< Dagiti Salmo 55 >

1 Ipangagmo ti kararagko, O Dios, ken saanmo kadi nga ilemmengan ti ararawko.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe. Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,
2 Ipangagnak ket sungbatannak; awan ti inanak kadagiti pakariribukak
mverani ndipo mundiyankhe. Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
3 gapu kadagiti timek dagiti kabusorko, gapu iti panangparigat dagiti nadangkes; ta riribuk ti iyegda kaniak ket kapungtotdak.
chifukwa cha mawu a adani anga, chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa; pakuti andidzetsera masautso ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
4 Nasaktan unay ti pusok, ken nagtupak kaniak ti alliaw ni patay.
Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga; mantha a imfa andigwera.
5 Panagbuteng ken panagpigerger ti immay kaniak, ket linapunosnak ti buteng.
Mantha ndi kunjenjemera zandizinga; mantha aakulu andithetsa nzeru.
6 Kinunak, “O, no addaanak koma kadagiti payak a kasla iti kalapati! Ket makatayabak koma nga umadayo ken makainana.
Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda! Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
7 Kitaem, ket innak iti adayo a disso; agtalinaedak idiay let-ang. (Selah)
Ndikanathawira kutali ndi kukakhala mʼchipululu.
8 Agdardarasak a mapan iti panglinongan manipud iti napigsa nga angin ken bagio.”
Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo; kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
9 Dadaelem ida, O Apo, ket dimo pagkikinnaawaten ida, ta makitak ti kinaranggas ken riribuk iti siudad.
Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo; pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
10 Aldaw ken rabii, lawlawlawenda dagiti paderna; kinadakes ken riribuk ti adda iti tengngana.
Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake; nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
11 Adda ti kinadangkes iti tengngana; saan a pumanaw kadagiti kalsadana dagiti panangidadanes ken panangallilaw.
Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda; kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
12 No koma kabusor ti manglalais kaniak, maibturak; uray isuna a gimmura kaniak a nagpannakkel kaniak, mailemmengak.
Akanakhala mdani akundinyoza, ine ndikanapirira; akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane, ndikanakabisala.
13 Ngem sika, ti tao a kapadpadak, ti kaduak ken nasinged a gayyemko.
Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
14 Naaddaanta ti nasam-it a panaglinlinnangen; nagnata iti balay ti Dios agraman ti adu a tattao.
Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
15 Kellaat koma nga umay ni patay kadakuada; maipababada koma a sibibiag iti sheol, ta kinadangkes ti pagnanaedanda, iti mismo nga ayanda. (Sheol h7585)
Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol h7585)
16 No maipapan kaniak, umawagakto iti Dios, ket isalakannakto ni Yahweh.
Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu, ndipo Yehova anandipulumutsa.
17 Agdayengdeng ken umasugak iti rabii, bigat ken agmatuon; ipangagna ti timekko.
Madzulo, mmawa ndi masana ndimalira mowawidwa mtima, ndipo Iye amamva mawu anga.
18 Sitatalged nga ispalenna ti biagko manipud iti gubat a maibusor kaniak, ta adu dagiti bimmusor kaniak. (Selah)
Iye amandiwombola ine osavulazidwa pa nkhondo imene yafika kulimbana nane, ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
19 O Dios, a nagturay manipud iti un-unana, denggennakto ken parmekennanto ida. Saan nga agbalbaliw dagidiay a lallaki; saanda nga agbuteng iti Dios.
Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya, adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga, chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa ndipo saopa Mulungu.
20 Inlayat ti gayyemko dagiti imana kadagiti nakikapia kenkuana; saanna a rinaem ti katulaganda.
Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake; iye akuphwanya pangano ake.
21 Nalammuyot ti ngiwatna a kas iti mantikilia ngem adda gura ti pusona; naluklukneng ngem iti lana dagiti balikasna, ngem kinapudnona, immasutda kadagiti kampilan.
Mawu ake ndi osalala kuposa batala komabe nkhondo ili mu mtima mwake; mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta, komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
22 Ikamangyo dagiti dadagsenyo kenni Yahweh, ket saranayenakayonto; saanna pulos nga ipalubos a magaraw ti nalinteg a tao.
Tulani nkhawa zanu kwa Yehova ndipo Iye adzakulimbitsani; Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
23 Ngem sika, O Dios, ipisokmonto dagiti nadangkes iti abut ti pannakadadael; dagiti mawaw iti dara ken manangallilaw a lallaki ket saanto nga agbiag iti uray kaguddua iti kaatiddog ti panagbiag dagiti dadduma, ngem no siak, agtalekak kenka.
Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa kulowa mʼdzenje lachiwonongeko; anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo sadzakhala moyo theka la masiku awo, koma ine ndimadalira Inu.

< Dagiti Salmo 55 >