< Dagiti Salmo 106 >

1 Idaydayawyo ni Yahweh. Agyamankayo kenni Yahweh ta naimbag isuna, ta agtalinaed iti agnanayon ti kinapudnona iti tulagna.
Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Siasino ti makabael a mangbilang kadagiti mannakabalin nga aramid ni Yahweh wenno mangipakaammo a naan-anay kadagiti amin nga aramidna a rumbeng a bigbigen?
Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
3 Nagasat dagiti agaramid iti maiparbeng, ken dagiti kanayon a nalinteg dagiti aramidda.
Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
4 Lagipennak O Yahweh, inton ipakitam ti kinaimbagmo kadagiti tattaom; tulungannak inton isalakanmo ida.
Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
5 Ket makitakto ti panagdur-as dagiti pinilim, agrag-oak gapu iti kinaragsak ti nasionmo, ken agpasindayagak a kadua dagiti tawidmo.
kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
6 Nagbasolkami a kas kadagiti kapuonanmi; nagbiddutkami ken nakaaramidkami iti dakes.
Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
7 Saan a naragsakan dagiti ammami kadagiti nakaskasdaaw nga aramidmo idiay Egipto; saanda nga inkaskaso dagiti adu nga aramidmo kas panangipakitam iti kinapudnom iti tulagmo; nagsukirda iti kaaddada idiay baybay, ti baybay dagiti Runo.
Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
8 Nupay kasta, insalakanna ida gapu iti naganna tapno maiparangarangna ti pannakabalinna.
Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
9 Tinubngarna ti baybay dagiti Runo, ket namagaan daytoy. Ket indalanna ida iti kaadalman, a kas iti let-ang.
Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
10 Insalakanna ida manipud iti ima dagiti nanggura kadakuada, ken inispalna ida manipud iti pannakabalin ti kabusor.
Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
11 Ngem linemmes dagiti dandanum dagiti kabusorda; awan ti uray maysa kadakuada iti nakalasat.
Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
12 Ket namatida kadagiti sasaona, ken nagkantada iti pagdaydayaw kenkuana.
Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
13 Ngem nalipatanda a dagus dagiti inaramidna; saanda nga inuray dagiti pagannurotanna.
Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
14 Naaddaanda iti saan a makapnek a panagtarigagay iti makan idiay let-ang, ket sinuotda ti Dios idiay disierto.
Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
15 Intedna kadakuada dagiti kiddawda, ngem nangibaon isuna iti sakit a nangparigat kadagiti bagida.
Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
16 Idiay kampo, nagimonda ken Moises kenni Aaron a nasantoan a padi ni Yahweh.
Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
17 Nagringngat ti daga ket inallun-onna ni Datan ken ginaburanna dagiti pasurot ni Abiram.
Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
18 Rimsua ti apuy kadakuada; ket inuram ti apuy dagiti nadangkes.
Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
19 Nagaramidda iti baka idiay Horeb ket nagrukbabda iti nahulma a landok nga imahe.
Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
20 Insukatda ti dayag ti Dios iti imahe dagiti baka a magmangan iti ruot.
Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
21 Nilipatanda ti Dios a Mangisalakanda, a nangaramid kadagiti nakaskasdaaw nga aramid idiay Egipto.
Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
22 Nangaramid isuna kadagiti nakaskasdaaw a banbanag idiay daga ni Ham ken naindaklan nga aramid idiay baybay dagiti Runo.
zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
23 Ikeddengna koman ti pannakadadaelda, no saan a bimmallaet ni Moises a pinilina kenkuana idiay naggidiatan tapno pukawen ti ungetna a mangdadael kadakuada.
Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
24 Ket inlaksidda ti nadam-eg a daga; saanda a pinati ti karina,
Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
25 ngem nagtanabutobda kadagiti toldada, ket saanda a nagtulnog kenni Yahweh.
Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
26 Isu nga ingngatona ti imana ken insapatana kadakuada nga itulokna a matayda idiay disierto,
Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
27 iwarasna dagiti kaputotanda kadagiti nasion, ken iwarasna ida kadagiti gangannaet a dagdaga.
kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
28 Nagrukbabda iti Baal ti Peor ket kinnanda dagiti naidaton kadagiti natay.
Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
29 Pinaungetda isuna gapu kadagiti tignayda, ket rimsua ti maysa a didigra kadakuada.
anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
30 Ket timmakder ni Finees tapno mangiballaet, ket nagsardeng ti didigra.
Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
31 Naibilang kenkuana daytoy a kas nalinteg nga aramid kadagiti amin a henerasion iti agnanayon.
Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
32 Pinaungetda pay ni Yahweh idiay danum ti Meriba, ket nagsagaba ni Moises gapu kadakuada.
Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
33 Pinagsakitda ti nakem ni Moises, ket nagsao isuna a siraranggas.
pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
34 Saanda a dinadael dagiti nasion a kas imbilin ni Yahweh kadakuada,
Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
35 ngem nakilangenlangenda kadagiti nasion ket nasursoroda dagiti wagas dagitoy
Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
36 ken nagrukbabda kadagiti didiosen dagitoy a nasion, nga isu ti nagbalin a palab-og kadakuada.
Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
37 Indatonda dagiti annakda kadagiti demonio.
Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
38 Nangpasayasayda iti dara iti awan basolna, ti dara dagiti annakda a lallaki ken babbai, nga indatonda kadagiti didiosen ti Canaan, tinulawanda ti daga babaen iti dara.
Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
39 Natulawanda babaen kadagiti aramidda; kasda la kadagiti balangkantis kadagiti tignayda.
Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
40 Isu a nakaunget ni Yahweh kadagiti tattaona, ket linaksidna dagiti bukodna a tattao.
Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
41 Inyawatna ida kadagiti nasion, ket inturayan ida dagiti nanggura kadakuada.
Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
42 Indadanes ida dagiti kabusorda, ken naikabilda iti panangituray dagitoy.
Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
43 Adu a daras nga immay isuna tapno tulonganna ida, ngem nagsukirda latta ket naipababada gapu iti bukodda a basol.
Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
44 Nupay kasta, impangagna dagiti pakariribukanda idi immasugda kenkuana.
Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
45 Linagipna ti tulagna kadakuada ket naasian isuna gapu iti kinapudnona iti tulagna.
Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
46 Nagtignay isuna kadagiti nangparmek kadakuada tapno maasida kadakuada.
Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
47 Isalakannakami O Yahweh a Diosmi. Ummongennakami manipud kadagiti nasion tapno makapagyamankami iti nasantoan a naganmo ken ipannakkelmi ti dayawmo.
Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
48 Maidaydayaw koma ni Yahweh, ti Dios ti Israel iti agnanayon nga awan inggana. Kinuna amin dagiti tattao, “Amen.” Idaydayawyo ni Yahweh. Maikalima a Libro
Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.

< Dagiti Salmo 106 >