipat?
Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima, kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?
13 Ngem umawagak kenka, O Yahweh; dumanon ti kararagko kenka iti bigbigat.
Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo; mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.
14 O Yahweh, apay a laklaksidennak? Apay nga ilengedmo ti rupam kaniak?
Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana ndi kundibisira nkhope yanu?
15 Kankanayon ti pannakaparigat ken kaaddak iti ngarab ni patay sipud pay iti kinaagtutubok. Nagsagabaak manipud kadagiti pungtotmo; awan iti maaramidak.
Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa; ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.
16 Sinagabak dagiti naunget a tigtignaymo, ken dinadaeldak dagiti nakabutbuteng nga aramidmo.
Ukali wanu wandimiza; zoopsa zanu zandiwononga.
17 Liklikmutendak a kasla danum iti agmalmalem, pinalawlawandak amin.
Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula; zandimiza kwathunthu.
18 Inyadayom kaniak dagiti amin a gagayyemko ken dagiti am-ammok. Kinasipnget laeng ti kakaisuna a kaduak.
Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga; mdima ndiye bwenzi langa lenileni.