< Dagiti Salmo 71 >

1 Kenka O Yahweh, agkamangak; saanmo koma nga ipalubos a mapabpabainanak.
Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
2 Ispalennak ken pagbalinennak a natalged iti kinalintegmo; iyalingagmo ta lapayagmo kaniak ken isalakannak.
Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
3 Agbalinka kadi a kasla maysa a dakkel a bato nga agpaay a kamangko a kankanayon a mabalin papanak; nagitedka iti bilin a mangisalakan kaniak, ta sika ti kamang ken salinongko.
Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
4 Ispalennak, O Diosko, manipud iti ima dagiti nadangkes, manipud iti ima dagiti saan a nalinteg ken dagiti naranggas a tao.
Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
5 Ta sika ti namnamak, O Apo Yahweh. Nagtaltalekak kenka sipud pay ti kinaubingko.
Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
6 Babaen kenka, nasarsaranayak manipud iti tian ti inak; sika ti nangiruar kaniak manipud iti tian ti inak; ti panangidayawko ket kanayonto a maipanggep kenka.
Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
7 Maysaak a pagtuladan kadagiti adu a tattao; sika ti natibker a kamangko.
Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
8 Mapnonto ti ngiwatko iti panangidaydayaw kenka ken iti panangitan-ok kenka iti agmalmalem.
Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
9 Saannak nga ibelleng iti panawen ti kinalakayko; saannak a baybay-an inton agkapuyakon.
Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
10 Ta pagsasaritaandak dagiti kabusorko; sangsangkamaysa nga agplanplano dagiti mangsisiim iti biagko.
Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
11 Kunkunada, “Binaybay-an isunan ti Dios; darupen ken alaentayo isuna, ta awan ti mangisalakan kenkuana.”
Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
12 O Dios, saanka koma nga umadayo kaniak; O Diosko, darasem ti mangtulong kaniak.
Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
13 Maibabain ken maibusa koma, dagiti agpapanggep iti biagko; magaburanda koma iti pannakababalaw ken pannakaibaba, dagiti mangsapsapul iti pakasaktak.
Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
14 Ngem kanayonak latta a mangnamnama kenka ken ad-addanto a dayawenka.
Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
15 Agmalmalem nga ibaganto ti ngiwatko ti maipanggep iti kinalintegmo ken ti panangisalakanmo, uray pay saanko a maawatan daytoy.
Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
16 Mapanak kadakuada nga addaan kadagiti nabibileg nga aramid ni Yahweh nga Apo; saritaekto ti kinalintegmo, ti laeng kinalintegmo.
Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
17 O Dios, insuronak manipud kinaagtutubok; uray ita, iwarwaragawagko dagiti nakakaskasdaaw nga aramidmo.
Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
18 Kinapudnona, uray inton lakayak ken purawton ti buokko, O Dios, saannak a baybay-an, bayat iti panangiwarwaragawagko iti kinabilegmo iti sumaruno a henerasion, ti pannakabalinmo iti amin nga umay.
Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
19 Ti pay kinalintegmo O Dios, ket nangato unay; sika a nagaramid kadagiti naindaklan a banbanag, O Dios, siasino ti kas kenka?
Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
20 Sika a nangipakpakita kadakami iti adu a nakaro a pakariribukan ti mangpapigsa manen kadakami ken mangiyaon manen kadakami manipud iti kaunggan a paset ti daga.
Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
21 Ad-adda pay a kinatan-ok ti ipaaymo kaniak; tumaliawka manen ket liwliwaennak.
Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
22 Babaen iti arpa, pagyamanak ti kinamatalekmo, O Diosko; kantaanka iti kankanta a pagdaydayaw a mabuyogan iti arpa, O Santo ti Israel.
Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
23 Agpukkaw toy bibigko gapu iti rag-o inton agkantaak iti kankanta a pagdaydayaw kenka—uray siak a sinubbotmo.
Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
24 Agmalmalem met nga isao daytoy dilak ti maipanggep iti kinalintegmo; ta naibabain ken natikawda, dagiti nangsapul iti pannakapasakitko.
Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.

< Dagiti Salmo 71 >