< Dagiti Salmo 65 >

1 Kenka, O Dios iti Sion, agur-uray dagiti pammadayawmi kenka; ituloymi nga aramiden dagiti sapatami kenka.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo. Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni; kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
2 Sika a dumdumngeg iti kararag, umayto kenka amin a lasag.
Inu amene mumamva pemphero, kwa inu anthu onse adzafika.
3 A kasla ab-abakennakami dagiti basbasolmi; maipanggep met kadagiti panaglabsingmi, pakawanemto dagitoy.
Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo, Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
4 Nagasat ti tao a pinilim nga iyasideg kenka tapno agtalinaed iti santuariom. Mapnekkaminto iti kinaimbag ti balaymo, ti nasantoan a templom.
Odala iwo amene inu muwasankha ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu! Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu, za mʼNyumba yanu yoyera.
5 Sililinteg a sungbatannakami babaen iti panagaramidmo kadagiti nakaskasdaaw, Dios iti pannakaisalakanmi; sika a pagtalkan ti amin a suli ti daga ken dagiti adda iti ballasiw ti taaw.
Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo, Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
6 Ta sika iti nangpatibker kadagiti banbantay, sika a nabarikesan iti kinapigsa.
amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu, mutadziveka nokha ndi mphamvu.
7 Sika ti mangpapaulimek ti daranudor ti taaw, ti daranudor dagiti dalluyon, ken dagiti panagringgor dagiti tattao.
Amene munakhalitsa bata nyanja kukokoma kwa mafunde ake, ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
8 Dagiti agnanaed kadagiti nasulinek a paset ti daga ket mabuteng iti pammaneknek dagiti aramidmo; pagragsakem ti laud ken ti daya.
Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu; kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera. Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.
9 Umaymo tultulongan ti lubong; sibsibugam daytoy; kasta unay ti panangpabaknangmo iti daytoy; napno iti danum iti karayan ti Dios; ipapaaymo iti apit idi insaganam ti lubong.
Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira; Inuyo mumalilemeretsa kwambiri. Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi kuti upereke tirigu kwa anthu, pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
10 Sibsibugam a sibubuslon dagiti talon a naarado; isubsublim dagiti nagungap a ringringngat; palpaluknengem dagitoy babaen iti arbis; benbendisionam dagiti katubtubo a mula dagitoy.
Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake, mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
11 Kinoronaam ti tawen iti kinaimbagmo; iti sadinoman a papanam, adu iti napipintas nga apit.
Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka, ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
12 Nagtinnag daytoy iti pagpaspastoran iti let-ang, ken nabarekesan dagiti turturod iti rag-sak.
Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira; mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
13 Nakawesan dagiti pagpaspastoran kadagiti arban; namulaan met dagiti tanap kadagiti trigo; agpukpukkawda gapu iti ragsak, ken agkankantada.
Madambo akutidwa ndi zoweta ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu; izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.

< Dagiti Salmo 65 >