< Pilipos 4 >
1 Ngarud, patpatgek a kakabsatko nga il-iliwek, dakayo a ragsak ken koronak iti daytoy a dalan a sititibker a pagtaktakderak iti Apo, patpatgek a gagayyem.
Tsono abale anga, ndimakukondani ndipo ndikukulakalakani. Ndinu chimwemwe changa ndi chipewa cha ulemerero wanga. Abwenzi okondedwa, chilimikani choncho mwa Ambuye.
2 Makipakpakaasiak kenni Evodias, ken makipakpakaasiak kenni Sintike, maaddaankayo koma iti sangsangkamaysa a panunot iti Apo.
Ndikudandaulira Euodiya ndi Suntuke kuti akhale ndi mtima umodzi mwa Ambuye.
3 Kinapudnona ipakpakaasik met kadakayo, pudno a padak nga agbakbaklay: tulonganyo dagitoy a babbai. Ta nakipagbannogda met kaniak iti pannakailawa ti ebangelio a kaduami ni Clemente ken dagiti dadduma nga agtrabtrabaho, nga adda met iti Libro ti Biag dagiti naganda.
Inde, ndikupempha iwe mnzanga pa ntchitoyi, thandiza amayiwa amene ndagwira nawo ntchito ya Uthenga Wabwino pamodzi ndi Klementonso ndi ena onse antchito anzanga amene mayina awo ali mʼbuku lamoyo.
4 Agrag-okayo a kanayon iti Apo. Ibagak manen, agrag-okayo.
Nthawi zonse muzikondwa mwa Ambuye. Ndikubwerezanso; muzikondwa!
5 Maipakita koma kadagiti amin a tattao ti kinaimmayo. Asidegen ti Apo.
Kufatsa kwanu kuzioneka pamaso pa anthu onse. Ambuye anu ali pafupi.
6 Saanyo a pakadanagan dagiti banbanag. Ngem ketdi, iti amin banag, maipakaammo koma iti Dios dagiti dawdawatenyo babaen iti karkararag ken dawdawat nga addaan panagyaman.
Musade nkhawa ndi kanthu kalikonse, koma pa china chilichonse, mwa pemphero ndi chidandaulo pamodzi ndi chiyamiko, perekani zopempha zanu kwa Mulungu.
7 Ken ti talna iti Dios, a nalablabes pay ngem iti amin a pannakaawat, bantayannanto dagiti puspuso ken panpanunotyo iti kaaddayo kenni Cristo Jesus.
Ndipo mtendere wa Mulungu, umene upambana nzeru zonse udzasunga bwino mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.
8 Kamaudiananna, kakabsat, aniaman a banbanag a pudno, aniaman a banbanag a nadayaw, aniaman a banbanag a nalinteg, aniaman a banbanag a nadalus, aniaman a banbanag a nakaay-ayat, aniaman a banbanag a mararaem, no adda aniaman a banag a nangato, no adda aniaman a banag a maidaydayaw, panunoten ti maipapan kadagitoy a banbanag.
Potsiriza, abale, muziyika mtima wanu pa zinthu zilizonse zabwino ndi zotamandika monga, zinthu zoona, zinthu zolemekezeka, zinthu zolungama, zinthu zoyera, zinthu zokongola ndi zinthu zosiririka.
9 Dagiti banbanag a naadalyo ken naawatyo ken nangngeganyo ken nakitayo kaniak, aramidenyo dagitoy a banbanag. Ken ti Dios ti kappia ket addanto kadakayo.
Muzichita chilichonse chimene mwaphunzira kapena kulandira kapena kumva kuchokera kwa ine kapena mwaona mwa ine. Ndipo Mulungu wamtendere adzakhala nanu.
10 Maragsakanak unay iti Apo gapu ta kamaudiananna napabaroyon ti pakaseknanyo kaniak. Pudno nga adda panangisakityo kaniak idi, ngem awan ti gundawayyo a tumulong kaniak.
Ndikukondwa kwambiri mwa Ambuye kuti patapita nthawi tsopano mwayambanso kuonetsa kuti mumandiganizira. Zoonadi, mwakhala mukundikumbukira, koma munalibe mpata woti muonetsere zimenezi.
11 Saan a gapu kadagiti kasapulak nga ibagbagak daytoy. Ta nasursurok no kasano ti mapnek kadagiti amin a pasamak.
Sindikunena izi chifukwa choti ndikusowa thandizo, poti ine ndaphunzira kukhala wokwaniritsidwa ndi zimene ndili nazo.
12 Ammok no kasano ti agkasapulan, ken ammok met no kasano ti maaddaan iti aglaplapusanan a parabur. Iti tunggal wagas ken iti amin a banbanag, nasursurok ti palimed no kasano a mangan iti adu ken ti mabisinan, no kasano ti maaddaan iti aglaplapusanan ken ti agkasapulan.
Ndimadziwa kusauka nʼkutani, ndipo ndimadziwa kulemera nʼkutani. Ndaphunzira chinsinsi chokhala wokhutitsidwa mwa njira ina iliyonse, kaya nʼkudya bwino kapena kukhala ndi njala, kaya kukhala ndi chuma kapena umphawi.
13 Maaramidko amin dagitoy a banbanag babaen kenkuana a mangmangted iti pigsak.
Ndikhoza kuchita zonse kudzera mwa Iye amene amandipatsa mphamvu.
14 Nupay kasta, nasayaat ti inaramidyo iti pannakipagsagabayo kaniak.
Komatu munachita bwino kundithandiza mʼmavuto anga.
15 Ket ammoyo, dakayo a taga-Filipos, nga idi rugrugi ti ebanghelio, idi pimmanawak idiay Macedonia, awan ti Iglesia a timmulong kaniak maipanggep iti panangited ken panangawat malaksid laeng kadakayo.
Ndipo inu Afilipi mukudziwa kuti masiku oyambirira olalikira Uthenga Wabwino, nditachoka ku Makedoniya, panalibe mpingo ndi umodzi omwe umene unagwirizana nane pa nkhani yopereka ndi kulandira, kupatula inu.
16 Uray pay idi addak idiay Tesalonica, impatulodandak iti tulong para kadagiti kasapulak saan laeng a naminsan.
Pakuti ngakhale pamene ndinali ku Tesalonika, munanditumizira kangapo zondithandiza pa zosowa zanga.
17 Saan a gapu ta sapulek ti sagut. Ngem ketdi, sapulek ti bunga a mangpaadu iti pagsayaatanyo.
Osati ndikufuna mphatso zanu, koma ndikufuna kuti pa zimene muli nazo pawonjezerekepo phindu.
18 Naawatkon amin a banag, ken adun ti adda kaniak. Napnoanakon. Naawatkon manipud kenni Epafrodito dagiti banag manipud kadakayo. Nabanglo ti ayamuomda, maysa a maikari a daton a makaay-ayo iti Dios.
Ndalandira zonse ndipo ndili nazo zokwanira zoposa zosowa zanga popeza ndalandira kwa Epafrodito mphatso zochuluka zimene munatumiza. Ndizo zopereka za fungo labwino, nsembe zolandiridwa zokondweretsa Mulungu.
19 Ket punnoanto ti Diosko ti tunggal pagkasapulanyo segun iti kinabaknang ti dayag ni Cristo Jesus.
Ndipo Mulungu wanga adzakwaniritsa zosowa zanu monga mwa chuma chake chaulemerero mwa Khristu Yesu.
20 Ita, iti Dios ken Amatayo, kenkuana ti dayaw iti agnanayon. Amen. (aiōn )
Kwa Mulungu ndi Atate athu, kukhale ulemerero mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
21 Kablaawanyo ti tunggal namati kenni Cristo Jesus. Kabkablaawan dakayo dagiti kakabsat a kaduak.
Perekani moni kwa oyera mtima onse mwa Khristu Yesu. Abale amene ali ndi ine akupereka moni wawo.
22 Kabkablaawandakayo amin dagiti namati ditoy, nangnangruna ti sangkabalayan ni Cesar.
Oyera mtima onse akupereka moni, makamaka iwo a ku nyumba ya Kaisara.
23 Ti parabur ni Apotayo a Jesu-Cristo ket adda koma iti espirituyo.
Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wanu. Ameni.