< Dagiti Salmo 10 >

1 O Yahweh, apay nga umad-adayoka? Apay nga aglemlemmengka iti tiempo ti riribuk?
Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali? Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?
2 Gapu iti kinapalangguadda, kamaten dagiti nadangkes a tattao dagiti maidaddadanes; ngem pangngaasim ta ipalubosmo a mapalab-ogan dagiti nadangkes babaen kadagiti bukodda a panggep nga insaganada.
Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka, amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.
3 Ta ipaspasindayag ti nadangkes a tao ti nalaus a tarigagayna; padpadayawanna dagiti naagum ken lalaisenna ni Yahweh.
Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake; amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.
4 Ti nadangkes a tao ket natangsit, saanna a sapsapulen ti Dios. Pulos a saanna a panpanunoten ti Dios gapu ta saanna a pagan-ano ti maipapan kenkuana.
Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu; mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.
5 Natalged isuna iti amin a tiempo, ngem nangato unay kenkuana dagiti nalinteg a bilbilinmo; tagtagibassitenna dagiti amin a kabusorna.
Zinthu zake zimamuyendera bwino; iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali; amanyogodola adani ake onse.
6 Kunaenna iti pusona, “Saanakto pulos a mapaay; saanakto a makapadas iti riribuk iti amin a henerasion.”
Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze. Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”
7 Napnoan ti ngiwatna iti panangilunod, panangallilaw, ken makapasakit a sasao; mangdangran ken mangdadael ti dilana.
Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza; zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.
8 Agab-abang isuna nga agsaneb iti asideg dagiti purpurok; patpatayenna dagiti awan basolna kadagiti nalimed a lugar; agsisiim dagiti matana kadagiti biktimaenna nga awan gawayna.
Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi, kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa, amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.
9 Aglemlemmeng isuna a kasla leon iti kasamekan; agpadpadaan isuna a mangtiliw kadagiti maidaddadanes. Tiltiliwenna dagiti maidaddadanes no guyodenna ti silona.
Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba. Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu; amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.
10 Marumek ken madangran dagiti biktimana; matnagda kadagiti nalagda a silona.
Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka; amakhala pansi pa mphamvu zake.
11 Kunaenna iti pusona, “Nanglipat ti Dios; lenglengdanna ti rupana; saannan a kayat ti kumita.”
Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala, wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”
12 Bumangonka, O Yahweh; ingatom ti imam iti panangukom, O Dios. Saanmo a lipaten dagiti maidaddadanes.
Dzukani Yehova! Onetsani dzanja lanu Inu Mulungu. Musayiwale anthu opanda mphamvu.
13 Apay a laklaksiden ti nadangkes a tao ti Dios ken kunaenna iti pusona, “Awanto ti sungsungbatak kenka”?
Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu? Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake, “Iye sandiyimba mlandu?”
14 Nakitam, ta kanayon a makitkitam ti mangpaspasagrap iti riribuk ken liday. Italtalek dagiti awan gawayna ti bagida kenka; is-ispalem dagiti ulila.
Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa, mumaganizira zochitapo kanthu. Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.
15 Tukkolem ti takiag ti nadangkes ken managdakdakes a tao; dusaem isuna gapu kadagiti dakes nga aramidna, nga impagarupna a saanmo a matakuatan.
Thyolani dzanja la woyipitsitsa ndi la munthu woyipa; muzengeni mlandu chifukwa cha zoyipa zake zimene sizikanadziwika.
16 Ni Yahweh ti Ari iti agnanayon ken awan patinggana; mapapanaw dagiti nasion iti dagana.
Yehova ndi Mfumu kwamuyaya; mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.
17 O Yahweh, nangngegmo dagiti kasapulan dagiti maidaddadanes; pappapigsaem ti pusoda, dengdenggem ti kararagda;
Mumamva Inu Yehova, zokhumba za osautsidwa; mumawalimbikitsa ndipo mumamva kulira kwawo.
18 ikankanawam dagiti ulila ken dagiti maidaddadanes tapno awan ti tao ditoy rabaw ti daga ti mangbutbuteng manen.
Kuteteza ana amasiye ndi oponderezedwa, ndi cholinga chakuti munthu amene ali wa dziko lapansi asaopsenso.

< Dagiti Salmo 10 >