< Mikias 6 >

1 Ita, denggem no ania ti kuna ni Yahweh. Kinuna ni Mikias kenkuana, “Bumangonka ket idatagmo ti kasom iti kabanbantayan; bay- am a mangngeg dagiti turod ti timekmo.
Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
2 Denggenyo ti darum ni Yahweh, dakayo a kabanbantayan, ken dakayo a naandor a pamuon iti daga. Ta adda darum ni Yahweh kadagiti tattaona, ket ilabanna iti pangukoman a maibusor iti Israel.”
Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
3 Tattaok, ania ti inaramidko kadakayo? Kasano koma a binannogkayo? Agsaksikayo a maibusor kaniak!
“Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
4 Ta inruarkayo iti daga ti Egipto ket insalakankayo iti balay ti pannakaadipen. Imbaonko kadakayo ni Moises, ni Aaron, kenni Miriam.
Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
5 Tattaok, lagipenyo ti pinanggep ni Balak nga ari ti Moab, ken ania ti insungbat kenkuana ni Balaam nga anak ni Beor, bayat a mapmapankayo manipud Sittim agingga iti Gilgal, tapno maammoanyo ti nalinteg nga inaramidko, Siak a ni Yahweh.”
Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
6 Ania ti rumbeng nga idatagko kenni Yahweh, kas agrukbabak iti kangatoan a Dios? Nasken kadi nga umayak kenkuana nga addaan ti daton a mapuoran, iti urbon a baka a natawenan?
Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
7 Maay-ayo ngata ni Yahweh kadagiti rinibu a karnero a kalakian, wenno dagiti sangapulo-ribu a karayan iti lana? Itedko kadi ti inauna nga anakko a para iti salungasingko, ti bunga ti bagik a para iti basolko?
Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
8 Imbagana kenka, O tao, no ania ti naimbag, ken ania ti sapsapulen ni Yahweh kenka: Aramidem ti nalinteg, ayatem ti kina-imbag, ken magnaka a sipapakumbaba iti Diosmo.
Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
9 Ti timek ni Yahweh ket agiwarwaragawag iti siudad— uray ti kinasirib ket bigbigenna ti naganmo: “Ipangagmo ti sarukod, ken ti nangisaad daytoy iti ayanna.
Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
10 Adda kinabaknang kadagiti babbalay dagiti managdakdakes ken naulbod, dagiti ulbod a timbangan a makarimon.
Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
11 Ibilangko kadi nga awan basol ti maysa a tao no mangaramat isuna iti nakusit a pagtimbangan, nga addaan ti supot dagiti manangallilaw a pagtimbangan?
Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
12 Dagiti nabaknang a tattao a napnoan ti kinaranggas, dagiti agnanaed sadiay ket agsaoda iti inuulbod, ken ti dila kadagiti ngiwatda ket manangallilaw.
Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
13 Ngarud, sugatenka iti nakaro, pinagbalinka a pakadadaelan gapu kadagiti basolmo.
Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
14 Manganka ngem saanka a mapnek; addanto latta kenka ti kinaunga-ong. Agidulinka ngem saanka a maka-urnong, ket ti maurnongmo ket iyawatkonto iti kampilan.
Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
15 Agmulaka ngem saankanto nga agapit; agbaddekka iti olibo ngem saanmo a masapsapuan ta bagim iti lana; agpespeska iti ubas ngem awan ti mainummo nga arak.
Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
16 Sinalimetmetam dagiti allagaden nga inaramid ni Omri, ken dagiti amin nga ar-aramid iti balay ni Ahab. Nagnaka babaen kadagiti balakadda. Isu a sika a siudad, pagbalinenka a dadael, ken dakayo nga agnanaed ket pagbalinekto a malalais, ket awitenyonto ti pannakaibabain a kas kadagiti tattaok.”
Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”

< Mikias 6 >