< Uk-ukom 16 >

1 Napan ni Samson idiay Gaza ket nakakita isuna sadiay iti maysa a balangkantis, ket nakikaidda isuna kenkuana.
Tsiku lina Samsoni anapita ku Gaza. Kumeneko anaonako mkazi wachiwerewere, ndipo analowa mu nyumba yake.
2 Naibaga kadagiti Gazita, “Immay ditoy ni Samson.” Linakub dagiti taga- Gaza ti lugar, ken nagpatpatnag nga inurayda isuna a nalimed iti ayan ti ruangan ti siudad. Naulimekda bayat iti nagpatnag. Ket kinunkunada, “Aguraytayo agingga iti aglawag, ket papatayentayo isuna.”
Anthu a ku Gaza anawuzidwa kuti, “Samsoni ali kuno!” Choncho anthuwo anazungulira malowo, kumubisalira usiku wonse ku chipata cha mzindawo. Iwo anakhala chete usiku wonse namanena kuti, “Tidzamupha mmamawa.”
3 Nagidda ni Samson agingga iti tengnga ti rabii. Bimmangon isuna iti tengnga ti rabii ket iniggamanna ti ruangan ti siudad ken dagiti dua a postena daytoy. Pinarutna dagitoy, ti balunet ken dagiti amin, binaklayna dagitoy nga impan iti tapaw ti turod, iti sango ti Hebron.
Koma Samsoni anangogonako mpaka pakati pa usiku. Kenaka pakati pa usiku anadzuka nagwira zitseko za chipata cha mzinda ndi maferemu ake awiri, ndipo anazizula zonse pamodzi ndi mpiringidzo womwe. Anazisenza pa mapewa pake napita nazo pamwamba pa phiri loyangʼanana ndi Hebroni.
4 Kalpasan daytoy ket nagayat ni Samson iti maysa a babai nga agnanaed idiay tanap ti Sorek. Ti naganna ket Delila.
Pambuyo pake, Samsoni anayamba kukonda mtsikana wina wa ku chigwa cha Soreki dzina lake Delila.
5 Immay kenkuana dagiti mangiturturay kadagiti Filisteo ket kinunada kenkuana, “Allilawem ni Samson tapno kitaem no sadino ti paggapgapuan iti pigsana, ket no ania a wagas a maabakmi isuna, tapno mareppettayo isuna tapno ibabaintayo isuna. Aramidem daytoy, ket tunggal maysa kadakami ket mangted kenka iti 1, 100 a pidaso ti pirak.”
Olamulira Afilisti anapita kwa mkaziyo ndipo anati, “Umunyengerere Samsoni kuti udziwe chinsinsi cha mphamvu zake zoopsazi, komanso ndi mmene ife tingamupambanire kuti timumange ndi kumugonjetsa. Ukatero aliyense wa ife adzakupatsa ndalama zasiliva 1,100.”
6 Ket kinuna ngarud ni Delila kenni Samson, “Pangaasim, ibagam kaniak no apay a napigsaka unay, ken no kasano a mareppetnaka ti maysa a tao tapno matengngelka?”
Choncho Delila anati kwa Samsoni, “Inu tandiwuzani pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi ndi mmene anthu akhoza kukumangirani kuti akugonjetseni.”
7 Kinuna ni Samson kenkuana, “No reppetendak babaen iti pito a sadiwa a lapnit ti bai ti pana a saan pay a nagango ket agkapsutakto ken agbalinak a kasla iti sabali a tao.”
Samsoni anamuyankha kuti, “Ngati wina atandimanga ndi zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndidzafowoka ndi kusanduka ngati munthu wina aliyense.”
8 Ket nangiyeg dagiti mangiturturay kadagiti Filisteo kenni Delila iti pito a sadiwa a lapnit ti bai ti pana a saan pay nagango, ket rineppetna ni Samson babaen kadagitoy.
Tsono atsogoleri a Afilisti aja anapita kwa mkazi uja namupatsa zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndipo mkaziyo anamanga nazo Samsoni.
9 Ita, addaan isuna kadagiti lallaki nga aglemlemmeng a nalimed iti makin-uneg a siledna. Kinuna kenkuana, “Samson! Umay kenka dagiti Filisteo!” Ngem pinugsatna dagiti lapnit ti bai iti pana a kasla maysa a sinulid no naidekket daytoy iti apoy. Ket saanda a naammoan ti palimed ti pigsana.
Nthawi imeneyo nʼkuti mkazi uja atayika anthu omubisalira mʼchipinda. Tsono anati kwa mwamuna wake, “Amuna anga, Afilisti aja afika!” Koma iye anangodula zingwe zija ngati mmene imadukira nkhosi ya chingwe ikamapsa. Choncho chinsinsi cha mphamvu zake sichinadziwike.
10 Ket kinuna ni Delila kenni Samson, “Kastoy iti panangallilawmo ken panangulbodmo kaniak. Pangaasim ta ibagam kaniak no kasanodaka a maparmek.”
Kenaka Delila anati kwa Samsoni, “Inu mwandipusitsa ndi kundiwuza zabodza. Chonde tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.”
11 Kinuna kenkuana, “No reppetendak babaen kadagiti barbaro a tali a saan pay a nausar ket agbalinakto a nakapsut ken kasla iti sabali a tao.”
Iye anati, “Ngati aliyense atandimanga ine ndi zingwe zatsopano zimene sanazigwiritseko ntchito, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala monga munthu wina aliyense.”
12 Nangala ngarud ni Delila kadagiti barbaro a tali ket inreppetna dagitoy kenkuana, ket kunana kenkuana, “Samson! Umay kenka dagiti Filisteo.” Dagiti lallaki nga agur-uray ket adda iti makin-uneg a siled. Ngem pinugsat ni Samson dagiti tali manipud kadagiti imana a kasla maysa dagitoy a sinulid.
Choncho Delila anatenga zingwe zatsopano namumanga nazo. Kenaka anati “Amuna anga, Afilisti aja afikanso!” Nthawi iyi nʼkuti anthu omubisalira aja ali mʼchipinda chamʼkati. Koma iye anadulanso zingwe mʼmanja ake ngati akudula ulusi wa thonje.
13 Kinuna ni Delila kenni Samson, “Agingga ita ket al-allilawennak ken ul-ulbodannak. Ibagam kaniak no kasanodaka a maparmek.” Kinuna ni Samson kenkuana, “No mangabelka iti pito a linabag iti buokko iti tela, ket ilansam dagitoy iti pagabelan, agbalinakto a kasla iti sabali a tao.”
Ndipo Delila anati kwa Samsoni, “Mpaka tsopano mwakhala mukundipusitsa ndi kumandiwuza zabodza. Chonde, tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.” Iye anayankha kuti, “Ngati njombi zisanu ndi ziwiri za kumutu kwanga utazilukira mu cholukira nsalu ndi kuchimanga molimbika ndi chikhomo, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala wofanana ndi munthu wina aliyense.”
14 Kabayatan a nakaturog isuna, nangabel ni Delila kadagiti pito a linabag iti buokna iti tela ket inlansana iti pagabelan, ket kinunana kenkuana, “Samson! Umay dagiti Filisteo kenka.” Nagriing isuna ket pinarutna ti tela ken ti lansa manipud iti pagabelan.
Choncho iye akugona, Delila analukira njombi za ku mutu kwa Samsoni mu cholukira nsalu nachimanga molimba ndi chikhomo. Pambuyo pake anati kwa Samsoni, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Tsono iye anadzuka ku tulo, nazula chikhomo chija ndipo njombi zinachoka mu cholukira chija.
15 Kinunana kenkuana, “Kasano a kunam nga, 'Ay-ayatenka,' no saanmo met nga ibingay kaniak ti palimedmo? Rinabrabaknak iti mamintallo a daras ket saanmo nga imbagbaga no kasanoka a naaddaan iti kasta a pigsa.”
Tsono mkaziyo ananenanso kwa iye kuti, “Munganene bwanji kuti mumandikonda pamene mtima wanu suli pa ine? Aka ndi kachitatu mukundipusitsa ndipo simunandiwuze pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi.”
16 Inaldaw a rengrengenna ni Samson babaen iti saona, ken pilpilitenna iti kasta unay nga urayla tarigagayan ni Samson ti matay.
Tsono popeza anamupanikiza ndi mawu ake tsiku ndi tsiku ndi kumukakamiza, mtima wa Samsoni unatopa pafupi kufa.
17 Imbaga ngarud ni Samson kenkuana amin ket kinuna kenkuana, “Saanko pay a pulos a pinapukisan ti buok iti ulok, gapu ta maysaak a Nazireo a maipaay iti Apo manipud iti aanakan ti inak. No mapukisan ti ulok, ket panawannak ti pigsak, ket agbalinak a nakapsut ken kas iti sabali a tao.”
Choncho anamuwuza mkaziyo zonse za mu mtima mwake nati “Lumo silinapitepo pa mutu wanga chifukwa ndakhala ndili Mnaziri wopatulikira Mulungu chibadwire. Ngati nditametedwa mphamvu zanga zidzandichokera, ndidzasanduka wofowoka ndipo ndidzafanana ndi munthu wina aliyense.”
18 Idi nakita ni Delila nga imbagana kenkuana ti kinapudno maipapan iti amin a banag, nangibaon ken pinaayabanna dagiti mangiturturay kadagiti Filisteo, kunana, “Umaykayo manen gapu ta imbaganan kaniak ti amin a banag.” Ket immay kenkuana dagiti mangiturturay kadagiti Filisteo ket tugotda dagiti pirak kadagiti imada.
Delila ataona kuti wamuwuza zonse za mu mtima mwake anatumiza uthenga kukayitana akuluakulu a Afilisti nati, “Bweraninso kamodzi kano kokha popeza wandiwululira zonse za mu mtima mwake.” Choncho akuluakulu a Afilisti aja anabwera ndi ndalama za siliva mʼmanja mwawo.
19 Pinaturogna ni Samson iti saklotna. Nangayab isuna iti maysa a tao a mangpukis kadagiti pito a linabag iti buokna, ket rinugianna a parukmaen isuna gapu ta nagpukawen ti pigsana.
Mkazi uja anagoneka Samsoni pa miyendo yake. Kenaka anayitana munthu wina ndipo anadzameta Samsoni njombi zisanu ndi ziwiri zija kumutu kwake. Pamenepo anayamba kufowoka, ndipo mphamvu zake zinamuchokera.
20 Kinuna ni Delila, “Samson! Umay kenka dagiti Filisteo.” Nakariing isuna ket kinunana, “Makaruk-atakto a kasla iti dadduma a tiempo ket iwagsakkonto ti bagik.” Ngem saanna nga ammo a pinanawanen ni Yahweh isuna.
Pambuyo pake mkaziyo anamuyitana kuti, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Iye anadzuka kutuloko, naganiza kuti, “Ndituluka monga ndimachitira nthawi zonse ndi kudzimasula.” Koma sanadziwe kuti Yehova wamuchokera.
21 Tiniliw isuna dagiti Filisteo ket kinautda dagiti matana. Insalogda isuna idiay Gaza ket ginalutanda isuna babaen iti kawar a bronse. Pinatayyekna ti paggilingan a bato idiay pagbaludan.
Afilisti anamugwira ndipo anamukolowola maso. Kenaka anapita naye ku Gaza atamumanga ndi maunyolo achitsulo. Kumeneko anakhala wa pamphero mu ndende.
22 Ngem nangrugi manen nga umatiddog ti buokna kalpasan ti pannakapukisna.
Pambuyo pake tsitsi la pa mutu wake, monga linametedwa, linayambanso kumera.
23 Naguummong dagiti mangiturturay kadagiti Filisteo tapno mangidatonda iti dakkel a sakrifisio kenni Dagon a diosda, ken tapno agrag-oda. Gapu ta kinunada, “Pinarmek ti diostayo ni Samson, ti kabusortayo ket intedna iti imatayo.”
Tsono atsogoleri a Afilisti anasonkhana kuti adzapereke nsembe yayikulu kwa Dagoni mulungu wawo ndi kukondwerera popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu mʼmanja mwathu.”
24 Idi makita isuna dagiti tattao, dinaydayawda ti diosda, ta kinunada, “Pinarmek ti diostayo ti kabusortayo ken intedna isuna kadatayo—ti manangdadael iti pagiliantayo, a nangpatay iti adu kadatayo.”
Anthuwo atamuona Samsoni, anayamba kutamanda mulungu wawo popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka mdani wathu mʼmanja mwathu, ndiye amene anawononga dziko lathu, napha anthu athu ambirimbiri.”
25 Idi agramrambakda, kinunada, “Ayabanyo ni Samson, tapno pagkakatawaennatayo.” Pinaruarda ni Samson iti pagbaludan, ket pinagkatkatawana ida. Pinagtakderda isuna iti nagbaetan dagiti adigi.
Ali mʼkati mosangalala, anthu aja amafuwula kuti, “Mutulutseni Samsoniyo kuti adzatisangalatse.” Choncho anamutulutsadi Samsoni mʼndende, ndipo anawasangalatsadi. Ndipo anamuyimiritsa pakati pa mizati.
26 Kinuna ni Samson iti ubing a lalaki a nangkibin kenkuana, “Ipalubosmo a maarikapko dagiti adigi a nagsaadan ti pasdek tapno makasanggirak kadagitoy.”
Pambuyo pake Samsoni anawuza mnyamata amene anamugwira dzanja kuti, “Ndilole kuti ndikhudze mizati imene yachirikiza nyumba yonseyi kuti ndiyitsamire.”
27 Ita, napno ti balay kadagiti babbai ken lallaki. Adda idiay dagiti amin a mangiturturay kadagiti Filisteo. Adda iti ngato ti balay iti agarup tallo ribu a lallaki ken babbai, nga agbuybuya bayat a parparagsaken ida ni Samson.
Nthawi imeneyi nʼkuti nyumbayo ili yodzaza ndi anthu aamuna ndi aakazi. Olamulira onse a Afilisti anali momwemo, ndipo pamwamba pa nyumbayo panali anthu 3,000 aamuna ndi aakazi amene amaonerera Samsoni akusewera.
28 Immawag ni Samson kenni Yahweh ket kinunana, “O Apo Yahweh, lagipennak! Pangaasim ta papigsaennak iti maminsan laeng iti daytoy a kanito, O Dios, tapno makaibalesak a maminpinsan kadagiti Filisteo iti panangkautda kadagiti matak.”
Tsono Samsoni anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Ambuye anga, ndikumbukireni. Chonde ndilimbitseni nthawi yokha ino, inu Yehova, kuti ndiwabwezere Afilistiwa chifukwa cha maso anga awiri.”
29 Tiniritir ni Samson dagiti dua nga akin-tengnga nga adigi a nagsaadan ti pasdek, ken nagsanggir isuna kadagitoy, maysa nga adigi iti makannawan nga imana ken ti maysa pay iti kannigidna.
Choncho Samsoni anagwira mizati iwiri yapakati imene inkachirikiza nyumbayo. Anayitsamira ndi mphamvu zake zonse, dzanja lake lamanja ku mzati wina ndi dzanja lamanzere ku mzati winanso,
30 Kinuna ni Samson, “Bay-annak a matay a kadduak dagiti Filisteo!” Induronna iti amin a pigsana, ket narba ti pasdek ken naigabor daytoy kadagiti mangiturturay ken iti amin a tattao nga adda idiay. Isu a dagiti natay a napatayna idi matay isuna ket ad-adu ngem iti pinapatayna bayat iti panagbiagna.
ndipo Samsoni anati, “Ndife nawo pamodzi!” Nthawi yomweyo anakankha ndi mphamvu zake zonse ndipo mizati inagwera atsogoleri a Afilisti ndi anthu onse anali mʼmenemo. Tsono chiwerengero cha anthu amene Samsoni anapha pa nthawi ya imfa yake chinaposa cha iwo amene anawapha akanali ndi moyo.
31 Ket simmalog dagiti kakabsatna a lallaki ken amin nga adda iti balay ni amana, ket innalada isuna, ken insublida ket intanemda isuna iti nagbaetan ti Zora ken Estaol, iti lugar a nakaitaneman ni Manoa, nga amana. Nagbalin ni Samson nga ukom iti Israel bayat ti duapulo a tawen.
Kenaka abale ake ndi onse a pa banja la abambo ake anapita kukamutenga. Ndipo anakamuyika pakati pa Zora ndi Esitaoli mʼmanda a abambo ake, Manowa. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka makumi awiri.

< Uk-ukom 16 >