< Numero 12 >
1 Kalpasanna, nagsao da Miriam ken Aaron maibusor kenni Moises gapu iti maysa a Cusita nga inasawana.
Miriamu ndi Aaroni anayamba kuyankhula motsutsana ndi Mose chifukwa cha mkazi wa ku Kusi, popeza Moseyo anakwatira Mkusi.
2 Kinunada, “Ni Moises laeng kadi ti kinasao ni Yahweh? Saan kadi a nakisao met isuna kadata?” Nangngeg ita ni Yahweh ti imbagada.
Iwowo anafunsa kuti, “Kodi Yehova anayankhula kudzera mwa Mose yekha? Kodi sanayankhule kudzeranso mwa ife?” Ndipo Yehova anamva zimenezi.
3 Ita, ti tao a ni Moises ket napakumbaba unay, napakpakumbaba ngem iti siasinoman iti daga.
(Koma Mose anali munthu wodzichepetsa kwambiri kuposa munthu aliyense pa dziko lapansi).
4 Kinasao a dagus ni Yahweh da Moises, Aaron ken Miriam: “Rummuarkayo, dakayo a tallo, inkayo iti tabernakulo.” Isu a rimmuarda a tallo.
Nthawi yomweyo Yehova anati kwa Mose, Aaroni ndi Miriamu, “Bwerani ku tenti ya msonkhano nonse atatu.” Ndipo atatuwo anapitadi kumeneko.
5 Ket bimmaba ni Yahweh babaen iti kasla adigi ti ulep. Nagtakder isuna iti pagserkan ti tolda ket inayabanna da Aaron ken Miriam. Nagpasango dagiti dua.
Tsono Yehova anatsika mu mtambo, nayima pa khomo la chihema. Kenaka anayitana Aaroni ndi Miriamu. Ndipo onse awiri atapita patsogolo,
6 Kinuna ni Yahweh, “Ita denggenyo dagiti sasaok. No adda kadakayo ti propetak, agparangak kenkuana babaen kadagiti sirmata ken makisaritaak kenkuana babaen iti tagtagainep.
Mulungu anati, “Mverani mawu anga: “Pakakhala mneneri wa Yehova pakati panu, ndimadzionetsera kwa iyeyo mʼmasomphenya, ndimayankhula naye mʼmaloto.
7 Saan a kasta ti adipenko a ni Moises. Napudno isuna iti entero a balayko.
Koma sinditero ndi Mose mtumiki wanga; Iyeyu ndi wokhulupirika mʼnyumba yanga yonse.
8 Makisarsaritaak kenkuana a sangon-sango, saan nga iti sirmata wenno burburtia. Makitkitana ti langak. Isu nga apay a saankayo a mabuteng nga agsao iti maibusor iti adipenko, maibusor kenni Moises?”
Ndimayankhula naye maso ndi maso, momveka bwino osati mophiphiritsa; ndipo amaona maonekedwe a Yehova. Nʼchifukwa chiyani simunaope kuyankhula motsutsana ndi Mose mtumiki wanga?”
9 Nakaunget unay ni Yahweh kadakuada, ken kalpasanna, pinanawanna ida.
Ndipo Yehova anawakwiyira, nachoka.
10 Nagpangato ti ulep manipud iti ngatoen ti tolda, ket dagus a nagketong ni Miriam—pimmurpuraw isuna a kas iti niebe. Idi simmango ni Aaron kenni Miriam, nakitana nga adda ketong ni Miriam.
Pamene mtambo unachoka pamwamba pa Chihema, taonani, Miriamu anagwidwa ndi khate. Aaroni atachewuka anaona Miriamu ali ndi khate;
11 Kinuna ni Aaron kenni Moises, “O, apok, pangaasim ta saanmo nga ibilang daytoy a basol a maibusor kadakami. Minamaag dagiti imbagbagami ket nakabasolkami.
ndipo Aaroni anawuza Mose kuti, “Pepani mbuye wanga, musatilange chifukwa cha tchimo limene tachita mopusa.
12 Pangaasim ta saanmo nga ipalubos nga agbalin isuna a kasla natay a maladaga a narunot ti kagudua ti bagina idi rimmuar iti aanakan ti inana.”
Musalole kuti Miriamu akhale ngati mwana wobadwa wakufa kuchoka mʼmimba mwa amayi ake, thupi lake litawonongeka.”
13 Isu nga immawag ni Moises kenni Yahweh. Kinunana, “Pangaasim ta paimbagem isuna, O Dios pangaasim.”
Tsono Mose anafuwulira Yehova kuti, “Chonde Inu Mulungu, muchiritseni!”
14 Kinuna ni Yahweh kenni Moises, “No tinupraan ti amana ti rupana, maibabain isuna iti pito nga aldaw. Iserraanyo isuna iti ruar ti kampo iti pito nga aldaw. Kalpasan dayta, pastrekenyo manen isuna.”
Yehova anayankha Mose kuti, “Abambo ake akanamulavulira malovu mʼmaso, kodi sakanakhala wonyozeka masiku asanu ndi awiri? Mutsekereni kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri, kenaka mumulowetsenso.”
15 Isu a naserraan ni Miriam iti ruar ti kampo iti las-ud ti pito nga aldaw. Saan a nagdaliasat dagiti tattao agingga a nagsubli ni Miriam iti kampo.
Choncho anamutsekera Miriamu kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri ndipo anthu sanayende ulendo wawo mpaka Miriamu atamulowetsanso.
16 Kalpasan dayta, nagdaliasat dagiti tattao manipud Hazerot ket nagkampoda iti let-ang ti Paran.
Pambuyo pake anthu ananyamuka ku Heziroti ndi kukamanga mʼchipululu cha Parani.