< Dagiti Salmo 25 >

1 Kenka, O Yahweh itag-ayko ti biagko!
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 O Diosko, agtalekak kenka. Saanmo nga ipalubos a maibabainak; saanmo nga ipalubos nga agrag-o kaniak a sibaballigi dagiti kabusorko.
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 Awan koma iti maibabain a mangnamnama kenka, maibabain koma dagiti agaramid iti panangliput nga awan gapuna.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Ipakaammom kaniak dagiti daldalanmo, O Yahweh; isurom kaniak dagiti pagnaam.
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 Iturongnak iti kinapudnom ken isuronak, ta sika iti Dios ti pannakaisalakanko; ta mangnamnamaak kenka iti agmalmalem.
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Lagipem, O Yahweh, dagiti aramid ti kinamanangngaasim ken kinapudno ti tulagmo; ta agnanayon nga addada idin.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 Saanmo a panunoten dagiti basol iti kinaagtutubok wenno dagiti kinasukirko; Lagipennak iti kinapudno ti tulagmo gapu iti kinaimbagmo, O Yahweh!
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Ni Yahweh ket naimbag ken nalinteg; gapu iti dayta isurona ti dalan kadagiti managbasol.
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 Iturongna ti napakumbaba iti kinalinteg, ken isurona ti napakumbaba iti dalanna.
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 Amin dagiti dalan ni Yahweh ket naaramid manipud iti kinapudno ti tulag ken kinamatalek kadagiti mangsalsalimetmet iti katulaganna ken dagiti napasnek a bilbilinna.
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 Gapu iti nagannmo, O Yahweh, pakawanem dagiti basolko, ta dakkel unay daytoy.
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 Siasino a tao ti agbuteng kenni Yahweh? Isuro ti Apo kenkuana ti dalan a rumbengna a pilien.
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 Agtultuloyto ti biagna iti kinanam-ay; ken tawidento dagiti kaputotanna ti daga.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 Ti pannakigayyem ni Yahweh ket para kadagiti agdayaw kenkuana, ken ipakaammona ti tulagna kadakuada.
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 Kankanayon a nakaturong dagiti matak kenni Yahweh, ta wayawayaannanto dagiti sakak manipud iti iket.
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Talliawen ken kaasiannak; ta agmaymaysaak ken naparigatak.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 Dagiti pakariribukan ti pusok ket dimmakkelda; alawennak manipud iti pakadanagak!
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 Kitaem ti pakarigatak ken banbannogko; pakawanem dagiti amin basolko.
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Kitaem dagiti kabusorko, ta aduda; gurguraendak iti naulpit a panangggura.
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Salaknibam ti biagko ket ispalennak; saanakto a maibabain, ta agkamangak kenka!
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 Taginayonennak koma ti kinapudno ken ti kinalinteg aywanannak koma, ta mangnamnamaak kenka.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 Ispalem ti Israel, O Dios, manipud iti amin a pakariribukanna!
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!

< Dagiti Salmo 25 >