< Malakias 1 >

1 Ti pannakaipablaak ti sao ni Yahweh para iti Israel babaen kenni Malakias.
Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.
2 “Inayatkayo,” kuna ni Yahweh. Ngem kunayo, “Kasanonakami nga inayat?” “Saan kadi a kabsat ni Jacob ni Esau?” kuna ni Yahweh.
Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’” Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo,
3 “Ngem inayatko ni Jacob, idinto a ginurak ni Esau. Pinagbalinko a langalang dagiti bantayna, ket pinagbalinko ti tawidna a lugar dagiti atap nga aso ti let-ang.”
koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”
4 No kuna ti Edom, “Naabaktayo, ngem agsublitayo ket bangonentayo dagiti nadadael;” Kuna ni Yahweh a Mannakabalin amin, “Ibangondanto, ngem duprakekto; ket panagananto ida dagiti lallaki a 'Ti pagilian iti kinadangkes; ken 'Dagiti tattao a kaunget ni Yahweh iti agnanayon.''
Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.” Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya.
5 Maimatanganto daytoy dagiti mismo a matayo, ket kunaenyonto, “Naindaklan ni Yahweh iti labes dagiti beddeng ti Israel.”
Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’
6 Raemen ti anak ti amana, ken raemen ti adipen ti amona. Ngarud, no maysaak nga ama, ayanna ti dayawko? Ken no maysaak nga amo, ayanna ti panagraem nga agpaay kaniak. Kasasaonakayo ni Yahweh a Mannakabalin amin, dakayo a papadi, a nangum-umsi iti naganko. Ngem kunaenyo, 'Kasanomi koma nga inumsi ti naganmo?'
“Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’
7 Babaen iti panangidatonyo iti narugit a tinapay iti rabaw ti altarko. Ket kunaenyo, 'Kasano koma a rinugitandaka?' Iti panangibagayo iti dayta nalabit a naumsi ti lamisaan ni Yahweh.
“Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’ “Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka.
8 No mangisagutkayo kadagiti bulsek nga ayup a maidaton, saan kadi a dakes dayta? Ken no mangidatonkayo iti pilay ken masakit, saan kadi a dakes dayta? Isagutyo dayta iti gobernadoryo; awatennakayo ngata wenno pakitaannakayo ngata iti pabor?” kuna ni Yahweh a Mannakabalin amin.
Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
9 Ket ita, agkiddawkayo iti pabor ti Dios, tapno paraburannatayokoma. “Babaen iti bukbukodyo a daton, awatenna ngata a siaayat ti siasinoman kadakayo?” kuna ni Yahweh a mannakabalin amin.
“Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
10 “O, no adda la koma maysa kadakayo a mabalin a mangrikep kadagiti ruangan ti templo, tapno saan koma a masayang ti panangarunyo iti rabaw ti altarko! Saanak a maay-ayo kadakayo,” kuna ni Yahweh a Mannakabalin amin, “ken saankonto nga awaten ti aniaman a daton manipud kadakayo.
“Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu.
11 Ta manipud iti panagsingising ti init agingga a lumnek daytoy, maitan-okto ti naganko kadagiti nasion; iti tunggal disso, maidatonto dagiti insenso iti naganko, kasta met ti nadalus a daton. Ta agbalinto a naindaklan ti naganko kadagiti nasion,” kuna ni Yahweh a Mannakabalin amin.
Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
12 Ngem saanyo a raraemen daytoy no ibagayo a narugitan ti lamisaan ti Apo, dagiti bunga ken taraon daytoy ket maumsi.
“Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’
13 Ibagbagayo pay, 'Makabannog unay daytoyen,' ken siuumsiyo nga ibang-es daytoy,” kuna ni Yahweh a Mannakabalin amin. “Inyegyo ti nakimmeg dagiti atap nga ayup wenno pilay wenno masakit; ket inyegyo daytoy a kas datonyo! Rumbeng kadi nga awatek daytoy manipud kadakayo?” kuna ni Yahweh.
Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova.
14 “Mailunod koma dagiti manangallilaw nga addaan iti kalakian nga ayup iti arbanna ken agsapsapata nga itedna daytoy kaniak, ngem nangidaton kaniak, nga Apo, iti adda pakapilawanna; ta Siak ti naindaklan nga Ari,” kuna ni Yahweh a Mannakabalin amin, “ken pagbutbutngan ti naganko kadagiti nasion.”
“Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’”

< Malakias 1 >