< Dagiti Salmo 132 >

1 O Yahweh, lagipem para kenni David dagiti amin a pakarigatanna.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Inu Yehova, kumbukirani Davide ndi mavuto onse anapirira.
2 Lagipem no kasano a nagsapata isuna kenni Yahweh, ti panagkarina iti Mannakabalin a Dios ni Jacob.
Iye analumbira kwa Yehova ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,
3 Kinunana, “Saanakto a sumrek iti balayko wenno mapan iti pagiddaak,
“Sindidzalowa mʼnyumba mwanga kapena kugona pa bedi langa:
4 saanakto a maturog wenno aginana
sindidzalola kuti maso anga agone, kapena zikope zanga ziwodzere,
5 aginggana makabirukak iti lugar nga agpaay kenni Yahweh, a tabernakulo para iti Mannakabalin a Dios ni Jacob.”
mpaka nditamupezera malo Yehova, malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”
6 Adtoy, nangngegmi iti maipanggep iti daytoy idiay Efrata; nasarakanmi daytoy kadagiti kataltalonan ti Jaar.
Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata, tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:
7 Umunegkaminto iti tabernakulo ti Dios; agdayawkaminto iti sakaananna.
“Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo; tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.
8 Tumakderka, O Yahweh; umayka iti pagin-inanaam a lugar.
‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira, Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.
9 Makawesan koma iti kinatarnaw dagiti papadim; agpukkaw koma iti rag-o dagiti napudno a taom.
Ansembe anu avekedwe chilungamo; anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’”
10 Para iti adipenmo a ni David, saanmo a tallikodan ti pinulotam nga ari.
Chifukwa cha Davide mtumiki wanu, musakane wodzozedwa wanu.
11 Nagsapata ni Yahweh nga agbalin a matalek kenni David; saananto a baliwan iti sapatana: “Isaadkonto ti maysa kadagiti kaputotam iti tronom.
Yehova analumbira kwa Davide, lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha: “Mmodzi wa ana ako ndidzamuyika pa mpando waufumu;
12 No salimetmetan dagiti annakmo ti tulag ken dagiti lintegko nga isurokto kadakuada, agtugawto met dagiti annakda iti tronom iti agnanayon nga awan patinggana.”
ngati ana ako azisunga pangano langa ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa, pamenepo ana awo adzakhala pa mpando wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”
13 Pudno a pinili ni Yahweh ti Sion; tinarigagayanna isuna a pagnaedanna.
Pakuti Yehova wasankha Ziyoni, Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:
14 Daytoy ti lugar a paginanaak iti agnanayon, agnaedakto ditoy, ta tarigagayak isuna.
“Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi; ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.
15 Aglaplapusananto a bendisionak isuna iti pakasapulanna; pennekekto iti tinapay dagiti nakurapayna.
Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri; anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.
16 Kawesakto dagiti papadina iti pannakaisalakan; agpukkawto dagiti napudno a tattaona iti napigsa gapu iti rag-o.
Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso, ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.
17 Sadiay, patuboekto ti sara ni David; nangikabilak sadiay iti pagsilawan para iti pinulotak.
“Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.
18 Kawesakto dagiti kabusorna iti bain, ngem agraniagto ti balangatna.
Ndidzaveka adani ake manyazi, koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”

< Dagiti Salmo 132 >