< Levitico 7 >

1 Daytoy ti linteg iti daton a pangsupapak iti biddut. Kasasantoan daytoy.
“‘Malamulo a nsembe yopepesera kupalamula imene ndi nsembe yopatulika kwambiri ndi awa:
2 Masapul a papatayenda ti daton a pangsupapak ti biddut iti disso a pangpatpatayanda iti daytoy, ken masapul nga iwarsida ti darana iti tunggal sikigan ti altar.
Nsembe yopepesera machimo iziphedwa pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza ndipo awaze magazi ake mbali zonse za guwa.
3 Amin a taba iti daytoy ket maidatonto; ti nalukmeg nga ipus, ti taba a nangbalkot kadagiti lalaem,
Tsono apereke mafuta ake onse: mchira wamafuta ndi mafuta amene amakuta matumbo.
4 ti dua a bekkel ken ti taba nga adda kadakuada, a kaabay ti lumo, ken ti mangbalbalkot ti dalem, agraman kadagiti bekkel - masapul a maikkatto amin daytoy.
Aperekenso impsyo ziwiri, mafuta ake pamodzi ndi mafuta onse amene ali chamʼchiwuno, ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi.
5 Masapul a puoran ti padi dagitoy a paset iti rabaw ti altar a kas maysa a daton a mapuoran para kenni Yahweh. Daytoy ti daton a pangsupapak iti biddut.
Wansembe azitenthe pa guwa kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, yoperekedwa kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo lopalamula.
6 Tunggal lalaki kadagiti papadi ket mabalin a mangan iti daytoy a daton. Masapul a kanenda daytoy iti nasantoan a disso gapu ta kasasantoan daytoy.
Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kudyako nsembeyo koma adyere ku malo opatulika. Imeneyi ndi nsembe yopatulika kwambiri.
7 Ti daton a gapu iti basol ket kas met laeng iti daton a pangsupapak iti biddut. Agpada a linteg ti maaramat kadagitoy a dua. Kukua ida ti padi a mangar-aramid iti seremonia ti panangabbong kadakuada.
“‘Nsembe yopepesera tchimo lopalamula ndi yofanana ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo. Ndipo nsembe ziwiri zonsezi zili ndi lamulo limodzi lokha. Wansembe amene wachita mwambo wa nsembe yopepesera machimo a kupalamula atenge nyamayo ngati yake.
8 Ti padi a mangidaton iti daton a maipuor amin a kukua ti maysa a tao ket mabalinna nga alaen ti lalat dayta daton a para iti bagina.
Wansembe wopereka nsembe yopsereza ya munthu wina aliyense, atenge chikopa cha nsembe yopserezayo kuti chikhale chake.
9 Tunggal daton a bukbukel a nailuto iti horno, ken tunggal kasta a daton a nailuto iti pariok wenno iti bandeha ti horno ket kukuanto ti padi a mangidaton iti daytoy.
Chopereka chilichonse cha chakudya chophika mu uvuni kapena chokazinga mu mʼphika kapena mu chiwaya ndi cha wansembe amene wapereka nsembezo.
10 Tunggal daton a bukbukel, namaga man wenno nalaokan iti lana, ket agpapadanto a kukua dagiti amin a kaputotan ni Aaron.
Ndipo chopereka china chilichonse cha chakudya chosakaniza ndi mafuta kapena chowuma, chikhale cha ana onse a Aaroni ndipo anawo achigawane mofanana.
11 Daytoy ti linteg iti daton a pakikapia nga idatonto dagiti tattao kenni Yahweh.
“‘Malamulo a nsembe ya chiyanjano imene munthu angathe kupereka kwa Yehova ndi awa:
12 No idaton ti siasinoman daytoy tapno agyaman, masapul ngarud nga idatonna daytoy a buyugen ti sakripisio a tinapay a naaramid nga awan lebadurana, ngem nalaokan iti lana, ti tinapay a naaramid nga awan lebadurana, ngem napulagidan iti lana, ken ti tinapay a naaramid manipud iti kasasayaatan nga arina a nalaokan iti lana.
“‘Ngati munthuyo apereka chifukwa cha kuthokoza, apereke nsembeyo pamodzi ndi makeke wopanda yisiti, osakaniza ndi mafuta; timitanda ta buledi wopanda yisiti, topyapyala, topaka mafuta, ndiponso makeke a ufa wosalala wophikidwa bwino, wosakaniza ndi mafuta.
13 Kasta met, maipaay iti panagyaman, masapul nga idatonna a kadua ti datonna a pakikapia ti tinapay a naaramid nga adda ti lebadurana.
Pamodzi ndi nsembe yachiyanjano yothokozerayo abwerenso ndi makeke opangidwa ndi yisiti ngati chopereka chake.
14 Masapul a mangidaton isuna iti maysa ti tunggal kita dagitoy a sakripisio a kas daton a maidatag kenni Yahweh. Kukuanto daytoy dagiti papadi a nangiwarsi iti dara dagiti daton a pakikapia iti altar.
Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano.
15 Ti tao a mangidatag iti daton a pakikapia a maipaay iti panagyaman ket masapul a kanenna ti karne ti datonna iti aldaw ti panangidatonna. Masapul a saan isuna a mangibati iti aniaman iti daytoy agingga iti sumaruno a bigat.
Nyama ya nsembe yachiyanjano yothokozera idyedwe pa tsiku lomwe nsembeyo yaperekedwa ndipo isatsaleko mpaka mmawa.
16 Ngem no ti datonna ket para iti panangtungpalna iti maysa a sapata, wenno daton a nagtaud iti bukodna a nakem, ti karne ket masapul a makan iti aldaw iti panangidatonna, ngem aniaman a matda iti daytoy ket mabalinto a kanen iti sumaruno nga aldaw.
“‘Koma ngati nsembe yakeyo apereka chifukwa cha lumbiro kapena mwaufulu, nsembeyo adye tsiku lomwe yaperekedwalo. Koma yotsala angathe kuyidya mmawa mwake.
17 Nupay kasta, aniaman a karne a mabati iti daton iti maikatlo nga aldaw ket masapul a mapuoran.
Ngati nyama ina ya nsembe yatsalabe mpaka tsiku lachitatu, imeneyo itenthedwe pa moto.
18 No ti aniaman a karne iti daton a pakikappia ti maysa a tao ket nakan iti maikatlo nga aldaw, saanto a maawat daytoy, wenno saanto a maibilang daytoy iti nangidaton. Makarimonto daytoy a banag, ket ti tao a nangan iti daytoy ket ikaronanto ti nagbasolanna.
Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo.
19 Aniaman a karne a maisagid iti narugit a banag ket masapul a saan a kanen. Masapul a mapuoran daytoy. Maipanggep kadagiti dadduma a karne, ti siasinoman a nadalus ket mabalin a mangan iti daytoy.
“‘Nyama imene yakhudza chilichonse chodetsedwa, munthu asayidye, koma itenthedwe pa moto. Aliyense amene ali woyeretsedwa angathe kudya nyama inayo.
20 Nupay kasta, ti maysa a tao a narugit a mangan iti aniaman a karne manipud iti daton a pakikapia a kukua ni Yahweh - dayta a tao ket masapul a mailaksid manipud kadagiti tattaona.
Koma ngati munthu wina amene ndi wosayeretsedwa adya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.
21 No masagid ti siasinoman ti aniaman a narugit a banag - kinarugit man daytoy ti tao, wenno ti narugit nga ayup, wenno iti aniaman a narugit ken makarimon a banag, ket no mangan isuna iti karne iti daton a pakikapia a kukua ni Yahweh, dayta a tao ket masapul a mailaksid manipud kadagiti tattaona.”
Ndipo ngati munthu wina akhudza chinthu chodetsedwa, kaya chonyansa cha munthu kapena cha nyama, kapenanso chonyansa china chilichonse, ndipo kenaka nʼkudya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati anthu a mtundu wake.’”
22 Ket nagsao ni Yahweh kenni Moises a kunana,
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
23 “Kasaritam dagiti tattao ti Israel ket ibagam, 'Masapul a saankayo a mangan iti taba ti baka wenno karnero wenno kalding.
“Awuze Aisraeli kuti, ‘Musadye mafuta a ngʼombe, nkhosa kapenanso mbuzi.
24 Ti taba ti maysa nga ayup a natay a saan a naisakripisio, wenno ti taba ti ayup a rinangrangkay dagiti naaatap nga ayup, ket mabalin a maaramat para iti sabali a pakaipaayanna, ngem masapul a saanyonto pulos a kanen daytoy.
Mafuta a nyama yofa yokha, kapena mafuta a nyama yophedwa ndi zirombo akhoza kuwagwiritsa ntchito iliyonse, koma inu musadye mafuta amenewo.
25 Ti siasinoman a mangan iti taba ti maysa nga ayup a mabalin nga idaton dagiti tattao kenni Yahweh a kas daton a maipuor, dayta a tao ket masapul a mailaksid kadagiti tattaona.
Pakuti munthu wakudya mafuta a nyama yoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe yotentha pa moto, ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
26 Masapul a saankayo a mangan iti aniaman a dara iti sadinoman iti balayyo, nagtaud man daytoy iti billit wenno ayup.
Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse.
27 Ti siasinoman a mangan iti aniaman a dara, dayta a tao ket masapul a mailaksid manipud kadagiti tattaona.”'
Ngati munthu aliyense adya magazi achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.’”
28 Isu a nagsao ni Yahweh kenni Moises ket kinunana,
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
29 “Kasaritam dagiti tattao ti Israel ket ibagam, 'Ti mangidatag iti daton a pakikapia kenni Yahweh ket masapul a mangiyeg iti paset iti sakripisiona kenni Yahweh.
“Awuze Aisraeli kuti, Aliyense amene apereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, abwere ndi gawo la nsembeyo kwa Yehova.
30 Ti daton a mapuoran a para kenni Yahweh ket masapul nga iyegna babaen kadagiti bukodna nga ima. Masapul nga iyegna ti taba agraman ti barukong, tapno ti barukong ket agabalinto a daton a maitag-ay iti sangoanan ni Yahweh ken maidatag kenkuana.
Atenge ndi manja ake zigawo za chopereka zoyenera kuzitentha pa moto ngati chopereka kwa Yehova. Abweretse mafuta, pamodzi ndi chidale chomwe, ndipo chidalecho achiweyule kuti chikhale chopereka choweyula kwa Yehova.
31 Masapul a puoran ti padi ti taba iti rabaw ti altar, ngem ti barukong ket kukuanto ni Aaron ken dagiti kaputotanna.
Wansembe atenthe mafutawo pa guwa koma chidalecho chikhale cha Aaroni ndi ana ake.
32 Masapul nga itedyo iti padi ti makannawan a luppo a kas maysa a daton a maidatag manipud kadagiti datonyo a pakikapia.
Mumupatse wansembe ntchafu ya kumanja ya nsembe yanu yachiyanjano kuti ikhale chopereka chanu kwa iye.
33 Ti padi, a maysa kadagiti kaputotan ni Aaron, a mangidaton ti dara dagiti daton a pakikapia ken ti taba - maitedto kenkuana ti makannawan a luppo a kas bingayna manipud iti daton.
Mwana wa Aaroni amene amapereka magazi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano, adzitenga ntchafu ya kumanja kukhala gawo lake.
34 Ta innalak ti daton a barukong ken luppo a naitag-ay ken naidatag kaniak, ket intedko dagitoy kenni Aaron, ti kangatoan a padi, ken kadagiti kaputonanna; kankanayonto a daytoy ti bingayda manipud kadagiti daton a pakikapia nga aramiden dagiti tattao ti Israel.
Choncho pa zopereka zachiyanjano za Aisraeli, Ine ndatengapo chidale chomwe amaweyula ndi ntchafu zimene amapereka nsembe ndipo ndazipereka kwa wansembe Aaroni ndi ana ake. Izi ndizo gawo lawo nthawi zonse pa zopereka za Aisraeli.”
35 Daytoy ti bingay a para kenni Aaron ken dagiti kaputotanna manipud kadagiti daton a maipuor a para kenni Yahweh, iti aldaw nga indatag ni Moises ida nga agserbi kenni Yahweh iti saad a kinapadi.
Zimenezi ndi chigawo cha Aaroni ndi ana ake chotapidwa pa zopereka kwa Yehova zoti zitenthedwe pa moto zimene zinaperekedwa pa tsiku limene anapatulidwa kuti akhale ansembe otumikira Yehova.
36 Daytoy ti bingay nga imbilin ni Yahweh a maited kadakuada a naggapu kadagiti tattao ti Israel, iti aldaw a pinulotanna dagiti papadi. Kankanayonto daytoy a bingayda iti amin a henerasion.
Yehova ndiye analamulira kuti pa zopereka za Aisraeli azitapapo zimenezi ndi kuwapatsa ansembe ngati gawo lawo. Yehovayo analamula zimenezi pa tsiku limene ansembewo anapatulidwa ndipo anachikhazikitsa ngati lamulo la nthawi zonse.
37 Daytoy ti linteg ti daton a maipuor amin, ti daton a bukbukel, ti daton a gapu iti basol, ti daton a pangsupapak iti biddut, ti daton a para iti panakakonsagrar, ken dagiti daton a pakikapia,
Awa ndi malamulo a nsembe izi: nsembe yopsereza, nsembe yachakudya, nsembe yopepesera machimo, nsembe yopepesera kupalamula, nsembe ya mwambo wodzoza ndi nsembe yachiyanjano.
38 nga imbilin ni Yahweh kenni Moises iti Bantay Sinai iti aldaw nga imbilinna kadagiti tattao ti Israel nga idatonda dagiti sakripisoda kenni Yahweh iti let-ang ti Sinai.”'
Malamulo amenewa Yehova anapereka kwa Mose pa Phiri la Sinai pa tsiku limene Yehova analamulira Aisraeli kuti abwere ndi zopereka za kwa Yehova, ku chipululu cha Sinai kuja.

< Levitico 7 >