< Dagiti Salmo 102 >
1 Denggem ti kararagko, O Yahweh, denggem ti sangitko kenka.
Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
2 Saanmo nga ilemmeng ti rupam kaniak iti tiempo ti panakariribukko. Denggennak. Inton umawagak kenka, sungbatannak a dagus.
Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
3 Ta kasla asuk nga agpukaw dagiti aldawko, ken mapupuoran a kasla apuy dagiti tulangko.
Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
4 Narumek ti pusok, ken kaslaak la ruot a nalaylay. Nalipatak ti mangan iti aniaman a taraon.
Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
5 Iti agtultuloy a panagas-asugko, kimmuttongak iti kasta unay.
Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
6 Kaslaak iti kalaw iti let-ang; nagbalinnak a kasla kullaaw iti langalang.
Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
7 Nakaiddaak a siririing a kasla agmaymaysa a billit, agmaymaysa iti tuktok ti balay.
Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
8 Agmalmalem nga uy-uyawendak dagiti kabusorko; us-usaren dagiti manguy-uyaw kaniak ti naganko iti panangilunod.
Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
9 Kankanek dagiti dapo a kasla tinapay ken nalaokan ti in-inumek iti luluak.
Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
10 Gapu iti nakaro a pungtotmo, binagkatnak tapno ipurruaknak.
chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
11 Dagiti aldawko ket kasla aniniwan nga agpukpukaw, ken malaylayak a kasla ruot.
Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
12 Ngem sika, O Yahweh, agtalinaedka iti agnanayon, ken ti kinalatakmo ket agpaay kadagiti amin a henerasion.
Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
13 Bumangonka ket kaasiam ti Sion. Ita ti tiempo a kaasiam isuna; dimtengen ti naituding a tiempo.
Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
14 Ta iggem dagiti adipenmo dagiti napapateg a bato ti Sion ket ipatpategda ti tapok ti pannakadadaelna.
Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
15 Raemento dagiti nasion ti naganmo, O Yahweh, ken itan-ok dagiti amin nga ari iti daga ti dayagmo.
Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
16 Bangonento manen ni Yahweh ti Sion ket agparangto iti dayagna.
Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
17 Iti dayta a tiempo, sungbattannanto dagiti kararag dagiti napanglaw; saannanto nga ilaksid dagiti karagragda.
Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
18 Maisuratto daytoy para iti sumaruno a henerasion, ket dagiti tattao a saan pay a naipasngay ket dayawendanto ni Yahweh.
Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
19 Ta kimmita isuna manipud kadagiti ngato a nasantoan; nakita ni Yahweh ti daga manipud idiay langit
“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
20 tapno denggenna ti panagasug dagiti balud, tapno wayawayaanna dagiti naikeddeng a matay.
kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
21 Kalpasanna, ipaakaamonto dagiti tattao ti nagan ni Yahweh idiay Sion ken ti dayawna idiay Jerusalem
Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
22 inton agmaymaysa nga agtitipon dagiti tattao ken dagiti pagarian tapno agserbida kenni Yahweh.
pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
23 Inikkatna ti pigsak iti katengngaan ti biag. Pinaababana dagiti aldawko.
Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
24 Kinunak, “Diosko, saannak pay nga alaen iti katengngaan iti biag; addaka ditoy iti amin a henerasion.
Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
25 Idi un-unana a tiempo, insaadmo ti daga; dagiti langit ket aramid dagiti imam.
Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
26 Agpukawda ngem agnanayonto nga addaka; dumaanda a kas iti pagan-anay; kas iti kawes, ikkatemto ida ket agpukawdanto.
Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
27 Ngem saanka nga agbalbaliw, ken saan nga agpatingga dagiti tawenmo.
Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
28 Agtultuloy nga agbiag dagiti annak dagiti adipenmo, ken agbiag iti presensiam dagiti kaputotanda.”
Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”