< Levitico 13 >
1 Nagsao ni Yahweh kada Moises ken Aaron, kinunana,
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
2 “No ti maysa a tao ket adda lumlumteg iti kudilna, wenno aggadgaddil, wenno adda nasileng a kabiteg ket nagbalin a makaakar, ken adda ti sakit ti kudilna, ket masapul a maipan isuna kenni Aaron, ti nangato a padi wenno iti maysa kadagiti putotna a lallaki a padi.
“Munthu akakhala ndi chithupsa, kapena mʼbuko, kapena chikanga pa thupi lake chimene chitha kusanduka nthenda ya khate, abwere naye munthuyo kwa Aaroni wansembe kapena kwa mmodzi mwa ana ake amene ndi ansembe.
3 Ket kitaen ti padi ti sakit ti kudilna. No pimmuraw ti buok iti masakit a paset ti kudilna, ken no naun-uneg ti masakit a paset ngem ti kudil, ket makaakar daytoy a sakit. Kalpasan a kinita isuna ti padi, masapul nga ipakaammona a narugit isuna.
Tsono wansembe ayangʼanitsitse nthendayo pa khungupo, ndipo ngati ubweya wa pamalo pamene pali nthendapo wasanduka woyera, komanso kuti nthendayo yazama mʼkati kupitirira khungu, ndiye kuti nthendayo ndi khate. Wansembe akamuonetsetsa alengeze kuti ndi wodetsedwa.
4 No ti nasileng a kabiteg iti kudilna ket puraw, ken saan a naun-uneg ti langana ngem ti kudil, ken no saan a pimmuraw ti buok iti masakit a paset, ket masapul nga ilasin ti padi dayta a tao nga addaan iti sakit iti pito nga aldaw.
Ngati chikanga cha pa khungulo chikuoneka choyera, ndipo kuya kwake sikukuonekera kuti kwapitirira khungu ndi ubweya wake pamalopo sunasanduke woyera, wansembe amuyike wodwalayo padera kwa masiku asanu ndi awiri.
5 Iti maikapito nga aldaw, masapul a kitaen ti padi isuna tapno makitana a no iti kapanunotanna ket saan a kimmaro ti sakit ken no saan a nagwaras daytoy iti kudil. No saan a nagwaras daytoy, ket masapul nga ilasin ti padi isuna iti pito pay nga aldaw.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso bwino wodwalayo. Ndipo ngati waona kuti nthendayo sinasinthe ndipo sinafalikire pa khungu, amuyikenso wodwalayo padera kwa masiku ena asanu ndi awiri.
6 Kitaen manen isuna ti padi iti maikapito nga aldaw tapno makitana no simmayaaten ti sakit ken saan nga ad-adda a nagwaras iti kudil. No saan a nagwaras daytoy, ket ipakaammo ti padi a nadalus isuna. Gagatel daytoy. Masapul a labaanna dagiti kawesna ket nadaluston isuna.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembeyo amuonenso bwino munthuyo, ndipo ngati nthendayo yazima ndi kusafalikira pa khungu, wansembe amutchule munthuyo kuti ndi woyera. Umenewo unali mʼbuko chabe. Choncho munthuyo achape zovala zake ndipo adzakhala woyera.
7 Ngem no nagwaras ti gagatel iti kudil kalpasan nga imparangna ti bagina iti padi para iti pannakadalusna, masapul nga iparangna manen ti bagina iti padi.
Koma ngati mʼbukowo ufalikira pakhungu atakadzionetsa kale kwa wansembe ndipo wansembeyo nʼkulengeza kuti munthuyo ndi woyeretsedwa, ndiye kuti apitenso kukadzionetsa kwa wansembeyo.
8 Kitaen ti padi isuna tapno makitana no ad-adda pay a nagwaras ti gagatel iti kudil. No nagwaras daytoy, ket masapul nga ipakaammo ti padi a narugit isuna. Makaakar daytoy a sakit.
Wansembe amuonetsetsenso munthuyo, ndipo ngati mʼbukowo wafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa ndi kuti nthendayo ndi khate.
9 No ti makaakar a sakit ket adda iti maysa a tao, ket masapul a maipan isuna iti padi.
“Ngati munthu aliyense ali ndi nthenda ya pakhungu yoyipitsa thupi, wodwalayo abwere naye kwa wansembe.
10 Kitaen ti padi isuna tapno makitana no adda ti puraw a lumlumteg iti kudilna, no pimmuraw ti buok, wenno no adda ti saan pay nga naimbag a lasag iti lumlumteg a kudilna.
Wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati ali ndi chithupsa chamaonekedwe woyera pa khungupo chimene chasandutsa ubweya wa pamalopo kukhala woyera, ndipo ngati pali zilonda pa chotupacho,
11 No adda, ket nakaro unay a sakit ti kudil daytoy, ket masapul nga ipakaammo ti padi a narugit isuna. Saanna nga ilasin isuna gapu ta narugiten isuna.
limenelo ndi khate lachikhalire la pa khungu, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Asamutsekere munthu woteroyo pakuti ndi wodetsedwa kale.
12 No nagwaras ti sakit ket kinallubanna ti amin a kudil ti masakit a tao manipud iti ulona agingga iti sakana, a kas makita ti padi,
“Ndipo ngati, mʼkuona kwa wansembe, khate lija lafalikira pa khungu lonse moti lamugwira thupi lonse kuyambira kumutu mpaka kumapazi,
13 ket masapul a kitaen isuna ti padi tapno makitana no nagwaras ti sakit ti intero a bagina. No nagwaras daytoy, masapul nga ipakaammo ti padi a nadalus ti masakit a tao. No pimmuraw amin dagitoy, ket nadalus isuna.
wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati khatero lagwira thupi lake lonse, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Popeza kuti thupi lonse lasanduka loyera, munthuyo ndi woyeretsedwa.
14 Ngem no adda ti agparparang a saan pay a naimbag a lasag kenkuana, narugit isuna.
Koma pa tsiku limene zilonda zidzaoneka pa iye, munthuyo adzakhala wodetsedwa.
15 Masapul a kitaen ti padi ti saan pay a naimbag a lasag ken ipakaammona a narugit isuna gapu ta narugit ti saan pay a naimbag a lasag. Makaakar daytoy a sakit.
Wansembe aonetsetse zilondazo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zilondazo ndi zodetsedwa ndipo ili ndi khate.
16 Ngem no pimmuraw manen ti saan pay a naimbag a lasag, ket masapul a mapan dayta a tao iti padi.
Koma zilondazo zikasinthika ndi kusanduka zoyera, munthuyo ayenera kupita kwa wansembe.
17 Kitaen ti padi isuna tapno makitana no pimmuraw ti lasag. No pimmuraw daytoy, ipakaammo ti padi a nadalus dayta a tao.
Wansembe amuonetsetse ndipo ngati zilondazo zasanduka zoyera, wansembe amutchule wodwalayo kuti ndi woyera ndipo adzakhala woyera ndithu.
18 No ti maysa a tao ket adda ti litteg iti kudilna ken naimbaganen,
“Ngati pa khungu la munthu wodwalayo pali chithupsa chimene chinapola kale,
19 ken iti ayan ti litteg ket adda iti lumlumteg a pumuraw wenno nasileng a kabiteg, a lumabaga a puraw, ket masapul a maipakita daytoy iti padi.
ndipo pamalo pamene panali chithupsacho pakatuluka chotupa choyera kapena banga loyera mofiirira, munthuyo ayenera kukadzionetsa kwa wansembe.
20 Kitaen ti padi daytoy tapno makita no naun-uneg ti langana ngem ti kudil ken no nagbalin a puraw ti buokna idiay. No kasta, ket masapul nga ipakaammo ti padi a narugit isuna. Makaakar daytoy a sakit, no nagtubo daytoy iti sigud nga ayan ti litteg.
Wansembe aonetsetse bwino ndipo ngati chikuoneka kuti chazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka woyera, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Imeneyo ndi nthenda ya khate imene yatuluka mʼchithupsacho.
21 Ngem no kinita ti padi daytoy ket nakitana nga awan iti puraw a buokna, ken saan a naun-uneg ngem ti kudil ket umim-imbagen, ket masapul nga ilasin isuna ti padi iti pito nga aldaw.
Koma ngati wansembe waonetsetsa napeza kuti palibe ubweya woyera ndipo chithupsacho sichinazame, koma chazimirira, wansembeyo amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
22 No nagwaras daytoy iti kudil, masapul nga ipakaammo ti padi a narugit isuna. Makaakar daytoy a sakit.
Ngati nthendayo ikufalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limeneli ndi khate.
23 Ngem no nagtalinaed ti nasileng a kabiteg iti ayanna ken saan a nagwaras, ngarud, piglat daytoy ti litteg ket masapul nga ipakaammo ti padi a nadalus isuna.
Koma bangalo likakhala malo amodzi, wosafalikira, chimenecho ndi chipsera cha chithupsacho, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera.
24 No nasinit ti kudil ken ti saan pay a naimbag a lasag ti paset a nasinit ket nagbalin a lumabaga a puraw wenno pimmuraw,
“Munthu akakhala ndi bala lamoto pa khungu lake, ndipo chilonda cha balalo chikasanduka banga loyera mofiirira kapena loyera,
25 ket masapul a kitaen ti padi daytoy tapno makitana no pimmuraw ti buok iti dayta a paset ken no agparang a naun-uneg ngem ti kudil. No kasta, makaakar ngarud daytoy a sakit. Timmubo daytoy iti nasinit a paset ket masapul nga ipakaammo ti padi a narugit isuna. Makaakar daytoy a sakit.
wansembe aonetsetse bangalo, ndipo ngati ubweya wa pa bangapo usanduka woyera, ndipo balalo lioneka kuti ndi lozama, limenelo ndi khate lomwe latuluka pa balalo. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate la pa khungu.
26 Ngem no kinita ti padi daytoy ket naduktalanna nga awan ti puraw a buok iti nasinit a paset, ken saan a naun-uneg ngem ti kudil ket umim-imbagen, masapul nga ilasin isuna ti padi iti pito nga aldaw.
Koma ngati wansembe waonetsetsa balalo ndipo palibe ubweya woyera, ndipo ngati balalo silinazame ndi kuti lazirala, wansembe amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
27 Kalpasanna, masapul a kitaen ti padi isuna iti maikapito nga aldaw. No nagwaras daytoy iti kudil, ket masapul nga ipakaammo ti padi a narugit isuna. Makaakar daytoy a sakit.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso wodwalayo, ndipo ngati bangalo lafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate.
28 No nagtalinaed laeng ti nasinit a paset iti ayanna ken saan a nagwaras iti kudil ket umim-imbagen, ngarud, lumlumteg laeng daytoy gapu iti pannakasinitna ket masapul nga ipakaammo ti padi a nadalus isuna, ta piglat laeng daytoy gapu ti pannakasinit.
Koma ngati bangalo likhala pa malo amodzi wosafalikira pa khungu, ndipo lazimirira, limenelo ndi thuza la bala lamoto, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Chimenecho ndi chipsera chamoto.
29 No ti maysa a lalaki wenno babai ket addaan iti makaakar a sakit iti ulo wenno timid,
“Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi nthenda kumutu kapena ku chibwano,
30 ket masapul a kitaen ti padi dayta a tao para iti makaakar a sakit tapno kitaenna no agparparang daytoy a naun-uneg ngem ti kudil, ken no adda ti duyaw a naingpis a buokna daytoy. No adda, masapul nga ipakaammo ti padi a narugit isuna. Gagatel daytoy, maysa a makaakar a sakit iti ulo wenno timid.
wansembe aonetsetse balalo ndipo likaoneka kuti lazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka wachikasu ndi wonyololoka, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zimenezo ndi mfundu zonyerenyetsa, khate lakumutu kapena ku chibwano.
31 No kinita ti padi ti gagatel ket nakitana a saan daytoy a naun-uneg ngem ti kudil, ken no awan ti nangisit a buokna daytoy, ket ilasin ti padi ti tao nga addaan ti gagatel iti pito nga aldaw.
Koma wansembe akaonetsetsa mfundu zonyerenyetsazo, ndipo zikaoneka kuti sizinazame ndi kuti palibe ubweya wakuda, wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku asanu ndi awiri.
32 Iti maikapito nga aldaw, masapul a kitaen ti padi ti sakit tapno makitana no nagwaras daytoy. No awan ti duyaw a buokna, ken no agparparang a narabaw laeng ti sakit,
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo, ndipo ngati sizinafalikire ndipo palibe ubweya wachikasu pamalopo ndiponso sizinazame,
33 masapul a makuskusan isuna, ngem masapul a saan a makuskusan ti masakit a paset, ket masapul nga ilasin ti padi ti tao nga addaan iti gagatel iti pito pay nga aldaw.
wodwalayo ametedwe, koma pamene pali mfunduyo pasametedwe. Wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
34 Iti maikapito nga aldaw kitaen ti padi ti sakit tapno makitana no nagsardengen ti panagwarasna iti kudil. No saan a naun-uneg ti langana daytoy ngem ti kudil, ket masapul nga ipakaammo ti padi a nadalus isuna. Masapul a labaan dayta a tao dagiti kawesna ket agbalinton isuna a nadalus.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo ndipo ngati sizinafalikire pa khungu ndi kuti sizinazame, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Tsono achape zovala zake, ndipo adzakhala woyera.
35 Ngem no nagwaras ti sakit a gagatel iti kudil kalpasan nga imbaga ti padi a nadalus isuna,
Koma mfundu zonyerenyetsazo zikafalikira pa khungu, wansembe atalengeza kuti ndi woyera,
36 ket masapul a kitaen manen isuna ti padi. No nagwaras ti sakit iti kudil, saanen a kasapulan ti padi a mangsapul iti duyaw a buok. Ti tao ket narugit.
wansembe amuonetsetsenso wodwalayo ndipo ngati mfunduzo zafalikira pa khungu, iye asalabadirenso zoyangʼana ngati ubweya uli wachikasu. Munthuyo ndi wodetsedwa.
37 Ngem no iti panagkita ti padi ket nagsardengen nga agwaras ti gagatel ken addan ti nagtubo a nangisit a buok iti masakit a paset, naimbagen ngarud ti gagatel. Nadalus isuna ken masapul nga ipakaammo ti padi a nadalus isuna.
Koma ngati wansembe waonetsetsa kuti mfunduzo sizinasinthe ndipo ubweya wakuda wamera pa mfundupo, ndiye kuti wodwalayo wachira. Tsono wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa.
38 No ti maysa a lalaki wenno babai ket addaan kadagiti puraw a labang ti kudil,
“Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi mawanga woyera pa khungu,
39 masapul a kitaen ti padi dayta a tao tapno makitana no dagiti labang ket nalitem a puraw, a maysa laeng a gagatel a nagtubo iti kudil. Nadalus isuna.
wansembe aonetsetse mawangawo, ndipo ngati ali otuwa, ndiye kuti ndi mibuko chabe yotuluka pa khungu. Munthuyo ndi woyera.
40 No nagregreg ti buok ti tao manipud iti ulona, makalkalbo isuna, ngem nadalus isuna.
“Tsitsi la munthu likayoyoka kumutu ndiye kuti ndi dazi limenelo koma munthuyo ndi woyeretsedwa.
41 Ken no nagregreg ti buok iti sangoanan ti ulona, ken no kalbo ti mugingna, nadalus isuna.
Ngati tsitsi lake layoyoka chapamphumi ndiye kuti ndi dazi la pa chipumi limenelo koma munthuyo ndi woyera.
42 Ngem no adda ti gaddil a lumabaga a puraw iti kalbo nga ulona wenno mugingna, makaakar daytoy a sakit a nagtubo.
Koma ngati pa dazi la pamutu kapena la pa chipumi pakhala chithupsa choyera mofiirira, ndiye kuti ndi khate limenelo lochokera mu dazi la pamutu lija kapena pa chipumi lija.
43 Ket masapul a kitaen isuna ti padi tapno makitana no ti lumlumteg iti masakit a paset iti kalbo nga ulona wenno iti mugingna ket lumabaga a puraw, kas iti langa ti makaakar a sakit iti kudil.
Tsono wansembe amuonetsetse wodwalayo ndipo ngati chithupsa cha pa dazi lapankhongo kapena pa dazi lapachipumicho ndi choyera mofiirira monga nthenda ya khate imaonekera,
44 No kastoy, ket addaan isuna ti makaakar a sakit ket narugit isuna. Masapul a siguraduen ti padi nga ipakaammo a narugit isuna gapu iti sakit nga adda iti ulona.
ndiye kuti munthuyo ali ndi khate, motero ndi wodetsedwa. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa chifukwa cha chithupsa cha pamutu pakepo.
45 Ti tao nga addaan iti makaakar a sakit ket masapul nga agisuot kadagiti napigis a kawkawes, masapul a nakawakray ti buokna, ken masapul a kallubanna ti rupana agingga iti agungna ket ipukkawna ti 'Narugit, narugit.'
“Munthu wa khate lotere avale sanza, tsitsi lake alilekerere, aphimbe mlomo wake wapamwamba ndipo azifuwula kuti, ‘Ndine wodetsedwa, ndine wodetsedwa!’
46 Kadagiti amin nga aldaw nga addaan isuna iti makaakar a sakit ket narugit isuna. Gapu ta narugit isuna nga addaan iti makaakar a sakit, masapul nga agbiag isuna nga agmaymaysa. Masapul nga agnaed isuna iti ruar ti kampo.
Munthu wodwalayo adzakhala wodetsedwa kwa nthawi yonse imene ali ndi nthendayo. Iye ayenera kumakhala payekha kunja kwa msasa.
47 Ti lupot a nagbuot, naaramid man daytoy iti dutdut ti ayup wenno lino a lupot,
“Nsalu iliyonse ikakhala ndi nguwi,
48 wenno aniaman a nalaga wenno nagansilyo a dutdut ti ayup wenno lino, wenno lalat wenno aniaman a banag a naaramid ti lalat—
kaya ndi chovala chopangidwa ndi nsalu yathonje kapena yaubweya, yoluka ndi thonje kapena ubweya, yachikopa kapena yopangidwa ndi chikopa,
49 no adda ti kasla maris bulong wenno lumabaga a buot iti lupot, ti lalat, ti nalaga wenno nagansilyo a banag, wenno aniaman a banag a naaramid iti lalat, ket buot daytoy a nagwaras; masapul a maipakita daytoy iti padi.
ndipo ngati pamalo pamene pachita nguwiyo pali ndi maonekedwe obiriwira kapena ofiirira imeneyo ndi nguwi yoyipitsa chovala ndipo chovalacho chikaonetsedwe kwa wansembe.
50 Masapul a kitaen ti padi daytoy a banag para iti buot; masapul nga ilasinna ti aniaman a banag nga addaan iti buot iti pito nga aldaw.
Wansembeyo ayionetsetse nguwiyo ndipo chovalacho achiyike padera kwa masiku asanu ndi awiri.
51 Masapul a kitaenna manen ti buot iti maikapito nga aldaw. No nagwaras daytoy iti lupot wenno aniaman a banag a nalaga wenno nagansilio a dutdut ti ayup wenno lino, wenno lalat wenno aniaman a banag a nakaaramatan ti lalat, ngarud makadadael daytoy a buot, ket dayta a banag ket narugit.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri ayionetsetsenso nguwiyo ndipo ngati nguwiyo yafalikira pa chovalacho, chathonje kapena chaubweya, kapena pa chikopacho, kaya ndi cha ntchito ya mtundu wanji, imeneyo ndi nguwi yoopsa ndipo chovalacho ndi chodetsedwa.
52 Masapul a puoranna ti lupot, wenno aniaman a banag a nalaga wenno nagansilio a dutdut ti ayup wenno lino, wenno lalat wenno aniaman a banag a naaramid iti lalat, aniaman a banag a nakasakaran iti makadadael a buot, ta mabalin a pagrugian daytoy iti sakit. Masapul a mapuoran a naan-anay daytoy a banag.
Wansembe atenthe chovala chathonje kapena chaubweya chija, ngakhalenso chinthu chachikopa chija popeza nguwiyo yachidetsa. Nguwiyo ndi yoopsa choncho chinthucho achitenthe.
53 No kinita ti padi daytoy a banag ket nakitana a saan a nagwaras ti buot iti lupot wenno iti banag a nalaga wenno nagansilio a dutdut ti ayup wenno lino, wenno kadagiti banag a naaramid iti lalat,
“Koma ngati wansembe akayangʼanitsitsa nguwiyo apeza kuti sinafalikire pa chovalacho kapena pa chinthu chilichonse chachikopa,
54 ket bilinenna ida a labaanda ti banag a nakasarakan iti buot, ken masapul nga ilasinna daytoy iti pito pay nga aldaw.
iye alamulire kuti chinthu choyipitsidwacho achichape. Akatero achiyike padera kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
55 Kalpasanna, kitaen ti padi dayta a banag kalpasan a nalabaan daytoy. No saan a nagbaliw ti maris ti buot uray no daytoy ket saan a nagwaras, daytoy ket narugit. Masapul a puoranyo dayta a banag, uray no sadinoman a paset ti nagbuot.
Chovalacho chitachapidwa, wansembe achionenso ndipo ngati nguwiyo sinasinthe maonekedwe ake, ngakhale kuti sinafalikire, chovalacho ndi chodetsedwa ndithu. Muchitenthe, ngakhale kuti nguwiyo ili kumbuyo kapena kumaso kwa chinthucho.
56 No kinita ti padi dayta a banag, ken no napukaw ti buot kalpasan a nalabaan daytoy, ket masapul a pigisenna ti nagbuot a paset ti lupot wenno ti lalat, wenno ti nalaga wenno nagansilio a banag.
Koma ngati wansembe aonetsetsa nʼkupeza kuti nguwi ija yathimbirira pa chovala chija kapena pa chinthu chachikopa chija atachichapa, ndiye angʼambeko chinthucho pa banga la nguwiyo.
57 No adda pay laeng ti buot iti lupot, iti nalaga man wenno nagansilio a banag, wenno iti aniaman a banag a naaramid iti lalat, agwarwaras daytoy. Masapul a puoranyo ti aniaman a banag nga addaan iti buot.
Koma ngati nguwiyo iwonekanso pa chovala chathonje kapena chaubweya ndiye kuti nguwiyo ikufalikira. Chilichonse chimene chili ndi nguwi chiyenera kutenthedwa.
58 Ti lupot wenno aniaman a banag a nalaga wenno nagansilio a dutdut ti ayup wenno linen, wenno lalat wenno aniaman a banag a naaramid ti lalat- no nilabaanyo daytoy a banag ket napukaw ti buot, ket masapul a malabaan daytoy iti maikadua a daras, ket agbalinto daytoy a nadalus.
Chovala chathonje kapena chaubweya, ngakhale chinthu china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, mukachichapa nguwi yake nʼkuchoka muchichapenso kawiri ndipo chidzakhala choyeretsedwa.”
59 Daytoy ti linteg a maipapan iti buot iti lupot a dutdut ti ayup wenno lino, wenno aniaman a banag a nalaga wenno nagansilio a dutdut ti ayup wenno lino, wenno lalat wenno aniaman a banag a naaramid iti lalat, tapno maipakaamoyo daytoy a nadalus wenno narugit.”
Amenewa ndiwo malamulo a nguwi yokhala pa chovala chaubweya kapena pa chovala chathonje, kapenanso pa chinthu chilichonse chopangidwa ndi chikopa kuti muzitha kulekanitsa choyeretsedwa ndi chodetsedwa.