< Nehemias 13 >

1 Iti dayta nga aldaw, imbasa dagiti padi ti Libro ni Moises a mangmangngeg dagiti tattao. Naduktalanda a nakasurat iti daytoy a nasken a saan a makitipon dagiti Ammonita wenno Moabita iti taripnong ti Dios, iti agnanayon.
Pa tsiku limenelo anawerenga buku la Mose anthu akumva. Ndipo anapeza mawu akuti, Mwamoni kapena Mmowabu asalowe konse mu msonkhano wa Mulungu.
2 Gapu ta saanda a nangted iti tinapay ken danum kadagiti tattao ti Israel, ngem ketdi tinangdananda ni Balaam a mangilunod iti Israel. Nupay kasta, pinagbalin ti Diostayo ti lunod a bendision.
Paja iwowa sanawachingamire Aisraeli kukawapatsa chakudya ndi madzi. Mʼmalo mwake analemba ganyu Baalamu kuti adzawatemberere. Komabe Mulungu wathu anasandutsa tembererolo kukhala mdalitso.
3 Apaman a nangngegda ti linteg, inlasinda dagiti amin a gangannaet manipud iti Israel.
Anthu atamva lamuloli, anachotsa pakati pawo onse amene anali achilendo.
4 Ita, sakbay a nadutokan ni Eliasib a padi a mangaywan kadagiti siled a pagiduldulinan iti balay ti Diostayo. Gayyemnan ni Tobias.
Izi zisanachitike, wansembe Eliyasibu anali atasankhidwa kukhala woyangʼanira zipinda zosungiramo katundu za Nyumba ya Mulungu. Iyeyu ankagwirizana kwambiri ndi Tobiya.
5 Insagana ni Eliasib ti dakkel a siled a pagiduldulinan para kenni Tobias, a sigud a pagikabkabilanda kadagiti daton a bukbukel, kadagiti insenso, kadagiti alikamen, ken kadagiti apagkapullo ti trigo, baro nga arak, ken ti lana, a nairanta para kadagiti Levita, kadagiti kumakanta, kadagiti guardia ti ruangan, ken kadagiti kontribusion para kadagiti papadi.
Choncho anamupatsa chipinda chachikulu chimene kale ankasungamo zopereka zakudya, lubani, ziwiya, zopereka za chakhumi za tirigu, vinyo ndi mafuta zoyenera kuperekedwa kwa Alevi, oyimba nyimbo ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu, komanso mphatso zoyenera kupereka kwa ansembe.
6 Ngem iti tiempo a mapaspasamak amin dagitoy, awanak idiay Jerusalem. Gapu ta iti maikatallopulo ket dua a tawen a panagari ni Artaxerxes iti Babilonia, napanak iti ayan ti ari. Saan a nagbayag, nagkiddawak iti ari iti pammalubos a pumanaw,
Koma pamene izi zonse zinkachitika mu Yerusalemu, ine kunalibe popeza mʼchaka cha 32 cha Aritasasita mfumu ya Babuloni ine ndinabwerera kwa mfumu. Patapitanso nthawi ndinapempha chilolezo kwa mfumuyo
7 ket nagsubliak idiay Jerusalem. Natakuatak ti dakes nga inaramid ni Eliasib a panangipaaramatna kenni Tobias iti siled a pagiduldulinan iti paraangan iti balay ti Dios.
ndipo ndinabwerera ku Yerusalemu. Kumeneko ndinamva za chinthu choyipa chimene Eliyasibu anachita pomupatsa Tobiya chipinda mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
8 Kasta unay ti ungetko ket impurruakko dagiti alikamen ni Tobias iti ruar ti siled a pagiduldulinan.
Ndinapsa mtima kwambiri ndipo ndinataya kunja katundu yense wa Tobiya amene anali mʼchipindamo.
9 Imbilinko nga aramidenda ti seremonia ti pannakadalus kadagiti siled a pagiduldulinan, ket insublik kadagitoy dagiti alikamen iti balay ti Dios, dagiti daton a trigo, ken ti insenso.
Ndinalamulira kuti ayeretse zipinda, ndipo kenaka ndinabwezeramo zida za mʼNyumba ya Mulungu, pamodzi ndi chopereka cha zakudya ndi lubani.
10 Ken natakuatak a saan a naibunong kadagiti Levita dagiti bingay a nairanta a maited kadakuada, isu a dagus a pinanawanda ti templo, ket nagturong ti tunggal maysa iti talonna, kasta met ti inaramid dagiti kumakanta nga agserserbi.
Ndinapezanso kuti Alevi sankalandira magawo awo amene amayera kulandira. Chotsatira chake Alevi onse pamodzi ndi oyimba nyimbo amene ankagwira ku Nyumba ya Mulungu anathawa, aliyense kupita ku munda wake.
11 Isu nga inungtak dagiti opisial ket kinunak kadakuada, “Apayen a nabaybay-an ti balay ti Dios?” Inummongko ida ken pinaggianko ida kadagiti kampoda.
Choncho ndinadzudzula akuluakulu aja ndipo ndinawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Nyumba ya Mulungu yasiyidwa?” Ndipo ine ndinawayitanitsa pamodzi ndi kuwayika mʼmalo awo.
12 Ket inyeg dagiti amin a taga-Juda ti apagkapullo ti trigo, baro nga arak, ken ti lana kadagiti siled a pagiduldulinan.
Pambuyo pake Ayuda anayambanso kubwera ndi zopereka zawo za chakhumi cha tirigu, vinyo ndi mafuta kuti ziperekedwe ku nyumba yosungiramo chuma.
13 Insaadko a kas tresurero kadagiti siled a pagiduldulinan da Selemias a padi, Zadok nga eskriba, ken Pedaias a nagtaud iti Levita. Sumaruno kadakuada ni Hanan a putot ni Zaccur a putot ni Matanias, gapu ta ammok a mapagtalkak ida. Ti trabahoda ket agibunong kadagiti abasto kadagiti padada nga agtrabtrabaho.
Ndipo ndinasankha wansembe Selemiya, mlembi Zadoki, ndi Mlevi wotchedwa Pedaya kukhala oyangʼanira zipinda zosungiramo. Ndinasankhanso Hanani mwana wa Zakuri mwana wa Mataniya kukhala wowathandizira chifukwa ndinaona kuti anthu awa anali odalirika. Ntchito yawo inali yogawira abale awo zinthu zofunika.
14 Laglagipem, O Diosko ti maipapan iti daytoy, ken saanmo koma a punasen dagiti nasasayaat nga inaramidko para iti balay ti Diosko ken dagiti trabaho iti daytoy.
Inu Mulungu wanga, mundikumbukire pa zimenezi, ndipo musafafanize ntchito zanga zimene ndachita mokhulupirika pa Nyumba yanu pofuna kukutumikirani.
15 Kadidiay nga aldaw, nakakitaak kadagiti tattao idiay Juda nga agpespespes iti ubas iti Aldaw a Panaginana ken agaw-awitda kadagiti trigo ket ilugluganda dagitoy kadagiti asnoda, ken kasta met ti arak, ubas, igos, ken amin a kita dagiti nadagsen a karga sada inyeg idiay Jerusalem iti Aldaw a Panaginana. Nagririak ta aglaklakoda kadagiti taraon iti dayta nga aldaw.
Nthawi imeneyo ndinaona anthu a mu Yuda akuponda ndi kufinya mphesa pa tsiku la Sabata. Ena ankawunjika tirigu milumilu ndi kumasenzetsa abulu. Enanso ankabwera ndi vinyo, mphesa, mkuyu ndi katundu wa mitundumitundu ku Yerusalemu pa tsiku la Sabata. Choncho ndinawachenjeza za kugulitsa zakudya pa tsiku la Sabata.
16 Nagisangpet dagiti lallaki a taga-Tiro nga agnanaed idiay Jerusalem iti lames ken amin a kita ti magatang, ket inlakoda dagitoy kadagiti tattao ti Juda ken iti entero a siudad iti Aldaw a Panaginana!
Nawonso anthu a ku Turo amene ankakhala mu Yerusalemu ankabweretsa nsomba ndi akatundu ena onse amalonda kudzagulitsa pa Sabata kwa anthu a mʼdziko la Yuda ndi a mu Yerusalemu.
17 Binabalawko ngarud dagiti pangulo ti Juda, “Ania daytoy a dakes nga ar-aramidenyo, saanyo a raraemen ti Aldaw a Panaginana?
Ndipo ndinadzudzula anthu olemekezeka a dziko la Yuda. Ndinawafunsa kuti, “Nʼchoyipa chanji mukuchitachi, kumayipitsa tsiku la Sabata chotere?
18 Saan kadi nga inaramid dagiti ammayo daytoy? Ken saan kadi nga inyeg ti Diostayo amin dagitoy a dakes kadatayo ken iti daytoy a siudad? Ita, ad-adda pay a pagpungpungtotenyo ti Dios iti Israel gapu iti saanyo a panagraem iti Aldaw a Panaginana.”
Makolo anu anachita zomwezi ndipo Mulungu wathu anadzetsa mavuto pa ife ndi pa mzinda uwu. Kodi inu mukufuna kuwutsanso mkwiyo wa Mulungu pa Israeli pamene mukudetsa tsiku la Sabata?”
19 Apaman a sumipnget iti ruangan ti Jerusalem sakbay a mangrugi ti Aldaw a Panaginana, imbilinko a marikpan dagiti ridaw ken nasken a saan a maluktan dagitoy agingga a malpas ti Aldaw a Panaginana. Pinagbantayko dagiti sumagmamano kadagiti adipenko iti ruangan tapno awan ti karga a maiyuneg iti Aldaw a Panaginana.
Nʼchifukwa chake ndikulamula kuti pamene kuyamba kuda, tsiku la Sabata lisanayambe, azitseka zipata zonse za Yerusalemu ndipo asazitsekule mpaka sabata litatha. Ndinayika ena mwa antchito anga oyangʼanira pa zipata kuti katundu aliyense asalowe mu Yerusalemu pa tsiku la Sabata.
20 Naminsan wenno namindua a nagkampo dagiti komersiante ken dagiti aglaklako iti amin a kita ti tagilako iti ruar ti Jerusalem.
Choncho kamodzi kapena kawiri anthu amalonda ndi anthu ogulitsa katundu osiyanasiyana ankagona usiku wonse kunja kwa Yerusalemu.
21 Ngem binallaagak ida, “Apay ngay nga agkamkampokayo iti ruar ti pader? No aramidenyonto pay daytoy, pagtalawenkayo!” Manipud iti dayta a tiempo saandan nga immay iti Aldaw a Panaginana.
Koma ndinawachenjeza ndi kuwafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukugona pafupi ndi khoma? Ngati muchitanso zimenezi, ine ndidzakugwirani.” Kuyambira nthawi imeneyo, sanabwerenso pa tsiku la Sabata.
22 Ken binilinko dagiti Levita nga aramidenda ti seremonia ti pannakadalusda, sada mapan guardiaan dagiti ruangan, tapno mangilin ti Aldaw a Panaginana. Laglagipem met daytoy, O Diosko, ken kaassiannak gapu iti kinapudnom iti tulagmo kaniak.
Ndipo ndinalamulira Alevi kuti adziyeretse okha ndi kubwera kudzalonda pa zipata ndi cholinga choti tsiku la Sabata likhale tsiku loyera. Inu Mulungu wanga, kumbukireninso ine pa zimenezi ndipo mundisunge malingana ndi chikondi chanu chachikulu chosasinthika.
23 Kadagidiay nga aldaw, nakitak pay dagiti Judio a nakiasawa kadagiti babbai a taga-Asdod, Ammon ken Moab.
Masiku amenewo ndinaonanso anthu a ku Yuda amene anakwatira akazi ochokera ku Asidodi, Amoni ndi Mowabu.
24 Kagudua ti bilang dagiti annakda ti agsasao iti pagsasao ti Asdod, ngem saanda a makapagsao iti pagsasao ti Juda, ti laeng pagsasao dagiti tattao a pagnanaedanda.
Theka la ana awo linkayankhula chiyankhulo cha Asidodi kapena chiyankhulo chimodzi cha anthu ena, ndipo sankathanso kuyankhula chiyankhulo cha Ayuda.
25 Ket inungtak ida, inlunodko ida, kinabilko ti dadduma kadakuada ken pinarutko dagiti bubuokda. Pinagsapatak ida iti sangoanan ti Dios, kinunak, “Saanyo ipaasawa dagiti annakyo a babbai kadagiti annakda a lallaki, wenno ipaasawa dagiti annakda a babbai kadagiti annakyo a lallaki, wenno saanyo nga asawaen dagiti annakda a babbai.
Tsono ndinakangana nawo ndi kuwatemberera. Ndinamenya ena mwa anthuwo ndi kuzula tsitsi lawo. Ine ndinawalumbiritsa mʼdzina la Mulungu kuti, “Inu musapereke ana anu aakazi kuti akwatiwe ndi ana awo aamuna kapena inuyo ngakhale ana anu aamuna kukwatira ana awo aakazi.
26 Saan kadi a dagitoy a babbai ti nakaigapuan ti panagbasol ni Solomon nga ari ti Israel? Kadagiti adu a nasion awan ti ari a kas kenkuana, ken inayat isuna ti Diosna. Ken pinagturay ti Dios isuna nga ari iti entero nga Israel. Uray no kasta, dagiti ganggannaet nga assawana ti makagapu a nagbasol isuna.
Kodi Solomoni mfumu ya Israeli suja anachimwa chifukwa cha ukwati ngati umenewu. Pakati pa mitundu yambiri panalibe mfumu ngati iyi. Iye anakondedwa ndi Mulungu wake, ndipo Mulungu anamuyika kukhala mfumu ya Israeli yense, koma iyeyo anachimwa chifukwa cha akazi achilendo.
27 Dumngegkami kadi kadakayo ket aramidenmi amin daytoy a kinadakes ken agsukirkami iti Dios babaen iti panangasawami kadagiti ganggannaet a babbai?”
Kodi tsopano ife tizimva inu kuti mukuchita choyipa chachikulu chimenechi, kupandukira Yehova Mulungu wathu pomakwatira akazi achilendo?”
28 Maysa kadagiti annak ni Joyada a putot ni Eliasib a nangato a padi ket manugang ni Sanballat a Horonita. Pinapanawko ngarud isuna idiay Jerusalem.
Mmodzi mwa ana aamuna a Yehoyada mwana Eliyasibu mkulu wa ansembe nʼkuti nthawi imeneyi ali mpongozi wa Sanibalati wa ku Horoni. Choncho ndinamuthamangitsa pamaso panga.
29 Laglagipem ida O, Diosko, gapu iti panangtulawda iti akem a kinapadi, ken iti katulagan ti kinapadi ken dagiti Levita.
Inu Mulungu wanga, mukumbukire mmene iwo anayipitsira unsembe, pangano la unsembe komanso la Alevi.
30 Ket inaramidko ti seremonia ti pannakadalusda kadagiti amin a ganggannaet, ken imbagak dagiti pagrebbengan dagiti padi ken dagiti Levita, ti tunggal maysa iti trabahona.
Motero ndinayeretsa ansembe ndi Alevi powachotsera kalikonse kachilendo. Ndipo ndinakhazikitsa ntchito zawo, kuti aliyense akhale pa ntchito yake.
31 Impaayko dagiti kayo a pangpuor iti daton iti umno a tiempo ken dagiti umuna a bunga. Laglagipennak, O Diosko, para iti pagsayaatak.
Ndiponso kupereka nkhuni ndi zipatso zoyamba kucha pa nthawi yake. Ndikumbukireni pondikomera mtima, Inu Mulungu wanga.

< Nehemias 13 >